< Psaumes 129 >

1 En Jérusalem. Souvent ils m'ont attaqué dès ma jeunesse; que maintenant Israël dise:
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,” anene tsono Israeli;
2 Souvent ils m'ont attaqué dès ma jeunesse, et ils n'ont rien pu sur moi.
“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga, koma sanandipambane.
3 Les pécheurs ont frappé sur mon dos; ils ont prolongé leur iniquité.
Anthu otipula analima pa msana panga ndipo anapangapo mizere yayitali:
4 Le Seigneur en sa justice a brisé le cou des pécheurs.
Koma Yehova ndi wolungama; Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
5 Qu'ils soient confondus et mis en fuite, tous ceux qui haïssent Sion.
Onse amene amadana ndi Ziyoni abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
6 Qu'ils deviennent comme l'herbe des toits, qui sèche avant d'être arrachée,
Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba, umene umafota usanakule;
7 Et qui ne remplit ni la main du faucheur ni le sein du botteleur.
sungadzaze manja a owumweta kapena manja a omanga mitolo.
8 Sur eux les passants n'ont point dit: Que la bénédiction du Seigneur soit avec tous; nous vous bénissons au nom du Seigneur.
Odutsa pafupi asanene kuti, “Dalitso la Yehova lili pa inu; tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”

< Psaumes 129 >