< Jérémie 14 >

1 Et la parole du Seigneur vint à Jérémie au sujet de la sécheresse.
Awa ndi mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya onena za chilala:
2 La Judée a pleuré, et ses portes sont solitaires, et la terre est pleine de ténèbres, et un cri s'est élevé en Jérusalem.
“Yuda akulira, mizinda yake ikuvutika; anthu ake adzigwetsa pansi mwachisoni, kulira kwa Yerusalemu kwakula.
3 Et les plus grands ont envoyé les plus petits puiser de l'eau. Ceux-ci sont allés aux puits; mais ils n'ont point trouvé d'eau, et ils sont revenus les cruches vides.
Anthu awo wolemekezeka akutuma antchito awo kuti akatunge madzi. Apita ku zitsime osapezako madzi. Choncho amabwerera ndi mitsuko yopanda madzi. Amanyazi ndi othedwa nzeru adziphimba kumaso.
4 Et les travaux de la terre ont péri, parce qu'il ne pleuvait pas; les laboureurs ont été confondus, et ils se sont voilé la tête;
Popeza pansi pawumiratu chifukwa kulibe madzi, alimi ali ndi manyazi ndipo amphimba nkhope zawo.
5 Et les biches ont mis bas dans la plaine, et elles ont abandonné leurs faons, parce qu'il n'y avait point d'herbe.
Ngakhale mbawala yayikazi ikusiya mwana wake wakhanda ku thengo chifukwa kulibe msipu.
6 Les ânes sauvages se sont arrêtés dans les vallons ombragés, et ils ont aspiré l'air; leurs yeux ont défailli, parce qu'il n'y avait point de fourrage.
Mbidzi zikuyima pa zitunda zopanda kanthu nʼkumapuma wefuwefu ngati nkhandwe; maso awo achita chidima chifukwa chosowa msipu.”
7 Nos péchés se sont élevés contre nous, Seigneur; prenez soin de nous à cause de vous-même; car nos péchés contre vous sont nombreux, c'est contre vous que nous avons péché.
Anthu akuti, “Ngakhale machimo athu akutitsutsa, koma Inu Yehova chitanipo kanthu chifukwa cha dzina lanu. Pakuti kusakhulupirika kwathu nʼkwakukulu; ife takuchimwirani.
8 Seigneur, vous êtes l'espérance d'Israël; c'est vous qui sauvez au temps de l'affliction. Pourquoi êtes-vous devenu à notre égard comme un passager sur la terre, ou comme un indigène allant dans une hôtellerie.
Inu Yehova amene Aisraeli amakukhulupirirani ndi amene mumawapulumutsa pa nthawi ya masautso, chifukwa chiyani mukukhala ngati mlendo mʼdziko muno? Chifukwa chiyani muli ngati wapaulendo amene akungogona tsiku limodzi?
9 Serez-vous comme un homme endormi ou comme un homme impuissant à sauver? Vous êtes avec nous, Seigneur, et votre nom est le nom qui nous est donné; ne nous oubliez plus.
Chifukwa chiyani muli ngati munthu amene wadzidzimutsidwa, kapena ngati wankhondo amene alibe mphamvu yopulumutsa? Komabe Inu Yehova, muli pakati pathu, ndipo tikudziwika ndi dzina lanu; musatitaye ife!”
10 Ainsi dit le Seigneur à ce peuple: Ils ont aimé à remuer leurs pieds, et ils n'y ont pas mis de mesure, et Dieu ne les a pas fait prospérer; maintenant il va se souvenir de leurs iniquités.
Zimene Yehova akunena za anthuwa ndi izi: “Iwo amakonda kuyendayenda kwambiri; samatha kudziretsa. Nʼchifukwa chake Ine Yehova sindingawalandire, ndipo tsopano ndidzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo.”
11 Et le Seigneur me dit: Ne me prie pas en faveur de ce peuple pour le bénir.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Usawapempherere anthu awa kuti zinthu ziwayendere bwino.
12 Car lors même qu'ils jeûneraient, je n'exaucerai point leur prière; et s'ils m'offrent des holocaustes et des victimes, je ne les agréerai point. Car moi, je les exterminerai par le glaive, la famine et la mort.
Ngakhale asale zakudya, Ine sindidzamva kulira kwawo; ngakhale apereke nsembe zopsereza ndi chopereka cha chakudya, sindidzazilandira. Mʼmalo mwake, ndidzawapha ndi lupanga, njala ndi mliri.”
13 Et je répondis: O vous, Seigneur vivant, voilà que leurs prophètes prophétisent, et disent: Vous ne verrez pas de glaive; il n'y aura pas de famine parmi vous; car je donnerai à cette terre et à ce lieu la vérité et la paix.
Koma ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova, aneneri amawawuza anthuwo kuti, sadzaphedwa ndi lupanga kapena kuvutika ndi njala. Koma kuti Inu mudzawapatsa mtendere wokhawokha pamalo pano.”
14 Et le Seigneur me dit: Leurs prophètes prophétisent faussement en mon nom; je ne les ai point envoyés; je ne leur ai rien commandé; je ne leur ai rien dit. Ils vous prophétisent d'après des visions mensongères, des augures, des présages, des caprices de leur cœur.
Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Ndi zabodza kuti aneneriwa akunenera mʼdzina langa. Ine sindinawatume kapena kuwasankha kapenanso kuyankhula nawo. Iwo amakuwuzani zinthu zabodza zomwe amati anaziona mʼmasomphenya, kapena pogwiritsa ntchito mawula achabechabe. Zimene amayankhula ndi zongopeka mʼmutu mwawo.
15 À cause de cela, dit le Seigneur, et pour ce qui regarde les prophètes qui prophétisent faussement en mon nom, et que je n'ai point envoyés, et qui disent: Il n'y aura en cette terre ni glaive ni famine, ces prophètes mourront d'une maladie cruelle, et ils seront consumés par la faim,
Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti aneneri amenewa akulosera mʼdzina langa pamene Ine sindinawatume. Iwo amati simudzafa pa nkhondo kapena ndi njala mʼdziko muno. Koma tsono ndi iwowo, aneneriwa amene adzafe pa nkhondo kapena ndi njala.
16 Et le peuple pour qui ils prophétisent, gisant dans les rues de Jérusalem, périra par le glaive ou la famine; et nul n'ensevelira les morts, ni leurs femmes, ni leurs fils, ni leurs filles, et je ferai refluer sur eux leur propre méchanceté.
Ndipo anthu amene anawaloserawo adzaponyedwa mʼmisewu ya mu Yerusalemu atafa ndi njala ndi lupanga. Sipadzapezeka wowayika mʼmanda popeza iwowo, akazi awo, ana awo aamuna, onse adzakhala atafa. Ine ndidzawagwetsera chilango chowayenera.
17 Et tu leur diras cette parole: Que vos yeux versent des larmes nuit et jour, et que vos pleurs ne s'arrêtent pas; car la fille de mon peuple a été écrasée et broyée, et sa blessure est pleine de douleurs.
“Awuze mawu awa: “‘Maso anga akugwetsa misozi kosalekeza usana ndi usiku; chifukwa anthu anga okondedwa apwetekeka kwambiri, akanthidwa kwambiri.
18 Si je sors dans la plaine, voilà des cadavres frappés par le glaive; si je rentre dans la ville, voilà les horreurs de la famine, et le prêtre et le prophète sont allés en une terre qu'ils ne connaissaient pas.
Ndikapita kuthengo, ndikuona amene aphedwa ndi lupanga; ndikapita mu mzinda, ndikuona amene asakazidwa ndi njala. Ngakhale aneneri pamodzi ndi ansembe onse atengedwa.’”
19 Est-ce que vous avez répudié Juda; et votre âme s'est-elle éloignée de Sion? Pourquoi nous avez-vous frappés, et n'y a-t-il pas pour nous de remède? Nous attendions la paix, et il n'est rien venu d'heureux; la guérison, et voilà le trouble.
Kodi anthu a ku Yuda mwawakana kwathunthu? Kodi mtima wanu wanyansidwa nawo anthu a ku Ziyoni? Chifukwa chiyani mwatikantha chotere kuti sitingathenso kuchira? Ife tinayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chabwera, tinayembekezera kuchira koma panali kuopsezedwa kokhakokha.
20 Nous reconnaissons nos péchés et les iniquités de nos pères; car c'est contre vous que nous avons péché.
Inu Yehova, ife tikuvomereza kuyipa kwathu ndiponso kulakwa kwa makolo athu; ndithu ife tinakuchimwiranidi.
21 Cessez, en faveur de votre nom, de détruire le trône de votre gloire; souvenez-vous et ne rompez point votre alliance avec nous.
Musatikane kuopa kuti dzina lanu linganyozedwe; musanyoze mpando wanu waufumu waulemerero. Kumbukirani pangano lanu ndi ife ndipo musachiphwanye.
22 Y a-t-il une seule idole des nations qui fasse tomber la pluie? Et si le ciel nous accorde ses largesses, n'est-ce point par vous? Aussi nous espérons en vous, Seigneur; car c'est vous qui avez fait toutes ces choses.
Mwa milungu yachabechabe ya anthu a mitundu ina, kodi pali mulungu amene angagwetse mvula? Ife chikhulupiriro chathu chili pa Inu, popeza Inu nokha ndinu Yehova Mulungu wathu amene mukhoza kuchita zimenezi.

< Jérémie 14 >