< Isaïe 41 >

1 Faites-moi fête; car les princes ont recouvré leurs forces: qu'ils approchent, qu'ils parlent tous à la fois, et qu'alors ils proclament le jugement.
“Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja! Alekeni ayandikire ndi kuyankhula; tiyeni tikhale pamodzi kuti atiweruze.
2 Qui donc a suscité de l'Orient la justice? Il lui a dit: Viens à mes pieds; et elle y viendra. Il la fera comparaître devant les nations; il frappera les rois de stupeur. Il fera tomber à terre leurs glaives; il repoussera comme des broussailles leurs arcs et leurs flèches.
“Ndani anadzutsa wochokera kummawa uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita? Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
3 Et il les poursuivra; et il parcourra en paix la voie de ses pieds.
Amawalondola namayenda mosavutika, mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
4 Qui a opéré, qui a fait ces choses? C'est celui qui a appelé la justice, qui l'a appelée dès le commencement des générations. Je suis Dieu, le premier, et pour tous les siècles à venir je suis.
Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza, si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu? Ine Yehova, ndine chiyambi ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”
5 Les nations ont vu, et elles ont eu crainte, et elles sont accourues des extrémités de la terre; et elles sont venues toutes à la fois.
Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa; anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera. Akuyandikira pafupi, akubwera;
6 Chaque homme, jugeant pour son prochain, et pour secourir son frère, dira:
aliyense akuthandiza mnzake ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
7 L'artisan a réuni tous ses efforts, ainsi que l'ouvrier qui forge au marteau; et il dira: Voilà une pièce bien jointe; on en a ajusté les parties avec des clous, on va les fixer, et elles ne seront pas ébranlées.
Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide, ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala. Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.” Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.
8 Et toi, Israël, toi, Jacob, mon serviteur, toi que j'ai choisi, postérité d'Abraham, mon bien-aimé;
“Koma Iwe Israeli mtumiki wanga, Yakobo amene ndakusankha, Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
9 Toi que j'ai fait revenir des extrémités de la terre; je t'ai convoqué du haut de toutes ses collines, et je t'ai dit: Tu es mon serviteur; je t'ai élu, et je ne t'ai pas abandonné.
Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi, ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi. Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’ Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
10 Ne crains pas, car je suis avec toi; ne t'égare pas, car je suis ton Dieu; c'est moi qui t'ai fortifié, moi qui t'ai secouru, et t'ai affermi par la justice de ma droite.
Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe; usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.
11 Voilà que tous tes adversaires vont être humiliés et confondus; car ils seront comme s'ils n'étaient pas, et tous tes ennemis périront.
“Onse amene akupsera mtima adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa; onse amene akukangana nawe sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
12 Tu les chercheras et tu ne trouveras plus ces hommes qui t'insultaient dans l'ivresse; car ils seront comme s'ils n'étaient pas, et ceux qui te faisaient la guerre n'existeront plus.
Udzafunafuna adani ako, koma sadzapezeka. Iwo amene akuchita nawe nkhondo sadzakhalanso kanthu.
13 Je suis ton Dieu qui t'ai pris par la main droite et qui te dis: Ne crains pas.
Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako, amene ndikukugwira dzanja lako lamanja ndipo ndikuti, usaope; ndidzakuthandiza.
14 Jacob, Israël, si amoindri que tu sois, c'est moi qui t'ai secouru, dit ton Dieu; c'est moi, ô Israël, qui t'ai racheté.
Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi, iwe wochepa mphamvu Israeli, chifukwa Ine ndidzakuthandiza,” akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
15 Voilà que je t'ai façonné comme les roues d'un char à moudre, neuves et dentelées; et tu moudras les montagnes, et tu aplaniras les collines, et tu les réduiras en poudre.
“Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri. Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya, ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
16 Et tu les vanneras, et le vent les emportera, et un tourbillon les dispersera. Cependant tu te réjouiras dans les saints d'Israël.
Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso adzamwazika ndi kamvuluvulu. Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako, ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:
17 Et les pauvres et les indigents tressailliront d'allégresse; car ils auront cherché de l'eau, et il n'y en avait pas; et leur langue était desséchée par la soif. Mais moi, le Seigneur Dieu, moi le Dieu d'Israël, je les entendrai et je ne les abandonnerai pas.
“Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi, koma sakuwapeza; ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu. Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo; Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
18 Je ferai jaillir des fleuves sur les monts, et des sources dans la plaine; je changerai le désert en étangs, et la terre altérée en eaux courantes.
Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma, ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa. Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.
19 Dans la terre sans eau je placerai le cèdre, le buis, le myrte, le cyprès et le peuplier:
Mʼchipululu ndidzameretsa mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi. Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,
20 Afin que partout on voie, on sache, on comprenne, on sente à la fois que la main du Seigneur a fait ces choses, et que le Saint d'Israël les a montrées.
kuti anthu aone ndi kudziwa; inde, alingalire ndi kumvetsa, kuti Yehova ndiye wachita zimenezi; kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.
21 Votre jugement est proche, dit le Seigneur Dieu, et proches sont vos conseils, dit le Roi de Jacob.
“Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’ Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’
22 Qu'ils approchent, qu'ils vous annoncent ce qui doit arriver, ou ce qui d'abord a existé; parlez, et nous appliquerons notre pensée à votre parole, et nous saurons ce que sont les choses de la fin, les choses à venir.
Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze zomwe zidzachitike mʼtsogolo. Tifotokozereni zinthu zamakedzana tiziganizire ndi kudziwa zotsatira zake. Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,
23 Dites-nous, annoncez-nous les choses de la fin, et nous reconnaîtrons que vous êtes des dieux. Faites le bien, faites le mal, et nous admirerons, et en même temps nous verrons
tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani, ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu. Chitani chinthu chabwino kapena choyipa, ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.
24 D'où vous venez et d'où viennent vos œuvres: on vous a tirés de l'abomination de la terre.
Koma inu sindinu kanthu ndipo zochita zanu nʼzopandapake; amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.
25 Mais moi j'ai suscité celui qui vient de l'Aquilon et celui qui vient de l'Orient; ils seront appelés en mon nom. Que viennent les princes, et vous serez foulés aux pieds, comme l'argile du potier; ils vous fouleront comme le potier foule l'argile.
“Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera, munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana. Amapondaponda olamulira ngati matope, ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.
26 Qui donc, en effet, publiera les choses du commencement, afin que nous sachions ce qui précédemment a existé? Alors nous dirons: Cela est véritable. Mais il n'est personne qui prédise, ni qui écoute vos discours.
Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe, kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’ Palibe amene ananena, palibe analengeza zimenezi, palibe anamva mawu anu.
27 Je donnerai la principauté à Sion, et dans la voie je consolerai Jérusalem.
Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’ Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.
28 Car nul des Gentils, nulle des idoles ne peut rien apprendre; et si je leur demande: D'où venez-vous? nul ne pourra répondre.
Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe, palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu, palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.
29 Ce sont ceux qui vous fabriquent qui induisent les hommes en erreur.
Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo! Zochita zawo si kanthu konse; mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.

< Isaïe 41 >