< Job 28 >

1 Il y a des contrées où naît l'argent, d'autres où l'on épure l'or.
Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
2 Le fer se tire du sol, et l'airain, semblable à de la pierre, est extrait des mines.
Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
3 Le Seigneur a réglé les ténèbres; il maintient ponctuellement les limites qu'il a tracées; la roche sombre se distingue de l'ombre de la mort,
Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
4 Le lit du torrent d'un amas de poussière; ceux qui abandonnent leur chemin s'affaiblissent, ils sont rejetés du reste des mortels.
Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
5 Le fond du sol d'où sortira le pain a été tourmenté comme du feu.
Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
6 Parmi ses pierres on trouve le saphir, et il y a là aussi des amas d'or.
miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
7 Le sentier? L'oiseau ne l'a pas connu; l'œil du vautour ne s'y est point arrêté.
Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
8 Les fils des vaniteux n'y ont point porté leurs pas; le lion n'a point passé auprès.
Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
9 L'homme a étendu sa main jusqu'à la cime des monts, il a ouvert leurs racines.
Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
10 Il a fendu le tourbillon des fleuves, et mon œil a vu ce qu'il y a de précieux.
Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
11 L'homme a exploré le fond des rivières, et il a mis au jour sa puissance.
Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
12 Mais la sagesse, où est-elle trouvée? où la science réside-t-elle?
“Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
13 L'homme n'en sait pas le chemin, nul des mortels ne l'a découvert.
Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
14 L'abîme dit: Elle n'est point en moi; la mer a dit: Elle n'est pas avec moi.
Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
15 On ne l'obtient pas au prix de trésors; elle ne s'échange pas contre de l'argent.
Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
16 On ne la mettra point dans la balance avec de l'or d'Ophir, des saphirs et des onyx.
Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
17 Ni l'or ni le cristal ne la vaudront; on ne lui égalera pas des vases d'or.
Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
18 On oubliera éclat et grandeurs; place la sagesse au-dessus de ce qu'il y a de plus intime.
Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
19 On ne lui comparera pas la topaze de l'Ethiopie; on ne la pèsera pas avec de l'or pur.
Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
20 Où la sagesse a-t-elle été trouvée? En quel lieu est l'intelligence?
“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
21 Elle a échappé aux recherches de tous les hommes; elle est cachée pour les oiseaux du ciel.
Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
22 La perdition et la mort ont dit: Nous avons entendu parler de sa gloire.
Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
23 Dieu seul a tracé sa voie; seul il sait où elle est.
Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
24 Seul il voit tout sous le ciel; il connaît tout sur la terre.
pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
25 Il voit et il connaît ce qu'il a créé: la force des vents et la mesure des eaux.
Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
26 Aux jours de la création, après avoir tout considéré, il a tout réglé jusqu'aux ébranlements du tonnerre.
atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
27 Alors il a vu la sagesse et il lui a montré le chemin; il l'a préparée et observée avec attention.
pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
28 Et il a dit à l'homme: Ecoute, la sagesse c'est la piété; la science c'est s'abstenir du mal.
Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”

< Job 28 >