< Jérémie 7 >

1 Écoutez tous la parole du Seigneur, peuples de la Judée;
Mawu amene Yehova anayankhula kwa Yeremiya ndi awa,
2 Écoutez tous la parole du Seigneur, peuples de la Judée;
“Ima pa chipata cha Nyumba ya Yehova ndipo kumeneko ukalalikire uthenga uwu: “‘Imvani mawu a Yehova, inu nonse anthu a ku Yuda amene mumalowa pa chipata ichi kudzapembedza Yehova.
3 Voici ce que dit le Seigneur Dieu d'Israël Redressez vos voies et vos pensées, et j'habiterai avec vous en ce lieu.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Konzani makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndipo ndidzakulolani kukhala pa malo ano.
4 Ne mettez pas votre confiance en vous-mêmes, ni en des paroles de mensonge; car il ne vous servira nullement de dire: Le temple du Seigneur, le temple du Seigneur est ici.
Musamakhulupirire mawu anu achinyengo onena kuti, ‘Ino ndi Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova, Nyumba ya Yehova!’
5 Car si vous redressez vos voies et vos actions, si vous rendez la justice entre un homme et son prochain;
Ngati mutasinthadi makhalidwe anu ndi zochita zanu, ndi kumachitirana zolungama,
6 Si vous n'opprimez pas l'étranger, ni l'orphelin, ni la veuve; si vous ne versez pas le sang innocent dans ce lieu; si vous ne courez pas, pour votre malheur, après des dieux étrangers,
ngati mutaleka kuzunza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye ndi kuleka kupha anthu osalakwa pa malo ano, ndipo ngati muleka kutsatira milungu ina, kuti ingakuwonongeni,
7 J'habiterai ce lieu avec vous, en la terre que j'ai donnée, de siècle en siècle, à vos pères.
Ine ndidzakulolani kukhala pa malo ano, mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu mpaka muyaya.
8 Mais si vous mettez votre confiance en des paroles de mensonge, dont vous ne retirerez aucun secours;
Koma onani, inu mukudalira mawu abodza amene alibe phindu.
9 Si vous tuez, si vous commettez des adultères, si vous volez, si vous jurez faussement, si vous brûlez de l'encens à Baal, et si vous courez, pour votre malheur, après des dieux étrangers qui vous étaient inconnus;
“Kodi inu muziba ndi kupha, kuchita chigololo ndi kulumbira monama, kufukiza lubani kwa Baala ndi kutsatira milungu ina imene simunayidziwe,
10 Et après cela, si vous venez, si vous vous placez devant moi en cette maison où mon nom a été invoqué, disant: Nous nous sommes abstenus de commettre ces abominations,
ndipo kenaka nʼkubwera kudzayima pamaso panga mʼNyumba ino, Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langa, inu nʼkumati, ‘Tapulumuka.’ Mwapulumuka kuti muzichitabe zonyansazi?
11 Moi je vous dirai: Est-ce une caverne de voleurs, ma maison où mon nom a été invoqué devant vous? Je vous ai vus, dit le Seigneur.
Kodi Nyumba ino imene imadziwika ndi Dzina langa, yasanduka phanga la anthu olanda zinthu anzawo mwachifwamba inu mukuona? Komatu ndakhala ndi kuziona zonsezi! akutero Yehova.”
12 Allez en ce lieu qui m'appartient, à Silo, où d'abord j'avais abrité mon nom; et voyez comment je l'ai traité, à la vue de la méchanceté de mon peuple Israël.
“‘Pitani tsopano ku malo anga ku Silo, malo amene poyamba ankadziwika ndi Dzina langa, ndipo mukaone zimene ndinachita kumeneko chifukwa cha kuyipa kwa anthu anga Aisraeli.
13 Et maintenant parce que vous avez fait toutes ces œuvres, parce que je vous ai parlé, et que vous ne m'avez pas écouté; parce que je vous ai appelés et que vous ne m'avez pas répondu,
Tsono popeza munkachita zonsezi, ngakhale Ine kukuyankhulani koma inu osamvera, kukuyitanani koma inu osayankha,
14 Je traiterai cette maison où mon nom a été invoqué, et en qui vous mettiez votre confiance, je traiterai cette terre que j'ai donnée à vos pères et à vous, comme j'ai traité Silo.
choncho ndidzachita pa Nyumba imene imadziwika ndi Dzina langayi, Nyumba ya Yehova imene mumayidalira, malo amene ndinapereka kwa inu ndi makolo anu, zomwe ndinachita ku Silo.
15 Et je vous rejetterai loin de ma face, comme j'ai rejeté vos frères, toute la race d'Éphraïm.
Ndidzakuthamangitsani pamaso panga, ngati momwe ndinachitira abale anu onse, anthu a Efereimu.’”
16 Et toi, garde-toi de prier pour ce peuple; ne demande pas que je lui fasse miséricorde; ne prie pas et ne viens pas à moi pour eux, car je ne t'exaucerai point.
“Choncho iwe Yeremiya usawapempherere anthu awa ngakhale kuwapepesera kapenanso kuwapembedzera; usandidandaulire, chifukwa Ine sindidzakumvera.
17 Ne vois-tu pas ce qu'ils font dans les villes de Juda et dans les rues de Jérusalem?
Kodi sukuona zimene akuchita mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu?
18 Leurs fils amassent le bois, et les pères allument le feu, et leurs femmes pétrissent la pâte pour offrir des gâteaux à la reine du ciel, et ils répandent des libations pour des dieux étrangers, afin de provoquer ma colère.
Ana akutorera nkhuni, abambo akusonkha moto, ndipo amayi akukanda ufa kuti aphike makeke oti akapereke nsembe kwa mfumukazi yazakumwamba. Iwo amathira nsembe ya zakumwa kwa milungu ina kuti andipsetse mtima.
19 Est-ce moi qu'ils provoquent ainsi? dit le Seigneur. N'est-ce pas eux- mêmes, pour que leur front soit couvert de honte?
Koma kodi akuvutitsa Ine? Kodi sakungodzivuta okha, ndi kudzichititsa manyazi? akutero Yehova.”
20 Et c'est pourquoi le Seigneur a dit: Voilà que ma vengeance et ma colère vont fondre sur ce lieu et sur les hommes, et sur le bétail, et sur tous les arbres de leurs champs, et sur les fruits de la terre; ma colère brûlera et ne s'éteindra point.
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Ndidzatsanulira mkwiyo wanga pa Nyumba yangayi, anthu, nyama, mitengo ndi zipatso zomwe. Mkwiyowo udzakhala ngati moto wosazimitsika.
21 Voici ce que dit le Seigneur: Multipliez vos holocaustes et vos victimes, et mangez-en les chairs:
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Wonjezerani nsembe zanu zopsereza pa nsembe zanu zinazo ndipo mudye nyama yakeyo!
22 Parce que je n'ai point parlé à vos pères, et que je ne leur ai rien prescrit, le jour où je les ai ramenés de la terre d'Égypte, concernant les holocaustes et les sacrifices:
Pakuti pamene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto ndi kuyankhula nawo, sindinawalamulire kuti azipereka nsembe zopsereza kapena nsembe zinazo,
23 Mais je leur ai donné ce commandement: Écoutez ma parole, et je serai votre Dieu, et vous serez mon peuple; marchez dans toutes mes voies comme je vous l'ordonne, et vous serez bénis.
koma ndinawalamula kuti: Mverani Ine, ndipo ndidzakhala Mulungu wanu ndipo inu mudzakhala anthu anga. Muzitsata zonse zimene ndakulamulirani, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
24 Et ils ne m'ont point écouté, et ils ne m'ont point prêté l'oreille; mais ils ont couru après tous les désirs de leurs cœurs pervers, et ils ont reculé au lieu d'avancer,
Koma anthuwo sanamvere kapena kulabadira; mʼmalo mwake anapitirira kusamvera ndi mitima yawo yoyipa. Iwo anabwerera mʼmbuyo mʼmalo mopita patsogolo.
25 Depuis le jour où leurs pères sont sortis de l'Égypte jusqu'à ce jour. Et je vous ai envoyé mes serviteurs les prophètes de jour en jour dès l'aurore; je les leur ai envoyés,
Kuyambira tsiku limene makolo awo anachoka ku Igupto mpaka lero lino, ndakhala ndikuwatumizira atumiki anga, aneneri.
26 Et ils ne m'ont point écouté, et ils ne m'ont point prêté l'oreille, et ils ont endurci leur tête plus que leurs pères.
Koma anthuwo sanandimvere kapena kusamalira. Anawumitsa mitima yawo ndi kuchita zoyipa kuposa makolo awo.
27 Or tu leur diras cette parole:
“Ngakhale iwe uwawuze zonsezi koma sadzakumvera. Ngakhale uwayitane koma sadzakuyankha.
28 Voici la nation qui n'a point écouté la voix du Seigneur, et n'a point profité des corrections; la foi est bannie de leur bouche.
Nʼchifukwa chake udzawawuze kuti, ‘Uwu ndi mtundu wa anthu umene sunamvere Yehova Mulungu wake, wosalola kulangizidwa. Choonadi chatha; chazimirira pa milomo yawo.’
29 Coupe tes cheveux, et jette-les loin de toi; et mets une lamentation sur tes lèvres; car le Seigneur a réprouvé, il a répudié la race qui a fait ces choses.
“Tsono meta tsitsi lako ndi kulitaya. Ulire kwambiri pa zitunda zopanda zomera, pakuti Yehova waukana ndi kuwusiya mʼbado umene wamukwiyitsawu.”
30 Car les enfants de Juda ont fait le mal devant moi, dit le Seigneur; ils ont introduit leurs abominations dans la maison où était invoqué mon nom, afin de le profaner.
“Anthu a ku Yuda achita zoyipa pamaso panga, akutero Yehova. Ayimika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi Dzina langa ndipo ayipitsa.
31 Et ils ont bâti l'autel de Tapheth dans la vallée des fils d'Ennom pour y brûler par le feu leurs fils et leurs filles, sacrifice que je ne leur ai point prescrit et auquel je n'ai jamais songé en mon cœur.
Amanga nsanja yopembedzera Tofeti mʼChigwa cha Hinomu kuti apserezereko ana awo aamuna ndi aakazi. Zimenezi Ine sindinawalamulire ngakhale kuziganizira nʼkomwe.
32 A cause de cela, voilà que les jours arrivent, dit le Seigneur, et on ne dira plus: L'autel de Tapheth, la vallée des fils d'Ennom; mais, la vallée des égorgés; et on inhumera les morts en Tapheth, parce qu'on n'aura point d'autre place.
Nʼchifukwa chake masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzawatchulanso malowo Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma adzawatchula Chigwa cha Imfa, chifukwa adzakwirira anthu akufa ku Tofeti mpaka osapezekanso malo owayika.
33 Et les morts de ce peuple seront la proie des oiseaux du ciel et des bêtes fauves des champs; et nul ne sera là pour les chasser.
Ndipo mitembo ya anthu amenewa idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo, ndipo palibe wina amene adzazipirikitse.
34 Et dans les villes de Juda et dans les rues de Jérusalem je ferai taire la voix de la joie et de l'allégresse, la voix du fiancé et de la fiancée; car toute la terre sera devenue une solitude.
Ndidzathetsa nyimbo zonse zachisangalalo ndi zachikondwerero mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya ku Yerusalemu. Sikudzamvekanso mawu a chikondwerero a mkwatibwi ndi mkwati pakuti dzikolo lidzasanduka chipululu.”

< Jérémie 7 >