< Isaïe 43 >

1 Et maintenant voici ce que dit le Seigneur: Qui t'a créé, Jacob? qui t'a formé, Israël? Ne crains pas, car je t'ai racheté; je t'ai donné ton nom, tu es à moi.
Koma tsopano, Yehova amene anakulenga, iwe Yakobo, amene anakuwumba, iwe Israeli akuti, “Usaope, pakuti ndakuwombola; Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.
2 Si tu traverses les eaux, je suis avec toi; et les fleuves ne pourront te submerger; et si tu passes à travers la flamme, tu ne seras point brûlé, le feu ne te brûlera pas.
Pamene ukuwoloka nyanja, ndidzakhala nawe; ndipo pamene ukuwoloka mitsinje, sidzakukokolola. Pamene ukudutsa pa moto, sudzapsa; lawi la moto silidzakutentha.
3 Car je suis le Seigneur ton Dieu, le Saint d'Israël, ton sauveur. J'ai fait de l'Égypte et de l'Éthiopie ta rançon, et pour toi j'ai livré Soène.
Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako, Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako. Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe, ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.
4 Depuis que tu es devenu précieux devant moi, tu as été glorifié, et je t'aime, et je donnerai pour toi les hommes, et pour ta tête les princes.
Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga, ndipo chifukwa ndimakukonda, ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe, ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.
5 Ne crains pas, car je suis avec toi. De l'Orient je ramènerai ta race; je te ferai revenir de l'Occident.
Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe; ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa, ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.
6 Je dirai à l'aquilon: Ramène-les; et au midi: Ne retiens pas, ramène de loin mes fils, ramène mes filles des extrémités de la terre.
Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’ ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’ Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali, ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;
7 Ramène tous ceux qui ont invoqué mon nom; car j'ai préparé ce peuple, je l'ai formé, je l'ai fait pour ma gloire;
onsewo amadziwika ndi dzina langa; ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga, ndinawawumba, inde ndinawapanga.”
8 Et j'ai éloigné de moi un peuple aveugle, et ses yeux étaient comme aveuglés, et ses oreilles étaient sourdes.
Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya, anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.
9 Voilà tous les Gentils rassemblés à la fois, voilà leurs princes. Qui d'entre eux annoncera ces choses? Qui annoncera les choses à partir du commencement? Qu'ils produisent leurs témoins, qu'ils se justifient, qu'ils écoutent et disent la vérité.
Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi, anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu. Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi? Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale? Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona, kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”
10 Soyez pour moi des témoins, et moi-même je porterai témoignage, dit le Seigneur Dieu; et aussi mon serviteur, celui que j'ai élu, afin que vous sachiez, que vous croyiez et compreniez que je suis. Avant moi il n'y a pas eu d'autre Dieu, et il n'en sera point après moi.
Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga, ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha, kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha. Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina, ngakhale pambuyo panga sipadzakhalaponso wina.”
11 Je suis Dieu, et, hormis moi, nul ne sauve.
Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova, ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.
12 J'ai prédit, j'ai sauvé, j'ai fait des reproches, et il n'y avait pas avec vous d'étranger. Vous êtes mes témoins, et moi je suis le Seigneur Dieu.
Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa; ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu. Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.
13 Je suis depuis le commencement, et il n'est personne qui puisse rien arracher de mes mains. Je ferai mon œuvre, et qui la détruira?
“Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse. Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga, ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”
14 Voici ce que dit le Seigneur Dieu qui vous a racheté, le Saint d'Israël: A cause de vous, j'enverrai un ennemi contre Babylone, et je les ferai tous fuir, et les Chaldéens seront enchaînés dans des vaisseaux.
Yehova akuti, Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti, “Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni ndi kukupulumutsani. Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.
15 Je suis le Seigneur Dieu, votre Saint, qui ai institué votre roi en Israël.
Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja, Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”
16 Voici ce que dit le Seigneur, qui traça une voie dans la mer, et des sentiers sur les grandes eaux;
Yehova anapanga njira pa nyanja, anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.
17 Qui y fit entrer des chars, des chevaux et une puissante multitude. Mais ils se sont endormis et ils ne se réveilleront plus; ils se sont éteints comme une mèche qu'on a éteinte.
Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo, gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu, ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,
18 Mais vous ne vous souvenez pas des choses du commencement; vous ne considérez point ce qui s'est fait autrefois.
“Iwalani zinthu zakale; ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.
19 Eh bien, je ferai de nouveaux prodiges, qui vont naître tout à l'heure, et vous les connaîtrez; je tracerai une voie dans le désert, et je ferai jaillir des fleuves sur une terre sans eau.
Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano! Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona? Ine ndikulambula msewu mʼchipululu ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.
20 Les bêtes des champs me béniront avec les petits oiseaux et les jeunes passereaux, parce que j'aurai donné de l'eau à une terre aride, et des fleuves au désert, pour abreuver ma race élue,
Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi zinandilemekeza. Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma kuti ndiwapatse madzi anthu anga osankhidwa.
21 Mon peuple dont j'ai pris soin, pour qu'il raconte mes vertus.
Anthu amene ndinadziwumbira ndekha kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.
22 Et pourtant je ne t'ai pas appelé, Jacob; je ne t'ai point coûté de fatigues, Israël!
“Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo, munatopa nane, Inu Aisraeli.
23 Tu ne m'as point offert d'holocauste de tes brebis; tu ne m'as point glorifié par tes sacrifices; je ne t'ai point assujetti à m'immoler des victimes; je ne t'ai pas donné la peine de brûler pour moi de l'encens.
Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza, kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu. Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.
24 Tu n'as pas acheté pour moi des victimes à prix d'argent; je n'ai point désiré la génisse de tes sacrifices, mais tu t'es présenté devant moi avec tes péchés et ton injustice.
Simunandigulire bango lonunkhira kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu. Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.
25 C'est moi cependant, c'est moi qui efface tes transgressions et tes péchés, à cause de moi-même, et je n'en garderai pas le souvenir.
“Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini, ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.
26 De ton côté souviens-toi, et plaidons ensemble; confesse d'abord tes iniquités, afin que tu sois justifié.
Mundikumbutse zakale, ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi; fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.
27 Vos pères les premiers, et vos princes ont péché contre moi.
Kholo lanu loyamba linachimwa; ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.
28 Et vos princes ont profané mes choses saintes, et j'ai livré Jacob et Israël à l'opprobre et à la destruction.
Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero, ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”

< Isaïe 43 >