< Jérémie 6 >
1 Enfants de Benjamin, fuyez vous-en [par troupes] du milieu de Jérusalem, et sonnez du cor à Tékoah, et élevez un signal de feu à Bethkérem; car le mal et une grande ruine a paru de l'Aquilon.
“Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
2 J'avais rendu la fille de Sion semblable à une femme qui ne bouge point de la maison, et qui est délicate.
Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
3 Les pasteurs avec leurs troupeaux viendront contre elles, ils planteront leurs tentes autour d'elle, chacun paîtra en son quartier.
Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
4 Préparez le combat contre elle, levez-vous, et montons en plein midi. Malheur à nous, car le jour décline, et les ombres du soir s'accroissent.
Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
5 Levez-vous, montons de nuit, et ruinons ses palais.
Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
6 Car ainsi a dit l'Eternel des armées: coupez des arbres, et dressez des terrasses contre Jérusalem; c'est la ville qui doit être visitée, elle n'est tout entière que rapine au dedans.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
7 Comme le puits fait bouillonner ses eaux, ainsi elle fait bouillonner sa malice; on n'entend en elle devant moi continuellement que violence et que dégât, avec des maladies et des plaies.
Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
8 Jérusalem, reçois instruction, de peur que mon affection ne se retire de toi, et que je ne fasse de toi un désert, [et] une terre inhabitable.
Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
9 Ainsi a dit l'Eternel des armées: on grappillera entièrement comme une vigne les restes d'Israël; remets ta main dans les paniers comme un vendangeur.
Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
10 A qui parlerai-je, [et] qui sommerai-je, afin qu'ils écoutent? voici, leur oreille est incirconcise, et ils ne peuvent entendre; voici, la parole de l'Eternel leur est en opprobre, ils n'y prennent point de plaisir.
Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
11 C'est pourquoi je suis plein de la fureur de l'Eternel, et je suis las de la retenir, de sorte que je la répandrai sur les enfants par la rue, et sur l'assemblée des jeunes gens, même le mari sera pris avec la femme, et l'homme âgé avec celui qui est rassasié de jours.
Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
12 Et leurs maisons retourneront aux étrangers, les champs, et les femmes aussi; car j'étendrai ma main sur les habitants du pays, dit l'Eternel.
Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
13 Parce que depuis le plus petit d'entre eux jusques au plus grand, chacun s'adonne au gain déshonnête, tant le Prophète que le Sacrificateur, tous se portent faussement.
“Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
14 Et ils ont pansé la froissure de la fille de mon peuple à la légère, disant: paix, paix; et il n'y avait point de paix.
Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
15 Ont-ils été confus de ce qu'ils ont commis des abominations? Ils n'en ont même eu aucune honte, et ils ne savent ce que c'est que de rougir; c'est pourquoi ils tomberont sur ceux qui seront tombés, ils tomberont au temps que je les visiterai, a dit l'Eternel.
Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
16 Ainsi a dit l'Eternel: tenez-vous sur les chemins, et regardez, et vous enquérez touchant les sentiers des siècles passés, quel est le bon chemin, et marchez-y, et vous trouverez le repos de vos âmes; et ils ont répondu: nous n'[y] marcherons point.
Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
17 J'avais aussi établi sur vous des sentinelles [qui disent]: soyez attentifs au son de la trompette; mais on a répondu: nous n'[y] serons point attentifs.
Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
18 Vous donc, nations, écoutez, et toi Assemblée, connais ce qui est entre eux.
Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
19 Ecoute, terre: voici, je m'en vais faire venir un mal sur ce peuple, [savoir] le fruit de leurs pensées, parce qu'ils n'ont point été attentifs à mes paroles, et qu'ils ont rejeté ma Loi.
Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
20 Pourquoi m'offrir de l'encens venu de Seba, et le bon roseau aromatique du pays éloigné? vos holocaustes ne [me] plaisent point, et vos sacrifices ne me sont point agréables.
Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
21 C'est pourquoi ainsi a dit l'Eternel: voici, je m'en vais mettre en ce peuple des achoppements, auxquels les pères et les enfants, le voisin et son compagnon heurteront ensemble, et ils périront.
Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
22 Ainsi a dit l'Eternel: voici, un peuple vient du pays de l'Aquilon, et une grande nation se réveillera du fond de la terre.
Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
23 Ils prendront l'arc et l'étendard; ils [seront] cruels, et n'auront point de compassion; leur voix bruira comme la mer, et ils seront montés sur des chevaux, chacun d'eux est rangé en homme de guerre contre toi, fille de Sion!
Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
24 En aurons-nous ouï le bruit? nos mains [en] deviendront lâches; l'angoisse nous saisira, [et] un travail comme de celle qui enfante.
A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
25 Ne sortez point aux champs, et n'allez point par le chemin, car l'épée de l'ennemi [et] la frayeur est tout à l'entour.
Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
26 Fille de mon peuple, ceins-toi d'un sac, et te vautre dans la cendre; mène deuil [comme] sur un fils unique, et [fais] une lamentation très-amère, car le destructeur viendra subitement sur nous.
Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
27 Je t'ai établi [comme] une place forte et une forteresse au milieu de mon peuple, afin que tu connaisses et sondes leur voie.
“Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
28 Ils sont tous revêches, et plus que revêches, et ils vont médisant; ils sont [comme] de l'airain, et du fer; ils sont tous des gens qui se perdent l'un l'autre.
Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
29 Le soufflet est brûlé, le plomb est consumé par le feu, le fondeur a fondu en vain, car les mauvais n'ont point été séparés.
Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
30 On les appellera: Argent réprouvé; car l'Eternel les a réprouvés.
Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”