< Psaumes 45 >

1 Jusqu'à la Fin, avec chants alternés, une instruction des fils de Koré, un cantique au sujet du bien-aimé. Mon cœur a exhalé une bonne parole; je dédie mes œuvres au Roi. Ma langue est le roseau d'un scribe écrivant avec rapidité.
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
2 Tu es plus beau que les fils des hommes; la grâce est répandue sur tes lèvres. A cause de cela, Dieu t'a béni à jamais.
Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
3 Ceins l'épée qui s'appuie sur ta cuisse, ô Puissant!
Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
4 En ta jeunesse et en ta beauté, tends ton arc, marche et prospère, et règne par l'amour de la vérité, de la douceur et de la justice, et ta droite te guidera merveilleusement.
Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
5 Tes traits sont aiguisés, ô Puissant; ils renverseront les peuples; ils perceront le cœur des ennemis du Roi.
Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
6 Ton trône, ô mon Dieu, sera dans les siècles des siècles; ton sceptre de roi est le sceptre de la justice.
Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
7 Tu aimes la justice et tu hais l'iniquité; à cause de cela, ô Dieu, ton Dieu a fait de toi son Christ; il a répondu sur toi plus que sur tes compagnons l'huile de l'allégresse.
Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
8 La myrrhe, les essences et la casse s'exhalent de tes vêtements et de tes palais d'ivoire, et, réunies en ton honneur, elles te réjouissent,
Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
9 Les filles des rois. La reine s'est placée à ta droite, revêtue d'un manteau d'or diversement orné.
Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
10 Écoute, ma fille, et vois, et incline ton oreille; oublie ton peuple et la maison de ton père;
Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
11 Car le roi s'est épris de ta beauté, lui qui est ton seigneur:
Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
12 Et les filles de Tyr t'adoreront avec des présents; les riches du peuple de la terre prieront devant ta face.
Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
13 Toute sa gloire est comme celle de la fille du roi d'Esebon, revêtue d'une parure de franges d'or,
Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
14 Et diversement ornée. Les vierges de sa suite sont amenées au roi; ses compagnes te seront amenées.
Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
15 Elles te seront amenées avec joie et allégresse; elles seront conduites en la demeure du Roi.
Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
16 A la place de tes frères, des fils te sont nés; tu les institueras chefs de toute la terre.
Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
17 Ils se souviendront de ton nom de génération en génération; à cause de cela, les peuples te rendront grâces éternellement et dans les siècles des siècles.
Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.

< Psaumes 45 >