< Isaïe 1 >

1 Vision d'Isaïe, fils d'Amos, qu'il eut sur la Judée et Jérusalem, sous le règne d'Ozias et de Joatham, d'Achaz et d'Ézéchias, qui furent rois de la Judée.
Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.
2 Écoute, ciel; prête l'oreille, terre, parce que le Seigneur a parlé, disant: J'ai engendré des fils, et je les ai élevés en gloire; mais eux, ils m'ont méprisé.
Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi! Pakuti Yehova wanena kuti, “Ndinabala ana ndi kuwalera, koma anawo andiwukira Ine.
3 Le bœuf connaît son possesseur, et l'âne, la crèche de son maître; pour Israël, il m'a méconnu, et son peuple ne m'a pas compris.
Ngʼombe imadziwa mwini wake, bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake, koma Israeli sadziwa, anthu anga samvetsa konse.”
4 Malheur à toi, peuple pécheur, nation pleine de péchés, race de méchants, fils pervertis! vous avez abandonné le Seigneur, et irrité le Saint d'Israël.
Haa, mtundu wochimwa, anthu olemedwa ndi machimo, obadwa kwa anthu ochita zoyipa, ana odzipereka ku zoyipa! Iwo asiya Yehova; anyoza Woyerayo wa Israeli ndipo afulatira Iyeyo.
5 A quoi bon vous frapper encore, en ajoutant à votre iniquité? Toute tête est en souffrance, et tout cœur en tristesse.
Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe? Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira? Mutu wanu wonse uli ndi mabala, mtima wanu wonse wafowokeratu.
6 Des pieds à la tête, rien n'est sain en lui, rien qui ne soit contusion, meurtrissure, plaie enflammée; point d'émollients à y appliquer, point d'huile, point de ligature.
Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu palibe pabwino, paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda, mabala ali magazi chuchuchu, mabala ake ngosatsuka, ngosamanga ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.
7 Votre terre est déserte, vos villes consumées par le feu; votre contrée, des étrangers la dévorent sous vos yeux; elle est désolée et bouleversée par des nations étrangères.
Dziko lanu lasanduka bwinja, mizinda yanu yatenthedwa ndi moto; minda yanu ikukololedwa ndi alendo inu muli pomwepo, dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.
8 La fille de Sion sera délaissée comme une tente dans une vigne, comme la cabane d'un garde dans un champ de concombres, comme une ville prise d'assaut.
Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha ngati nsanja mʼmunda wampesa, ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka, ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.
9 Et si le Seigneur des armées ne nous eût laissé une semence, nous serions comme Sodome, nous ressemblerions à Gomorrhe.
Yehova Wamphamvuzonse akanapanda kutisiyira opulumuka, tikanawonongeka ngati Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.
10 Ecoutez la parole du Seigneur, princes de Sodome; soyez attentifs à la loi de Dieu, peuple de Gomorrhe.
Imvani mawu a Yehova, inu olamulira Sodomu; mverani lamulo la Mulungu wathu, inu anthu a ku Gomora!
11 Qu'ai-je besoin de la multitude de vos victimes? Je suis rassasié des holocaustes de béliers; la graisse des agneaux, le sang des taureaux et des boucs, je n'en veux plus.
Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani nsembe zanu zochuluka?” “Zandikola nsembe zanu zopsereza za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa; sindikusangalatsidwanso ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.
12 Ne venez plus vous montrer à moi; car qui vous a demandé ces offrandes de vos mains? Ne continuez plus de fouler mon parvis.
Ndani anakulamulirani kuti mubwere nazo pamaso panga? Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?
13 Quand vous m'apportez de la fleur de farine, ou un encens inutile, c'est pour moi une abomination. Vos nouvelles lunes, vos sabbats, votre grand jour, je ne puis les souffrir; votre jeûne, votre repos,
Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo! Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine. Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa, kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.
14 Vos nouvelles lunes, vos fêtes, mon âme les déteste. Je vous ai en dégoût, je ne vous remettrai plus vos péchés.
Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika ndimadana nazo. Zasanduka katundu wondilemera; ndatopa kuzinyamula.
15 Si vous étendez la main, je détournerai de vous mes yeux; et si vous multipliez vos prières, je ne vous écouterai pas; car vos mains sont pleines de sang.
Mukamatambasula manja anu popemphera, Ine sindidzakuyangʼanani; ngakhale muchulukitse mapemphero anu, sindidzakumverani. Manja anu ndi odzaza ndi magazi;
16 Lavez-vous, soyez purs; ôtez de devant mes yeux la malice de vos âmes; mettez fin à vos méfaits.
sambani, dziyeretseni. Chotsani pamaso panu ntchito zanu zoyipa! Lekani kuchita zoyipa,
17 Apprenez à faire le bien, cherchez la justice, protègez l'opprimé; jugez équitablement l'orphelin, rendez justice à la veuve.
phunzirani kuchita zabwino! Funafunani chilungamo, thandizani oponderezedwa. Tetezani ana amasiye, muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”
18 Et puis venez m'accuser, dit le Seigneur. Et quand même vos péchés seraient comme la pourpre, je les rendrai blancs comme la neige; et quand ils seraient comme de l'écarlate, je les rendrai blancs comme une toison.
Yehova akuti, “Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu. Ngakhale machimo anu ali ofiira, adzayera ngati thonje. Ngakhale ali ofiira ngati kapezi, adzayera ngati ubweya wankhosa.
19 Et si vous êtes de bonne volonté, si vous m'écoutez, vous mangerez les biens de la terre.
Ngati muli okonzeka kundimvera mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;
20 Mais si vous n'êtes point de bonne volonté, si vous ne m'écoutez point, le glaive vous dévorera; car voici ce qu'a dit la bouche du Seigneur:
koma mukakana ndi kuwukira mudzaphedwa ndi lupanga.” Pakuti Yehova wayankhula.
21 Comment est devenue prostituée Sion, la cité fidèle, jadis pleine de justice? L'équité reposait en elle, et maintenant ce sont des meurtriers.
Taonani momwe mzinda wokhulupirika wasandukira wadama! Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama; mu mzindamo munali chilungamo, koma tsopano muli anthu opha anzawo!
22 Votre argent n'est pas de bon aloi; vos cabaretiers mêlent de l'eau à leur vin.
Siliva wako wasanduka wachabechabe, vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.
23 Vos princes sont incrédules, associés aux voleurs, amis des présents, gagnés par les salaires, sans justice pour les orphelins, sans égard pour la cause des veuves.
Atsogoleri ako ndi owukira, anthu ogwirizana ndi mbala; onse amakonda ziphuphu ndipo amathamangira mphatso. Iwo sateteza ana amasiye; ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.
24 C'est pourquoi voici ce que dit le Seigneur, maître des armées: Malheur aux puissants d'Israël! car ma fureur contre mes adversaires ne s'apaisera point, et je tirerai vengeance de mes ennemis.
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu, Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti, “Haa, odana nane ndidzawatha, ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.
25 Et je ferai tomber ma main sur toi, et je te purifierai par le feu; et j'exterminerai les incrédules, et j'enlèverai tous les prévaricateurs loin de toi.
Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe; ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa, monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.
26 Et je rétablirai tes juges comme autrefois, et tes conseillers comme dès le commencement. Et après cela tu seras appelée Ville de justice, métropole fidèle, Sion.
Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana, aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja. Kenaka iweyo udzatchedwa mzinda wolungama, mzinda wokhulupirika.”
27 Car ses captifs seront délivrés par le jugement et par la miséricorde.
Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama, anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.
28 Et les méchants seront écrasés, et avec eux les pécheurs; et ceux qui auront abandonné le Seigneur périront avec eux.
Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi, ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.
29 C'est pourquoi ils seront confondus par les idoles mêmes qu'ils avaient voulues, et ils rougiront des jardins qu'ils avaient convoités.
“Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu imene inkakusangalatsani; mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda imene munayipatula.
30 Car ils seront comme un térébinthe dépouillé de ses feuilles, et comme un jardin sans eau.
Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota, mudzakhala ngati munda wopanda madzi.
31 Et leur force sera comme le chaume du concombre, et leurs œuvres comme des étincelles, et les méchants seront consumés, et avec eux le pécheur; et nul ne sera là pour éteindre la flamme.
Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma, ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali; motero zonse zidzayakira limodzi, popanda woti azimitse motowo.”

< Isaïe 1 >