< Psaumes 54 >

1 Jusqu'à la Fin, parmi les hymnes, instruction de David, Quand ceux de Ziph entrèrent, et dirent à Saül: N'as-tu pas vu où David est caché parmi nous? Dieu, sauve-moi par ton nom, et juge-moi par ta puissance!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.” Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu; onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
2 Dieu, écoute ma prière; sois attentif aux paroles de ma bouche!
Imvani pemphero langa, Inu Mulungu mvetserani mawu a pakamwa panga.
3 Car des étrangers se sont élevés contre moi, et des hommes puissants en veulent à ma vie; ils n'ont point eu le Seigneur devant les yeux. (Pause)
Alendo akundithira nkhondo; anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga, anthu amene salabadira za Mulungu.
4 Et voilà que Dieu me vient en aide, et le Seigneur est le sauveur de mon âme.
Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa; Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
5 Il fera retomber le mal sur ses ennemis; détruis-les dans ta vérité.
Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe; mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
6 Je te ferai un sacrifice volontaire; je rendrai grâces à ton nom, Seigneur parce que cela est bien.
Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu; ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova, pakuti ndi labwino.
7 Car c'est toi qui m'as délivré de toutes mes tribulations, et mon œil a regardé de haut tous mes ennemis.
Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse, ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.

< Psaumes 54 >