< Psaumes 9 >

1 Psaume de David, [donné] au maître chantre, [pour le chanter] sur Muth-Labben. Je célébrerai de tout mon cœur l'Eternel; je raconterai toutes tes merveilles.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
2 Je me réjouirai et je m'égayerai en toi; je psalmodierai ton Nom, ô Souverain!
Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
3 Parce que mes ennemis sont retournés en arrière; ils sont tombés, et ils ont péri de devant ta face.
Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
4 Car tu m'as fait droit et justice; tu t'es assis sur le trône, toi juste juge.
Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
5 Tu as réprimé fortement les nations, tu as fait périr le méchant, tu as effacé leur nom pour toujours, et à perpétuité.
Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
6 Ô ennemi! les désolations ont-elles pris fin? as-tu aussi rasé les villes pour jamais? leur mémoire est-elle périe avec elles?
Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
7 Mais l'Eternel sera assis éternellement; il a préparé son trône pour juger;
Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
8 Et il jugera le monde avec justice, [et] fera droit aux peuples avec équité.
Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
9 Et l'Eternel sera une haute retraite à celui qui sera foulé, il lui sera une haute retraite au temps qu'il sera dans l'angoisse.
Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
10 Et ceux qui connaissent ton Nom, s'assureront sur toi: car, ô Eternel! tu n'abandonnes point ceux qui te cherchent.
Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
11 Psalmodiez à l'Eternel qui habite en Sion; annoncez ses exploits parmi les peuples.
Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
12 Car il recherche les meurtres, [et] il s'en souvient; il n'oublie point le cri des débonnaires.
Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
13 Eternel! aie pitié de moi; regarde mon affliction causée par ceux qui me haïssent, toi qui me retires des portes de la mort.
Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
14 Afin que je raconte toutes tes louanges dans les portes de la fille de Sion. Je me réjouirai de la délivrance que tu m'auras donnée.
kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
15 Les nations ont été enfoncées dans la fosse qu'elles avaient faite; leur pied a été pris au filet qu'elles avaient caché.
Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
16 L'Eternel s'est fait connaître; il a fait jugement; le méchant est enlacé dans l'ouvrage de ses mains. (Higgajon, Sélah)
Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
17 Les méchants retourneront vers le sépulcre, toutes les nations, [dis-je], qui oublient Dieu. (Sheol h7585)
Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
18 Car le pauvre ne sera point oublié à jamais, [et] l'attente des affligés ne périra point à perpétuité.
Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
19 Lève-toi, ô Eternel! et que l'homme [mortel] ne se renforce point! que la vengeance soit faite des nations devant ta face!
Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
20 Eternel, remplis-les de frayeur; [et] que les nations sachent qu'elles ne sont que des hommes [mortels]. (Sélah)
Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)

< Psaumes 9 >