< Isaïe 39 >

1 En ce temps-là, Marodach Baladan, fils de Baladan, roi de Babylone, envoya à Ézéchias des lettres, des messagers et des présents, parce qu'il avait appris sa maladie mortelle et sa guérison.
Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira.
2 Et à cause d'eux Ézéchias fut réjoui, et il leur montra la maison de Nechotha, et l'or, et l'argent, les parfums, les aromates et la myrrhe, puis l'arsenal et ses magasins, enfin tout ce qui se trouvait dans ses trésors. Et il n'y eut rien qu'Ézéchias ne fit voir dans son palais et dans ses domaines.
Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.
3 Mais le prophète Isaïe alla trouver le roi Ézéchias, et il lui dit: Que vous ont dit ces hommes, et d'où sont-ils venus? Ézéchias répondit: Ils sont venus vers moi d'une contrée lointaine, de Babylone.
Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
4 Et le prophète reprit: Qu'ont-ils vu dans ton palais? Et le roi répondit: Ils ont vu tout ce que mon palais renferme; il n'y a rien que je ne leur aie montré, soit dans mon palais, soit dans mes trésors.
Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?” Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”
5 Et le prophète Isaïe dit à Ézéchias: Écoute la parole du Seigneur des armées.
Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse:
6 Voilà que les jours approchent où tout ce que renferme ton palais, tous les trésors que tes pères ont amassés jusqu'à ce moment, seront pris et iront à Babylone, et ils n'en laisseront rien; ainsi l'a dit Dieu.
Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe.
7 Quant à tes fils que tu as engendrés, ils les prendront, ils les feront eunuques dans le palais du roi de Babylone.
Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”
8 Et Ézéchias dit à Isaïe: Juste est la parole que le Seigneur a prononcée; mais que la paix et la justice se maintiennent tous les jours de ma vie.
Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”

< Isaïe 39 >