< Isaïe 3 >

1 Voilà que le Dominateur, Dieu des armées, va enlever de la Judée et de Jérusalem le puissant et la puissante, la force du pain et la force de l'eau;
Taonani tsopano, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda zinthu pamodzi ndi thandizo; adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,
2 Le grand, le fort et l'homme de guerre, le juge, le sage et l'ancien;
anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo, oweruza ndi aneneri, anthu olosera ndi akuluakulu,
3 Le chef de cinquante hommes et le conseiller vénérable, l'habile architecte et l'auditeur intelligent.
atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka, aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.
4 Et je ferai des jeunes gens leurs princes, et des railleurs les gouverneront.
Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo; ana akhanda ndiwo adzawalamulire.
5 Et le peuple en viendra aux mains, homme contre homme, ami contre ami; l'enfant frappera sur le vieillard, l'infâme sur l'honnête homme.
Anthu adzazunzana, munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake. Anthu wamba adzanyoza akuluakulu.
6 L'homme prendra son frère ou son proche parent dans la famille de son père, et il lui dira: Tu as un manteau, sois notre prince, et que ma nourriture soit dans ta main.
Munthu adzagwira mʼbale wake mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati, “Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu; lamulira malo opasuka ano!”
7 Et ce jour-là l'antre répondra: Je ne serai pas ton prince, car il n'y a en ma maison ni pain ni manteau; je ne serai pas le prince de ce peuple.
Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti, “Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake. Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga; musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”
8 Car Jérusalem est ruinée et Juda est tombé; et leurs langues sont avec l'iniquité, et ils n'obéissent point au Seigneur. C'est pourquoi leur gloire est maintenant abaissée,
Yerusalemu akudzandira, Yuda akugwa; zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova, sakulabadira ulemerero wa Mulungu.
9 Et la confusion de leur visage porte témoignage contre eux; et, comme Sodome, ils ont montré et proclamé leur péché. Malheur à leurs âmes! car ils ont pris une funeste résolution contre eux-mêmes,
Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa; amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu; salibisa tchimo lawolo. Tsoka kwa iwo odziputira okha mavuto.
10 Disant: Enchaînons le juste, parce qu'il nous est insupportable. Aussi goûteront-ils les fruits de leurs œuvres.
Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino, pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.
11 Malheur à l'impie! il lui arrivera mal à cause des œuvres de ses mains.
Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo! Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.
12 Mon peuple, tes exacteurs rapinent, et des usuriers te maîtrisent; mon peuple, ceux qui te déclarent heureux t'égarent, et ils bouleversent le sentier où tu marches.
Achinyamata akupondereza anthu anga, ndipo amene akuwalamulira ndi akazi. Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani; akukuchotsani pa njira yanu.
13 Mais maintenant le Seigneur va siéger pour juger, et il entrera en jugement avec son peuple.
Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu; wakonzeka kuti aweruze anthu ake.
14 Le Seigneur en personne entrera en jugement avec les anciens et les princes du peuple. Ô vous donc, pourquoi avez-vous mis le feu à ma vigne? pourquoi la dépouille du pauvre est-elle en vos maisons?
Yehova akuwazenga milandu akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake: “Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa; nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.
15 Pourquoi faites-vous tort à mon peuple? pourquoi couvrez-vous de confusion la face des pauvres?
Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga, nʼkudyera masuku pamutu amphawi?” Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
16 Or voici ce que dit le Seigneur: Parce que les filles de Sion sont altières, et qu'elles ont marché la tête haute, en faisant signe des yeux, et qu'elles ont traîné leurs tuniques du mouvement de leurs pieds, et qu'elles ont eu une démarche étudiée,
Yehova akunena kuti, “Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri, akuyenda atakweza makosi awo, akukopa amuna ndi maso awo akuyenda monyangʼama akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo
17 Dieu humiliera dans Sion les filles du premier rang, et le Seigneur les dépouillera de leurs ornements.
Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo; Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”
18 Et ce jour-là le Seigneur détruira la gloire de leur parure, leurs réseaux, leurs tresses et leurs épingles d'or,
Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi,
19 Et leurs colliers et le fard de leur visage,
ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope,
20 Et l'ensemble de leurs joyaux de gloire, bracelets, anneaux, chaînettes, bagues et pendants d'oreilles,
maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa,
21 Et leurs franges de pourpre et leurs robes de pourpre,
mphete ndi zipini,
22 Et leurs habits de l'intérieur de la maison, et leurs habits transparents de Laconie,
zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama,
23 Et leurs robes de fin lin, d'hyacinthe et d'écarlate, et leurs tissus de fin lin, d'or et d'hyacinthe, et leurs longs voiles d'été.
magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa.
24 Et au lieu de suaves parfums tu te couvriras de cendre; et au lieu de tes rubans tu te ceindras d'une corde; et au lieu d'une tête ornée de bijoux d'or tu auras un crâne chauve, en punition de tes œuvres; et au lieu d'une tunique de pourpre tu te revêtiras d'un cilice.
Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha, mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe; mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi; mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli; mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.
25 Et le fils si beau que tu chéris tombera sous le glaive, et tes forts périront par l'épée.
Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga, asilikali ako adzafera ku nkhondo.
26 Et ils seront humiliés, et les trésors où tu gardais tes bijoux pleureront; et tu resteras seule, et tu seras brisée contre terre.
Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira; Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.

< Isaïe 3 >