< Josué 3 >

1 Et Josué fut debout de grand matin, et il leva le camp de Sétim. Ils marchèrent jusqu'au Jourdain; et là ils firent halte avant de le traverser.
Yoswa ndi Aisraeli onse anadzuka mmamawa nanyamuka ku Sitimu kupita ku Yorodani. Iwo anagona kumeneko asanawoloke mtsinje wa Yorodaniwo.
2 Après trois jours, les scribes parcoururent le camp.
Patatha masiku atatu, atsogoleri anayendera misasa yonse,
3 Ils donnèrent au peuple les ordres de Josué, et dirent: Lorsque vous verrez l'arche de l'alliance du Seigneur notre Dieu, et nos prêtres et nos lévites la portant, quittez chacun votre poste et marchez à sa suite.
kulangiza anthu kuti, “Mukaona ansembe a Chilevi atanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu, inu munyamuke pa malo ano ndi kumalitsatira.
4 Mais laissez un grand intervalle entre vous et elle, tenez-vous à une distance de deux mille coudées; gardez-vous d'en approcher, afin que vous sachiez la voie que vous devez suivre, car vous n'avez jamais fait semblable chemin.
Potero mudzadziwa njira yoti mudzere, popeza simunayendepo njira ino nʼkale lomwe. Koma musaliyandikire. Pakati pa inu ndi bokosilo pakhale mtunda pafupifupi kilomita imodzi.”
5 Et Josué dit au peuple: Sanctifiez-vous pour demain, car demain le Seigneur fera au milieu de vous des merveilles.
Yoswa anawuza anthu kuti, “Dzipatuleni tsono pakuti mawa Yehova adzachita zodabwitsa pakati panu.”
6 Et Josué dit aux prêtres: Enlevez l'arche de l'alliance du Seigneur et marchez devant le peuple. Les prêtres enlevèrent donc l'arche de l'alliance du Seigneur, et ils marchèrent devant le peuple.
Mmawa mwake Yoswa ananena kwa ansembe kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano muwoloke ndipo mukhale patsogolo pa anthu.” Motero iwo analinyamula ndi kupita patsogolo pawo.
7 Et le Seigneur dit à Josué: C'est aujourd'hui que je commence à te rehausser aux yeux de tous les fils d'Israël, afin qu'ils sachent que de même que j'étais avec Moïse, je serai avec toi.
Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Lero Ine ndidzayamba kukukweza pamaso pa Aisraeli onse kuti adziwe kuti ndili nawe monga ndinalili ndi Mose.
8 Et maintenant, donne mes ordres aux prêtres qui portent l'arche de l'alliance; dis-leur: Lorsque vous serez entrés dans les eaux du Jourdain, arrêtez-vous.
Ansembe amene akunyamula Bokosi la Chipangano uwalamule kuti, ‘Mukafika ku mtsinje wa Yorodani mulowe mu mtsinjemo ndi kuyima mʼmphepete.’”
9 Et Josué dit aux fils d'Israël: Venez ici, écoutez les paroles du Seigneur votre Dieu.
Yoswa anati kwa Aisraeli, “Bwerani pano mudzamve mawu a Yehova Mulungu wanu.
10 Vous reconnaîtrez en elles, et en leur accomplissement, que le Dieu vivant est parmi vous, et qu'il exterminera devant votre face le Chananéen, l'Hettéen, l'Hevéen, le Phérézéen, le Gergéséen, le Jébuséen et l'Amorrhéen.
Umu ndi mmene mudzadziwira kuti Mulungu wamoyo ali pakati panu. Inu mukamadzapita patsogolo Iye adzathamangitsa Akanaani, Ahiti, Ahivi, Aperezi, Agirigasi, Aamori ndi Ayebusi.
11 Voilà que l'arche de l'alliance du Seigneur de toute la terre va traverser le Jourdain.
Pamenepo, Bokosi la Chipangano la Mbuye wa dziko lonse lapansi lidzawoloka mu Yorodani patsogolo panu.
12 Choisissez douze hommes des fils d'Israël, un de chaque tribu.
Musankhe amuna khumi ndi awiri kuchokera ku fuko lililonse la Israeli.
13 Et ceci arrivera: Lorsque les pieds des prêtres portant l'arche de l'alliance du Seigneur de toute la terre s'arrêteront dans l'eau du Jourdain, l'eau inférieure s'écoulera et les eaux supérieures s'arrêteront.
Mapazi a ansembe onyamula Bokosi la Yehova, Mbuye wa dziko lapansi, akadzangoponda mu Yorodani, madzi ake onse ochokera ku mtunda adzaleka kuyenda ndipo adzayima ngati chipupa.”
14 Et le peuple s'éloigna de ses tentes pour traverser le Jourdain; cependant, les prêtres transportèrent, en avant du peuple, l'arche de l'alliance du Seigneur.
Tsono Aisraeli anachoka ku misasa yawo kukawoloka mtsinje wa Yorodani. Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano ndiwo anatsogolera anthuwo.
15 Mais, au moment où entraient dans le Jourdain les prêtres portant l'arche de l'alliance du Seigneur, au moment où leurs pieds commencèrent à être baignés dans l'eau du fleuve du Jourdain, coulant à pleins bords, puisque c'était le temps de la moisson des froments,
Nyengo imeneyi inali yokolola ndipo mtsinje wa Yorodani umakhala wodzaza. Komabe, ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anafika ku Yorodani, ndipo atangoponda mʼmadzimo,
16 Les eaux supérieures s'arrêtèrent; elles s'arrêtèrent formant une masse compacte et immense, qui s'étendit bien loin, bien loin, jusqu'à Cariathiarim. L'eau qui descendait, s'écoula dans la mer d'Araba ou la mer de Sel, jusqu'à ce qu'il n'en restât plus, et le peuple s'arrêta devant Jéricho.
madzi ochokera ku mtunda anasiya kuyenda. Madzi a Yorodani ochokera ku mtunda anawunjikana pamodzi ngati khoma lalitali pa mtunda wautali ndithu ndi mzinda wa Adama chapafupi ndi mzinda wa Zaretani. Madzi othamangira ku nyanja ya Araba, ngakhalenso amene amachokera kuti Nyanja ya Mchere amathera pamenepo. Choncho anthu anawoloka tsidya lina moyangʼanana ndi Yeriko.
17 Et, pendant que tous les fils d'Israël traversaient à pied sec, les prêtres, qui portaient l'arche de l'alliance du Seigneur, se tinrent immobiles et à pied sec au milieu du fleuve, jusqu'à ce que tout le peuple en eut achevé le passage.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anali chiyimire powuma, pakati pa Yorodani pamene Aisraeli amawoloka mpaka gulu lonse linamaliza kuwoloka powuma.

< Josué 3 >