< Job 38 >

1 Alors l'Éternel répondit à Job du sein de la tempête, et dit:
Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
2 Qui est celui-ci qui obscurcit mes plans par des discours sans science?
“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
3 Ceins donc tes reins comme un vaillant homme, je t'interrogerai, et tu m'instruiras.
Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
4 Où étais-tu quand je jetais les fondations de la terre? Dis-le, si tu as de l'intelligence.
“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
5 Qui en a réglé les mesures, si tu le sais, ou qui a étendu le niveau sur elle?
Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
6 Sur quoi en a-t-on fait plonger les bases, ou qui en a posé la pierre angulaire,
Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
7 Quand les étoiles du matin poussaient ensemble des cris de joie, et les fils de Dieu, des acclamations?
pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
8 Et qui renferma la mer dans des portes, quand elle sortit en s'élançant du sein de la terre;
“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
9 Quand je lui donnai la nuée pour vêtement, et l'obscurité pour langes;
pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
10 Quand j'établis ma loi sur elle, quand je lui mis des verrous et des portes,
pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
11 Et que je lui dis: Tu viendras jusqu'ici, et tu n'iras pas plus loin; ici s'arrêtera l'orgueil de tes flots?
Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
12 Depuis que tu es au monde, as-tu commandé au matin, as-tu marqué à l'aurore sa place,
“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
13 Pour qu'elle saisisse les extrémités de la terre, et que les méchants soient chassés?
kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
14 La terre change de forme comme l'argile sous le cachet, et toutes choses se lèvent comme pour la vêtir.
Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
15 La lumière des méchants leur est ôtée, et le bras des menaçants est rompu.
Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
16 As-tu pénétré jusqu'aux sources de la mer, et t'es-tu promené au fond de l'abîme?
“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
17 Les portes de la mort se sont-elles découvertes à toi? Et as-tu vu les portes de l'ombre de la mort?
Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
18 As-tu compris l'étendue de la terre? Si tu sais tout cela, dis-le!
Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
19 Où est le chemin du séjour de la lumière? Et les ténèbres, où est leur demeure?
“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
20 Car tu peux les ramener à leur domaine, et tu connais les sentiers de leur maison!
Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
21 Tu le sais; car alors tu étais né, et le nombre de tes jours est grand!
Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
22 As-tu pénétré jusqu'aux trésors de neige? Et as-tu vu les trésors de grêle,
“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
23 Que je réserve pour les temps de détresse, pour le jour de la bataille et du combat?
zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
24 Par quels chemins se partage la lumière, et le vent d'orient se répand-il sur la terre?
Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
25 Qui a donné à l'averse ses canaux, et sa voie à l'éclair des tonnerres,
Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
26 Pour faire pleuvoir sur une terre sans habitants, sur un désert sans hommes,
kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
27 Pour abreuver des lieux déserts et désolés, et faire germer et sortir l'herbe?
kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
28 La pluie a-t-elle un père? Ou, qui enfante les gouttes de rosée?
Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
29 De quel sein est sortie la glace? Et qui enfante le givre du ciel?
Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
30 Les eaux se dissimulent, changées en pierre, et la surface de l'abîme se prend.
pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
31 Peux-tu resserrer les liens des Pléiades, ou détacher les chaînes d'Orion?
“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
32 Fais-tu sortir en leur temps les signes du zodiaque? Et conduis-tu la grande Ourse avec ses petits?
Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
33 Connais-tu les lois du ciel? Ou disposes-tu de son pouvoir sur la terre?
Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
34 Élèves-tu ta voix vers la nuée, pour que des eaux abondantes te couvrent?
“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
35 Envoies-tu les éclairs? Partent-ils, et te disent-ils: Nous voici?
Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
36 Qui a mis la sagesse dans les nues, qui a donné au météore l'intelligence?
Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
37 Qui compte les nuages avec sagesse, qui incline les outres des cieux,
Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
38 Quand la poussière se délaie et se met en fusion, et que les mottes s'agglomèrent?
pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
39 Chasses-tu pour le lion sa proie, et assouvis-tu la faim des lionceaux,
“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
40 Quand ils se tapissent dans leurs repaires, quand ils sont aux aguets dans les fourrés?
pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
41 Qui apprête la nourriture au corbeau, quand ses petits crient vers Dieu et volent çà et là, n'ayant rien à manger?
Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?

< Job 38 >