< Psaumes 11 >

1 Psaume de David, [donné] au maître chantre. Je me suis retiré vers l'Eternel; comment [donc] dites-vous à mon âme: Fuis-t'en en votre montagne, oiseau?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Yehova ine ndimathawiramo. Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti, “Thawira ku phiri lako ngati mbalame.
2 En effet, les méchants bandent l'arc, ils ont ajusté leur flèche sur la corde, pour tirer en secret contre ceux qui sont droits de cœur.
Pakuti taona oyipa akunga mauta awo; ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta, pobisala pawo kuti alase olungama mtima.
3 Puisque les fondements sont ruinés, que fera le juste?
Tsono ngati maziko awonongeka, olungama angachite chiyani?”
4 L'Eternel est au palais de sa Sainteté; l'Eternel a son Trône aux cieux; ses yeux contemplent, [et] ses paupières sondent les fils des hommes.
Yehova ali mʼNyumba yake yoyera; Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba. Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu; maso ake amawayesa.
5 L'Eternel sonde le juste et le méchant; et son âme hait celui qui aime la violence.
Yehova amayesa olungama, koma moyo wake umadana ndi oyipa, amene amakonda zachiwawa.
6 Il fera pleuvoir sur les méchants des filets, du feu, et du souffre; et un vent de tempête sera la portion de leur breuvage.
Iye adzakhuthulira pa oyipa makala amoto ndi sulufule woyaka; mphepo yotentha idzakhala yowayenera.
7 Car l'Eternel juste aime la justice, ses yeux contemplent l'homme droit.
Pakuti Yehova ndi wolungama, Iye amakonda chilungamo; ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.

< Psaumes 11 >