< Proverbes 16 >

1
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 Toutes les œuvres de l'homme humble sont rendues manifestes auprès de Dieu, mais pour les impies, ils périssent en un jour fatal.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 Tout homme au cœur hautain est impur devant Dieu; celui qui, ayant une pensée injuste, met sa main dans la main d'autrui, ne sera pas innocent pour cela.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 Pratiquer la justice, c'est le commencement de la bonne voie, plus agréable à Dieu que le sacrifice des victimes.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Celui qui cherche le Seigneur trouvera la science et la justice; ceux qui Le cherchent avec droiture trouveront la paix.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 Toutes les œuvres du Seigneur sont selon la justice. L'impie est réservé pour un jour fatal.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 L'oracle est sur les lèvres du roi; sa bouche ne s'égarera pas dans le jugement.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 La justice du Seigneur tient la balance en équilibre; les œuvres de Dieu ont des poids justes.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 Celui qui fait le mal est en abomination au roi; car son trône repose sur la justice.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Les lèvres justes sont agréables au roi; il aime les paroles droites.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 La colère du roi est messagère de mort; un homme sage l'apaisera.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 Le fils du roi est dans la lumière de la vie; ses favoris sont comme un nuage d'arrière-saison.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 Les enfants de la sagesse sont préférables à l'or; les enfants de la prudence sont préférables à l'argent.
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 Les sentiers de la vie détournent du mal; les voies de la justice mènent à une longue vie. Celui qui accepte les corrections prospérera; celui qui se rend aux réprimandes deviendra sage. Celui qui est ferme dans ses voies garde son ami, et celui qui aime la vie sera sobre de paroles.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 Le regret vient après l'orgueil; la ruine, après la méchanceté.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 Mieux vaut avoir la douceur avec l'humilité, que partager les dépouilles avec les orgueilleux.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 Être intelligent en affaires, c'est trouver des biens; mettre sa confiance dans le Seigneur, c'est être bien heureux.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 On dit des intelligents et des sages, ce sont gens de peu; on parlera mieux des hommes aux paroles mielleuses.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 L'intelligence est pour ceux qui la possèdent une source de vie; les insensés n'ont que la science du mal.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 Le cœur du sage méditera tout ce que dira sa bouche, et sur ses lèvres il portera sa science.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Les bonnes paroles sont des rayons de miel; leur douceur est la guérison de l'âme.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 Il est des voies qui semblent droites à l'homme; mais leur extrémité lui fait voir dans le fond de l'enfer. (questioned)
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 L'homme, en ses labeurs, travaille pour lui-même, et, de vive force, il éloigne sa ruine. Le fourbe porte sa perte sur sa langue.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 L'imprudent creuse pour son malheur, et sur ses lèvres il amasse du feu.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 Le pervers répand le mal autour de lui, et le fourbe allume des tisons de malheur, et il sépare les amis.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 L'injuste caresse ses amis, et les mène en des voies qui ne sont pas bonnes.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 Celui qui, les yeux fixes, trame de mauvais desseins, recèle tout mal entre ses lèvres. C'est une fournaise de méchanceté.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 La vieillesse est une couronne de gloire; on la trouve dans les voies de la justice.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 Mieux vaut l'homme patient que le fort, et celui qui maîtrise sa colère que celui qui prend une ville.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 Tout mal vient du sein des injustes; et toute justice, du Seigneur.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

< Proverbes 16 >