< Ézéchiel 27 >

1 Et la parole du Seigneur me vint, disant:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Et toi, fils de l'homme, chante sur Tyr une lamentation.
“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo.
3 Et dis à cette Tyr, qui réside à l'entrée de la mer, dis à ce marché des peuples venant d'une multitude d'îles: Ainsi parle le Seigneur à Tyr: Tu as dit: C'est de moi-même que je tiens ma beauté.
Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti, “Iwe Turo, umanena kuti, ‘Ndine wokongola kwambiri.’
4 Au cœur de la mer, tes fils t'ont revêtue de beauté pour te consacrer à Baal.
Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja; amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.
5 Le cèdre de Sénir a servi à construire tes vaisseaux; tes planches ont été prises en des poutres de cyprès du Liban, et pour faire tes mâts on a employé des sapins.
Anakupanga ndi matabwa a payini ochokera ku Seniri; anatenga mikungudza ya ku Lebanoni kupangira mlongoti wako.
6 On a fait tes rames de bois de Basan; on a fait en ivoire tes choses saintes, et tes chambres ombragées d'arbres en bois des Iles de Cétim.
Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani anapanga zopalasira zako; ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu. Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.
7 Le fin lin d'Égypte avec des broderies a formé ta couche; il en a été l'ornement; tu as été vêtue d'hyacinthe et de la pourpre des îles d'Élisa; c'était là ton manteau.
Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako, ndipo inakhala ngati mbendera. Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo zochokera ku zilumba za Elisa.
8 Et tes princes, ceux qui habitent Sidon, et ceux d'Arad, te servaient de rameurs; et tes sages, ô Tyr, ceux qui résidaient en toi, étaient là tes pilotes.
Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako. Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.
9 Les anciens de Biblos et leurs sages, ceux qui étaient en toi, ceux-là fortifiaient ton conseil. Et tous les navires de la mer, et tous leurs rameurs trafiquaient pour toi, jusqu'aux confins de l'Occident.
Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako, ngati okonza zibowo zako. Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.
10 Les Perses, les Lydiens, les Libyens étaient dans ton armée; tes hommes de guerre avaient suspendu chez toi leurs boucliers et leurs casques, pour servir à ta gloire.
“Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo. Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako, kubweretsa kwa iwe ulemerero.
11 Les fils d'Arad et ton armée étaient sur tes remparts; ils faisaient bonne garde sur tes tours; ils avaient suspendu leurs carquois autour de tes édifices; c'était l'achèvement de ta beauté.
Anthu a ku Arivadi ndi Heleki ankalondera mbali zonse za mpanda wako; anthu a ku Gamadi anali mu nsanja zako, Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse. Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.
12 Les Carthaginois, par leur trafic, t'apportaient une grande part de tes richesses; ils remplissaient ton marché d'argent, d'or, de fer, d'étain et de plomb.
“Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
13 La Grèce tout entière et ses colons entraient chez toi avec des âmes d'hommes, et ils apportaient sur ton marché des vases d'airain.
“Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
14 Ils t'amenaient des chevaux de Thogarma et des cavaliers.
“Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.
15 Les fils des Rhodiens trafiquaient avec toi; ils multipliaient sur ton marché ce qui provenait des îles; ils t'apportaient des dents d'éléphants; et à ceux qui entraient chez toi, tu donnais des marchandises en échange:
“Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.
16 Des esclaves pris dans la multitude de ceux que tu avais à vendre, de l'huile de myrrhe et des broderies de Tharsis; Rhamoth et Chorchor approvisionnaient aussi ton marché.
“Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.
17 Juda et les fils d'Israël trafiquaient avec toi; ils te vendaient du blé, des parfums et de la cannelle; ils t'apportaient le meilleur miel, de l'huile et de la résine pour tes marchands.
“Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.
18 Damas trafiquait avec toi; ils t'achetaient une part de la multitude de tes marchandises, du vin de Chelbon, des laines de Milet.
“Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari.
19 Et ils apportaient du vin sur ton marché. D'Asel venaient chez tes marchands du fer travaillé et des roues.
Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.
20 Dédan trafiquait avec toi; elle t'amenait des bêtes de somme, choisies pour les chars.
“Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.
21 L'Arabie et tous les princes de Cédar trafiquaient avec toi; ils venaient chez toi avec des chameaux, des agneaux et des béliers.
“Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
22 Les marchands de Saba et de Rhamma trafiquaient avec toi; ils apportaient à ton marché les épices les plus recherchées, des pierres précieuses et de l'or.
“Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.
23 Charrha et Chanaa trafiquaient avec toi; Assur et Charman trafiquaient avec toi.
“Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda.
24 Ils t'apportaient de l'hyacinthe et des ballots de marchandises précieuses, attachés avec des cordes, et des bois de cyprès
Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.
25 Pour en faire des navires. Ceux qui trafiquaient avec toi se mêlaient à la multitude de tes marchands, et tu étais remplie et pesamment chargée au cœur de la mer.
“Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali zonyamula malonda ako. Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi yodzaza ndi katundu wolemera.
26 Tes rameurs t'ont conduite dans les grandes eaux; et le souffle du midi t'a brisée au cœur de la mer.
Anthu opalasa ako amakupititsa pa nyanja yozama. Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola pakati pa nyanja.
27 Tes richesses, tes trésors, ceux de tes marchands; tes rameurs, tes pilotes, tes conseillers; ces hommes qui trafiquent avec toi, ces guerriers qui sont chez toi, toute la multitude rassemblée en toi, tomberont au cœur de la mer le jour de ta ruine.
Chuma chako, katundu wako, malonda ako, okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi, anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo adzamira mʼnyanja tsiku limene udzawonongeka.
28 Au cri de ta voix, tes pilotes seront frappés d'épouvante.
Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.
29 Tous tes rameurs, tous tes matelots descendront des navires; tous les pilotes de la mer resteront sur le rivage.
Onse amene amapalasa sitima zapamadzi, adzatuluka mʼsitima zawo; oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.
30 Et ils te plaindront à haute voix, et ils crieront amèrement, et ils mettront de la poussière sur leurs têtes, et ils se couvriront de cendre.
Iwo akufuwula, kukulira iwe kwambiri; akudzithira fumbi kumutu, ndi kudzigubuduza pa phulusa.
31 Et leurs fils feront sur toi une lamentation, une complainte sur Tyr, disant:
Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe ndipo akuvala ziguduli. Akukulira iweyo ndi mitima yowawa kwambiri.
32 Et leurs fils feront sur toi une lamentation, une complainte sur Tyr, disant:
Akuyimba nyimbo yokudandaulira nʼkumati: ‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo pakati pa nyanja?’
33 Quel profit as-tu retiré de la mer? Tu avais rempli de ton abondance toutes les nations; tu avais enrichi par ton trafic tous les rois de la terre.
Pamene malonda ako ankawoloka nyanja unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu. Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako komanso ndi malonda ako.
34 Maintenant tu es brisée dans la mer; tes trafiquants sont au fond de l'abîme, avec toute la multitude assemblée en toi.
Koma tsopano wathyokera mʼnyanja, pansi penipeni pa nyanja. Katundu wako ndi onse amene anali nawe amira pamodzi nawe.
35 Tous tes rameurs sont tombés; tous les habitants des îles se sont affligés sur toi; leurs rois ont été saisis de stupeur, et leur visage s'est couvert de larme.
Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja aopsedwa ndi zimene zakuchitikira. Mafumu awo akuchita mantha ndipo nkhope zangoti khululu.
36 Les marchands des nations t'ont sifflée; tu es perdue, et tu ne seras plus dans les siècles.
Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola. Watha mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”

< Ézéchiel 27 >