< Jérémie 5 >

1 Promenez-vous par les rues de Jérusalem, et regardez maintenant, et sachez, et vous enquérez par ses places, si vous y trouverez un homme de bien, s'il y a quelqu'un qui fasse ce qui est droit, et qui cherche la fidélité; et je pardonnerai à la [ville].
“Pitani uku ndi uku mʼmisewu ya Yerusalemu, mudzionere nokha, funafunani mʼmabwalo ake. Ngati mungapeze munthu mmodzi amene amachita zachilungamo ndi kufunafuna choonadi, ndipo ndidzakhululukira mzinda uno.
2 Que s'ils disent: l'Eternel est vivant; ils jurent en cela plus faussement.
Ngakhale anthu akulumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ komabe akungolumbira mwachinyengo.”
3 Eternel, tes yeux [ne regardent-ils pas] à la fidélité? Tu les as frappés, et ils n'en ont point senti de douleur; tu les as consumés, [et] ils ont refusé de recevoir instruction; ils ont endurci leurs faces plus qu'une roche, ils ont refusé de se convertir.
Inu Yehova, kodi suja mumafuna anthu onena zoona? Inu munawakantha anthuwo, koma sanamve kupweteka; munawaphwanya anthuwo, koma sanatengepo phunziro. Anawumitsa mitima yawo ngati mwala ndipo anakaniratu kulapa.
4 Et j'ai dit: certainement ce ne sont que les plus abjects, qui se sont montrés fous, parce qu'ils ne connaissent point la voie de l'Eternel, le droit de leur Dieu.
Ndiye ndinati, “Awa ndi amphawi chabe; anthu ochita zopusa. Sadziwa njira ya Yehova, sazindikira zimene Mulungu wawo amafuna.
5 Je m'en irai donc aux plus grands, et je leur parlerai; car ceux-là connaissent la voie de l'Eternel, le droit de leur Dieu; mais ceux-là mêmes ont aussi brisé le joug, [et] ont rompu les liens.
Tsono ndidzapita kwa atsogoleri ndi kukayankhula nawo; ndithu iwo amadziwa njira ya Yehova, amadziwa zomwe Mulungu wawo amafuna.” Koma ayi, iwonso anathyola goli la Yehova ndipo anadula msinga zawo.
6 C'est pourquoi le lion de la forêt les a tués, le loup du soir les a ravagés, [et] le léopard est au guet contre leurs villes; quiconque en sortira sera déchiré, car leurs péchés sont multipliés, [et] leurs rébellions sont renforcées.
Choncho mkango wochokera ku nkhalango udzawapha, mmbulu wochokera ku thengo udzawawononga, kambuku adzawabisalira pafupi ndi mizinda yawo kuti akhadzule aliyense amene adzayesera kutuluka mʼmizindamo pakuti kuwukira kwawo ndi kwakukulu ndipo abwerera mʼmbuyo kwambiri.
7 Comment te pardonnerai-je en cela? tes fils m'ont abandonné, et ils jurent par ceux qui ne sont point dieux; je les ai rassasiés, et ils ont commis adultère et sont allés en foule dans la maison de la prostituée.
Yehova akuti, “Kodi ndingakukhululukireni bwanji ndi zimene mwachita? Ana anu andisiya Ine ndipo amapembedza milungu imene si milungu konse. Ine ndinawapatsa zonse zimene ankasowa, komabe iwo anachita chigololo namasonkhana ku nyumba za akazi achiwerewere.
8 Ils sont comme des chevaux bien repus, quand ils se lèvent le matin, chacun hennit après la femme de son prochain.
Monga amachitira akavalo onenepa akamamemesa, aliyense wa iwo ankathamangira mkazi wa mnzake.
9 Ne punirais-je point ces choses-là, dit l'Eternel? et mon âme ne se vengerait-elle pas d'une nation qui est telle?
Tsono ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi?” akutero Yehova. “Kodi nʼkuleka kuwulipsira mtundu woterewu?
10 Montez sur ses murailles, et les rompez; mais ne les achevez pas entièrement; ôtez ses créneaux; car ils ne sont point à l'Eternel.
“Pitani ku minda yake ya mipesa ndi kukayiwononga, koma musakayiwononge kotheratu. Sadzani nthambi zake pakuti anthu amenewa si a Yehova.
11 Parce que la maison d'Israël et la maison de Juda se sont portées fort infidèlement contre moi, dit l'Eternel.
Nyumba ya Israeli ndi nyumba ya Yuda onse akhala osakhulupirika kotheratu kwa Ine.”
12 Ils ont démenti l'Eternel, et ont dit: cela n'arrivera pas, et le mal ne viendra pas sur nous, nous ne verrons pas l'épée ni la famine.
Iwowa ankanama ponena za Yehova kuti, “Yehova sangachite zimenezi! Choyipa sichidzatigwera; sitidzaona nkhondo kapena njala.
13 Et les Prophètes sont légers comme le vent, et la parole n'est point en eux; ainsi leur sera-t-il fait.
Mawu a aneneri azidzangopita ngati mphepo; ndipo mwa iwo mulibe uthenga wa Yehova. Choncho zimene amanena zidzawachitikira okha.”
14 C'est pourquoi, ainsi a dit l'Eternel, le Dieu des armées: parce que vous avez proféré cette parole-là, voici, je m'en vais mettre mes paroles en ta bouche pour y être comme un feu, et ce peuple sera comme le bois, et ce feu les consumera.
Chifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akuti, “Popeza kuti anthu awa ayankhula mawu amenewa, tsono mawu anga ndidzawasandutsa moto mʼkamwa mwako ndipo anthu awa ndidzawasandutsa nkhuni zimene moto udzapserezeretu.
15 Maison d'Israël, voici, je m'en vais faire venir contre vous une nation d'un pays éloigné, dit l'Eternel, une nation robuste, une nation ancienne, une nation de laquelle tu ne sauras point la Langue, et dont tu n'entendras point ce qu'elle dira.
Inu Aisraeli,” Yehova akuti, “Ndikukubweretserani mtundu wa anthu ochokera kutali, ndi mtundu umene sunagonjetsedwepo, mtundu wakalekale umene chiyankhulo chawo inu simuchidziwa, zimene akunena inu simungazimvetse.
16 Son carquois est comme un sépulcre ouvert, [et] ils sont tous vaillants.
Zida zawo za nkhondo zapha anthu ambirimbiri; onsewo ndi ankhondo amphamvu okhaokha.
17 Et elle mangera ta moisson et ton pain, que tes fils et tes filles doivent manger; elle mangera tes brebis, et tes bœufs; elle mangera [les fruits] de tes vignes, et de tes figuiers, et réduira à la pauvreté par l'épée tes villes fortes, sur lesquelles tu te confiais.
Adzakudyerani zokolola zanu ndi chakudya chanu, adzapha ana anu aamuna ndi aakazi; adzakupherani nkhosa zanu ndi ngʼombe zanu, adzawononga mpesa wanu ndi mikuyu yanu. Ndi malupanga awo adzagwetsa mizinda yanu yotetezedwa imene mumayidalira.
18 Toutefois en ces jours-là, dit l'Eternel, je ne vous achèverai pas entièrement.
“Komabe pa masiku amenewo sindidzakuwonongani kotheratu,” akutero Yehova.
19 Et il arrivera que vous direz: pourquoi l'Eternel notre Dieu nous a-t-il fait toutes ces choses? et tu leur diras ainsi: comme vous m'avez abandonné, [et] avez servi les dieux de l'étranger dans votre pays, ainsi serez-vous asservis aux étrangers en un pays qui n'est point à vous.
Ndipo pamene anthu adzafunsa Yehova kuti, “Chifukwa chiyani Yehova Mulungu wathu wachita zimenezi?” Iwe udzawawuze kuti, “Monga momwe mwasiyira Ine ndi kutumikira milungu yachilendo mʼdziko mwanu, momwemonso mudzatumikira anthu a mʼdzikonso lachilendo.”
20 Faites savoir ceci dans la maison de Jacob, et le publiez dans Juda, en disant:
“Lengeza izi kwa ana a Yakobo ndipo mulalikire kwa anthu a ku Yuda kuti,
21 Ecoutez maintenant ceci, peuple fou, et qui n'avez point d'intelligence, qui avez des yeux, et ne voyez point; et qui avez des oreilles, et n'entendez point.
Imvani izi, inu anthu opusa ndi opanda nzeru, inu amene maso muli nawo koma simupenya, amene makutu muli nawo koma simumva.
22 Ne me craindrez-vous point, dit l'Eternel, et ne serez-vous point épouvantés devant ma face? moi qui ai mis le sable pour la borne de la mer, par une ordonnance perpétuelle, et qui ne passera point; ses vagues s'émeuvent, mais elles ne seront pas les plus fortes; et elles bruient, mais elles ne la passeront point.
Kodi simuyenera kuchita nane mantha?” Akutero Yehova. “Kodi simuyenera kunjenjemera pamaso panga? Ine ndinayika mchenga kuti ukhale malire a nyanja, malire a muyaya amene nyanjayo singadutsepo. Mafunde angawombe motani, koma sangathe kupitirira malirewo; mafunde angakokome motani, koma sangadutse malirewo.
23 Mais ce peuple-ci a un cœur rétif et rebelle; ils se sont reculés en arrière, et s'en sont allés.
Koma anthu awa ndi nkhutukumve ndiponso a mitima yowukira; andifulatira ndipo andisiyiratu.
24 Et ils n'ont point dit en leur cœur: craignons maintenant l'Eternel notre Dieu, qui nous donne la pluie de la première et de la dernière saison, [et qui] nous garde les semaines ordonnées pour la moisson.
Sananenepo mʼmitima mwawo kuti, ‘Tiyeni tizipembedza Yehova Mulungu wathu. Kodi suja amatipatsa pa nthawi yake mvula yachizimalupsa ndi yamasika. Iye salephera konse kutipatsa nyengo ya kholola.’
25 Vos iniquités ont détourné ces choses, et vos péchés ont empêché qu'il ne vous arrivât du bien.
Koma zolakwa zanu zalepheretsa zonsezi; ndipo machimo anu akumanitsani zabwino.
26 Car il s'est trouvé dans mon peuple des méchants qui sont aux aguets, comme celui qui tend des pièges, ils posent une machine de perdition pour y prendre les hommes.
“Pakati pa anthu anga pali anthu ena oyipa amene amabisalira anzawo monga amachitira mlenje mbalame ndiponso ngati amene amatchera misampha kuti akole anthu anzawo.
27 Comme la cage est remplie d'oiseaux, ainsi leurs maisons [sont] remplies de fraude, et par ce moyen ils se sont agrandis et enrichis.
Nyumba zawo zadzaza ndi chuma chochipeza mwa chinyengo ngati zikwere zodzaza ndi mbalame. Nʼchifukwa chake asanduka otchuka ndi olemera.
28 Ils sont engraissés et parés; même ils ont surpassé les actions des méchants; ils ne font justice à personne, non pas même à l'orphelin, et ils prospèrent, et ne font point droit aux pauvres.
Ndipo ananenepa ndi kukhala ndi matupi osalala. Ntchito zawo zoyipa nʼzopanda malire; saweruza mwachilungamo nkhani ya ana amasiye kuti iyende bwino, sateteza ufulu wa anthu osauka.
29 Ne punirais-je point ces choses-là, dit l'Eternel? et mon âme ne se vengerait-elle pas d'une nation qui est telle?
Kodi Ine ndingaleke kuwalanga chifukwa cha zimenezi? Kodi ndisawulipsire mtundu woterewu? Akutero Yehova.
30 Il est arrivé en la terre une chose étonnante, et qui fait horreur:
“Chinthu chothetsa nzeru ndi choopsa kwambiri chachitika mʼdzikomo:
31 C'est que les Prophètes prophétisent le mensonge, et les Sacrificateurs dominent par leur moyen; et mon peuple a aimé cela. Que ferez-vous donc quand elle prendra fin?
Aneneri akunenera zabodza, ndipo ansembe akuvomerezana nawo, ndipo anthu anga akukonda zimenezi. Koma mudzatani potsiriza?

< Jérémie 5 >