< Néhémie 8 >

1 Et le septième mois arriva, et les fils d'Israël étaient dans leurs villes; et tout le peuple se rassembla, comme un seul homme, sur la place, devant la porte de l'Eau; et ils dirent à Esdras le scribe d'apporter le livre de la loi de Moïse que le Seigneur a intimée à Israël.
Anthu onse anasonkhana ngati munthu mmodzi pabwalo limene lili patsogolo pa Chipata cha Madzi. Iwo anawuza mlembi Ezara kuti abwere ndi buku la malamulo a Mose limene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
2 Et le premier jour du septième mois, Esdras, le prêtre, apporta la loi devant la multitude d'hommes et de femmes, et devant tous ceux qui pouvaient l'entendre.
Choncho pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri wansembe Ezara, anabwera ndi buku la malamulo ku msonkhano wa amuna, akazi ndi ana onse amene ankatha kumvetsa zinthu bwino.
3 Et il la lut depuis l'heure où le soleil éclaire jusqu'au milieu du jour, devant les hommes et les femmes, et ils la comprenaient, et les oreilles de tout le peuple étaient attentives au livre de la loi.
Choncho Ezara anawerenga bukulo atayangʼana bwalo la Chipata cha Madzi kuyambira mmawa mpaka masana pamaso pa amuna, akazi ndi onse amene ankamvetsa bwino zinthu. Ndipo anthu onse anatchera khutu kuti amve malamulowo.
4 Et Esdras, le scribe, se tenait sur une estrade de bois, et il y avait auprès de lui, à sa droite: Matthathias, Samaïas, Ananias, Urie, Helcias et Maasia; à sa gauche: Phadaïas, Misahel, Melchias, Asom, Asubadma, Zacharie et Mesollam.
Mlembi Ezara anayimirira pa nsanja ya mitengo imene anthu anamanga chifukwa cha msonkhanowu. Ku dzanja lake lamanja kunayimirira Matitiya, Sema, Anaya, Uriya, Hilikiya ndi Maaseya, ndipo kudzanja lake lamanzere kunali Pedaya, Misaeli, Malikiya, Hasumu, Hasibadana, Zekariya ndi Mesulamu.
5 Et Esdras ouvrit le livre à la vue de tout le peuple, car lui-même était plus élevé que le peuple, et lorsqu'il ouvrit le livre, tout le peuple resta debout.
Tsono Ezara anatsekula buku, akuona popeza anayima pa nsanja. Pamene anafutukula bukulo anthu onse anayimirira.
6 Et Esdras bénit le Seigneur, le Dieu très-grand, et le peuple élevant les mains, répondit: Amen. Et ils s'inclinèrent, et ils adorèrent le Seigneur la face contre terre.
Ezara anatamanda Yehova, Mulungu wamkulu, ndipo anthu onse anakweza manja awo ndi kuyankha kuti, “Ameni, ameni.” Pambuyo pake onse anaweramitsa pansi mitu yawo napembedza Yehova akanali chizolikire choncho.
7 Ensuite, Josué, Banaïas et Sarabias, expliquèrent la loi au peuple, et le peuple ne bougea pas de sa place.
Anthuwo atayimiriranso Alevi awa: Yesuwa, Bani, Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetayi, Hodiya, Maaseya, Kerita, Azariya, Yozabadi, Hanani ndi Pelaya anawathandiza kuti amvetse bwino malamulowo.
8 Et ils lurent dans le livre de la loi de Dieu; puis, Esdras enseigna, et il apprit au peuple à connaître le Seigneur, et le peuple comprit à la lecture.
Iwo anawerenga buku la malamulo a Mulungu momveka bwino ndi kutanthauzira mawuwo kuti anthu amvetse bwino zowerengedwazo.
9 Alors, Néhémias et Esdras, le scribe et prêtre, et les lévites qui expliquaient la loi au peuple, dirent à tout le peuple: Ce jour est consacré au Seigneur notre Dieu, ne vous affligez pas, ne pleurez point. Car tout le peuple pleurait quand il entendait les paroles de la loi.
Tsono bwanamkubwa Nehemiya pamodzi ndi wansembe ndi mlembi Ezara komanso Alevi amene amaphunzitsa anthu anati kwa anthu onse, “Lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Musakhale ndi chisoni ndipo musalire.” Anayankhula choncho popeza anthu onse ankalira atamva mawu a buku la malamulo lija.
10 Et Néhémias leur dit: Allez, mangez des chairs grasses, buvez de douces boissons, et envoyez des parts à ceux qui n'en ont point, car ce jour est consacré au Seigneur notre Dieu, et ne soyez point abattus, puisque le Seigneur est notre force.
Nehemiya anatinso, “Pitani, kachiteni phwando ku nyumba ndipo mukawagawireko ena amene alibe kanthu kalikonse popeza lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova. Musakhale ndi chisoni, pakuti chimwemwe cha Yehova ndiye mphamvu yanu.”
11 Et les lévites faisaient taire tout le peuple, disant: Gardez le silence, car ce jour est saint, et ne soyez point abattus.
Alevi anakhalitsa bata anthu onse powawuza kuti, “Khalani chete, pakuti lero ndi tsiku lopatulika ndipo musakhale ndi chisoni.”
12 Et tout le peuple s'en alla pour manger, boire, envoyer des parts et faire grande liesse, parce qu'il avait compris les paroles que Néhémias leur avait fait connaître.
Anthu onse anachoka kupita kukadya ndi kumwa. Chakudya china anatumiza kwa anzawo. Choncho panali chikondwerero chachikulu popeza tsopano anali atamvetsa bwino mawu a Mulungu amene anawawerengera ndi kuwafotokozerawo.
13 Et le second jour, les chefs de famille, tout le peuple, les prêtres et les lévites, se réunirent autour d'Esdras, le scribe, pour qu'il les instruisît sur toutes les paroles de la loi.
Mmawa mwake atsogoleri a mabanja pamodzi ndi ansembe ndi alevi anasonkhana kwa Ezara, mlembi wa malamulo kuti aphunzire mawu a malamulowo.
14 Et ils trouvèrent écrit en la loi que le Seigneur avait commandé à Moïse que les fils d'Israël demeurassent sous des tabernacles, durant la fête du septième mois,
Tsono anapeza kuti zinalembedwa mʼbuku la malamulo kuti Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti Aisraeli azikhala mʼzithando pa nthawi yonse ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
15 Et qu'ils le publiassent au son de la trompette en toutes leurs villes et à Jérusalem. Et Esdras dit: Allez sur la montagne, rapportez-en des rameaux d'olivier, de cyprès, de tamaris, de palmier et de tous les arbres touffus, pour faire des tabernacles selon ce qui est écrit.
Choncho analengeza ndi kufalitsa mʼmizinda yawo yonse ndi mu Yerusalemu kuti, “Pitani ku phiri mukadule nthambi za mtengo wa olivi, za mtengo wa olivi wa kutchire, za mtengo wa mchisu, za mtengo wa mgwalangwa ndiponso za mitengo ina ya masamba, zomangira zithando monga zalembedweramu ndi kubwera nazo.”
16 Et le peuple sortit, et il rapporta des rameaux, et ils se firent des tabernacles, chacun sur sa terrasse, ou dans sa cour, ou dans les parvis du temple du Seigneur, ou dans les rues de la ville jusqu'à la porte d'Ephraïm.
Choncho anthu anapita kukatenga nthambi ndipo aliyense anadzimangira misasa pa denga ya nyumba yake, mʼmabwalo awo, mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, mʼbwalo la pa Chipata cha Madzi ndiponso mʼbwalo la pa Chipata cha Efereimu.
17 Et toute l'Église, tous ceux qui étaient revenus de la captivité se firent des tabernacles, et ils demeurèrent sous des tabernacles; et depuis le temps de Josué, fils de Nau, jusqu'à ce jour-là, le peuple d'Israël n'avait pas fait ainsi, et grande fut sa joie.
Gulu lonse la anthu limene linabwera ku ukapolo linamanga misasa ndipo linakhala mʼmenemo. Kuyambira nthawi ya Yoswa mwana wa Nuni mpaka tsiku limenelo nʼkuti Aisraeli asanachitepo zimenezi. Choncho panali chimwemwe chachikulu.
18 Et on lut dans le livre de la loi, tous les jours, depuis le premier jusqu'au dernier, et ils firent la fête sept jours, et le huitième jour la fin de la fête, selon la loi.
Tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba mpaka lomaliza, Ezara ankawerenga buku la malamulo a Mulungu. Anthu anachita chikondwerero masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panachitika msonkhano potsata buku la malamulo lija.

< Néhémie 8 >