< Jérémie 8 >

1 En ce temps-là, dit le Seigneur, on retirera de leurs sépulcres les os des rois de Juda, les os de ses princes, les os des prêtres, les os des prophètes, et les os des habitants de Jérusalem.
Yehova akuti, “‘Pa nthawi imeneyo, mafupa a mafumu ndi a akuluakulu a ku Yuda, mafupa a ansembe ndi a aneneri, ndiponso mafupa a anthu a ku Yerusalemu adzafukulidwa.
2 Et on les étalera pour qu'ils sèchent aux rayons du soleil, de la lune, de toutes les étoiles, et de toute l'armée céleste que ces hommes avaient aimés, qu'ils avaient servis, après lesquels ils avaient couru, auxquels ils s'étaient attachés et qu'ils avaient adorés. Et ces hommes, on ne pleurera plus sur eux, ils ne seront pas ensevelis et ils seront en exemple sur la face de la terre;
Adzawamwaza pa nthaka kuyangʼana dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zonse zamlengalenga, zimene ankazikonda, kuzitumikira ndi kuzitsatira, kupemphako nzeru ndiponso kuzilambira. Mafupawo sadzawasonkhanitsa kapena kuwakwirira, koma adzakhala ngati ndowe pamwamba pa nthaka.
3 Parce qu'ils ont préféré la mort à la vie, et ceux qui seront restés de cette race, en quelque lieu que ce soit, je les expulserai.
Otsala onse a mtundu woyipawu adzafuna imfa kopambana moyo kulikonse kumene ndidzawapirikitsirako, akutero Yehova Wamphamvuzonse.’”
4 Car voici ce que dit le Seigneur: Celui qui tombe ne se relève-t-il pas, et celui qui s'est détourné du chemin n'y revient-il pas?
“Tsono awuze anthuwa, ‘Yehova akuti: “‘Kodi anthu akagwa sangadzukenso? Munthu akasochera kodi sangathe kubwereranso?
5 Pourquoi donc mon peuple a-t-il dévié sans pudeur? pourquoi s'est-il opiniâtré dans son mauvais choix, et a-t-il refusé de se convertir?
Chifukwa chiyani nanga anthu awa akupitirirabe kuchimwa, osabwerera? Chifukwa chiyani Yerusalemu akubwerera mʼmbuyo? Iwo akangamira chinyengo; akukana kubwerera.
6 Maintenant prêtez l'oreille et écoutez: Nul ne se repent de sa méchanceté; en est-il qui diront: Qu'ai-je fait? Ils courent jusqu'à tomber dans leur course, comme un cheval trempé de sueur qui ne peut plus hennir.
Ine ndinatchera khutu kumvetsera koma iwo sanayankhulepo zoona. Palibe woyipa amene analapapo zoyipa zake, nʼkumati, ‘Ine ndachita chiyani?’ Aliyense akutsatira njira yake ngati kavalo wothamangira nkhondo.
7 La grue dans le ciel connaît sa saison; la tourterelle, l'hirondelle des champs et le passereau observent le moment où ils couvent; mais mon peuple n'a pas connu les jugements du Seigneur.
Mbalame yotchedwa kakowa ija imadziwa nthawi yake mlengalenga. Koma nkhunda, namzeze ndi chingalu zimadziwa nthawi yonyamukira ulendo, koma anthu anga sadziwa malamulo a Yehova.
8 Comment direz-vous: Nous sommes sages, et la loi du Seigneur est avec nous? La plume menteuse de vos scribes écrit des erreurs;
“‘Inu mukunena bwanji kuti, ‘Ndife anzeru ndipo timasunga malamulo a Yehova?’ Koma ndi alembi anu amene akulemba zabodza.
9 Vos sages ont été confondus, et ils ont tremblé, et ils ont été pris, parce qu'ils ont rejeté la loi du Seigneur; quelle sagesse y a-t-il donc en eux?
Anthu anzeru achita manyazi; athedwa nzeru ndipo agwidwa. Iwo anakana mawu a Yehova. Nanga tsono nzeru zawo ziwapinduliranji?
10 A cause de cela, je donnerai leurs femmes à d'autres, et leurs champs à des héritiers étrangers,
Nʼchifukwa chake akazi awo ndidzawapereka kwa amuna ena ndipo minda yawo ndidzayipereka kwa amene adzawagonjetse. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi khalidwe lofuna kupeza chuma mwakuba. Aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
11 Qui en recueilleront les fruits, dit le Seigneur; il n'y aura pas de raisins dans leurs vignes, pas de figues sur leurs figuiers, et les feuilles en tomberont.
Iwo amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba chabe nʼkumati, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
12 Qui en recueilleront les fruits, dit le Seigneur; il n'y aura pas de raisins dans leurs vignes, pas de figues sur leurs figuiers, et les feuilles en tomberont.
Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazi? Ayi, alibe manyazi ndi pangʼono pomwe; iwo sadziwa nʼkugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalanga, akutero Yehova.
13 Qui en recueilleront les fruits, dit le Seigneur; il n'y aura pas de raisins dans leurs vignes, pas de figues sur leurs figuiers, et les feuilles en tomberont.
“‘Ndidzatenga zokolola zawo, Sipadzakhalanso mphesa pa mpesa kapena nkhuyu pa mkuyu, ndipo masamba ake adzawuma. Zinthu zimene ndinawapatsa ndidzawachotsera.’”
14 Pourquoi demeurons-nous en repos? Rassemblons-nous, et retirons-nous dans nos places fortes, et là soyons comme des rebuts, puisque le Seigneur nous a rejetés, et qu'il nous a abreuvés d'eau mêlée de fiel en punition de nos péchés envers lui.
Koma amati, “Tikukhala pano chifukwa chiyani? Tiyeni tonse pamodzi tithawire ku mizinda yotetezedwa ndi kukafera kumeneko. Pakuti Yehova Mulungu wathu watsimikiza kuti tiyenera kufa. Watipatsa madzi aululu kuti timwe, chifukwa tamuchimwira.
15 Nous nous attendions à la paix, et il ne nous est venu rien de bon; à la guérison, et voilà que c'était la souffrance.
Tinkayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chinachitika, tinkayembekezera kuchira koma tinakumana ndi zoopsa zokhazokha.
16 De Dan nous entendons le bruit de leur cavalerie rapide; toute la terre a tremblé au bruit des hennissements de ses chevaux; elle viendra, elle dévorera la terre et ses richesses, la ville et ses habitants;
Kulira kwa ngʼombe zazimuna za mdani kukumveka kuchokera ku Dani; dziko lonse likunjenjemera chifukwa cha kulira kwa akavalowo. Akubwera kudzawononga dziko ndi zonse zimene zili mʼmenemo. Adzawononga mzinda ndi onse okhalamo.”
17 Car voilà que je vous envoie des serpents mortels contre lesquels il n'est point de charmes, et ils vous mordront,
Yehova akuti, “Onani, ndikukutumizirani njoka zaululu, mphiri zimene munthu sangathe kuzilodza, ndipo zidzakulumani,”
18 Sans qu'il y ait de remède, et vous aurez en outre les douleurs de vos cœurs défaillants.
Ndadzazidwa ndi chisoni kwambiri, mtima wanga walefukiratu.
19 J'entends les cris que jette, en une terre lointaine, la fille de mon peuple: Est-ce que le Seigneur n'est pas à Sion? est-ce qu'en Sion il n'y a plus de roi? Non, parce qu'ils m'ont exaspéré avec leurs idoles et leurs dieux étrangers.
Imvani kulira kwa anthu anga kuchokera ku dziko lakutali: akuti, “Kodi Yehova sali ku Ziyoni? Kodi mfumu yake sili kumeneko?” “Chifukwa chiyani akundiputa ndi mafano awo osema, ndi milungu yawo yachilendo?”
20 L'été est passé, la moisson est finie, et nous ne sommes point sauvés.
“Nthawi yokolola yapita, chilimwe chapita, koma sitinapulumuke.”
21 En mon angoisse, j'ai pris des vêtements de deuil en voyant l'affliction de la fille de mon peuple; j'ai été accablé de douleurs telles que celles de l'enfantement.
Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa; ndikungolira ndipo mantha aakulu andigwira.
22 N'y a-t-il plus de baume en Galaad? n'y a-t-il plus de médecin? D'où vient que la fille de mon peuple n'est point encore guérie?
Kodi ku Giliyadi kulibe mankhwala ochiritsa? Kodi kumeneko kulibe singʼanga? Nanga chifukwa chiyani mabala a anthu anga sanapole?

< Jérémie 8 >