< Isaïe 2 >

1 Parole qui vint à Isaïe, fils d'Amos, sur la Judée et sur Jérusalem.
Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:
2 Aux derniers jours la montagne du Seigneur sera glorieuse; sur la cime des monts apparaîtra la maison de Dieu; elle s'élèvera au-dessus des collines, et tous les Gentils y viendront.
Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse, lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.
3 Et maintes nations partiront, disant: Allons et montons à la montagne du Seigneur et à la maison du Dieu de Jacob, et il nous annoncera sa voie, et nous y marcherons; car la loi sortira de Sion, et la parole du Seigneur, de Jérusalem.
Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
4 Et il jugera entre les nations, et il réprimandera nombre de peuples. Et de leurs glaives ils forgeront des charrues, et des faux de leurs javelines; et l'on ne tirera plus l'épée nation contre nation, et l'on n'apprendra plus à se faire la guerre.
Iye adzaweruza pakati pa mayiko, ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
5 Et maintenant venez, maison de Jacob, et marchons à la lumière du Seigneur.
Inu nyumba ya Yakobo, bwerani, tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.
6 Car il avait abandonné son peuple, la maison d'Israël; parce qu'au commencement leur terre était remplie de devins et d'augures, comme celle des Philistins, et que beaucoup d'enfants leur étaient nés de femmes étrangères
Inu Yehova mwawakana anthu anu, nyumba ya Yakobo. Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa; amawombeza mawula ngati Afilisti, ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
7 Leur terre regorgeait d'argent et d'or, et leurs trésors étaient sans nombre. Et leur pays était couvert de chevaux, et l'on ne pouvait compter leurs chars.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide; ndipo chuma chawo ndi chosatha. Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo; ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
8 Et la terre était remplie de leurs œuvres d'abomination, faites de leurs mains, et ils adoraient des dieux façonnés de leurs doigts.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano; iwo amapembedza ntchito ya manja awo, amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
9 Et l'homme se courbait, et le guerrier s'humiliait; non, je ne leur pardonnerai point.
Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa ndi kutsitsidwa. Inu Yehova musawakhululukire.
10 Et maintenant entrez parmi les rochers, et cachez-vous dans la terre devant la crainte du Seigneur, devant sa gloire et sa puissance, lorsqu'il se lèvera pour frapper la terre.
Lowani mʼmatanthwe, bisalani mʼmaenje, kuthawa kuopsa kwa Yehova ndi ulemerero wa ufumu wake!
11 Car les yeux du Seigneur sont en haut, et l'homme en bas. Et la hauteur des hommes sera abattue, et en ce jour le Seigneur seul sera élevé en gloire.
Kudzikuza kwa anthu kudzatha, ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa; Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.
12 Le jour du Seigneur des armées sera contre tout homme insolent et superbe, contre tout homme altier et orgueilleux, et ils seront abaissés.
Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama, ndipo adzagonjetsa onse amphamvu,
13 Ce jour sera contre le grand cèdre du Liban qui s'élève jusqu'au ciel, et contre le palmier de Basan;
tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali, ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
14 Contre les hautes montagnes et les hautes collines,
tsiku la mapiri onse ataliatali ndiponso la zitunda zonse zazitali,
15 Contre les tours altières et les remparts altiers,
tsiku la nsanja zonse zazitali ndiponso malinga onse olimba,
16 Contre tous les vaisseaux de la mer, et contre les plus beaux navires.
tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi ndiponso la mabwato onse okongola.
17 Et tout homme sera humilié, et l'orgueil des hommes tombera, et en ce jour le Seigneur sera seul élevé en gloire.
Kudzikuza kwa munthu kudzatha ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa, Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
18 Et ils cacheront toutes les idoles, œuvres de leurs mains,
ndipo mafano onse adzatheratu.
19 Les emportant dans les cavernes, dans les fentes des rochers, dans les profondeurs de la terre, devant la crainte du Seigneur, devant sa gloire et sa puissance, lorsqu'il se lèvera pour frapper la terre.
Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndi mʼmaenje a nthaka, kuthawa mkwiyo wa Yehova, ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
20 Car ce jour-là l'homme rejettera les abominations d'or et d'argent qu'il aura faites pour adorer de vaines idoles et des oiseaux de nuit;
Tsiku limenelo anthu adzatayira mfuko ndi mileme mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide, amene anawapanga kuti aziwapembedza.
21 En pénétrant dans les creux, dans les cavernes et les fentes des plus durs rochers, devant la crainte du Seigneur, devant sa gloire et sa puissance, quand il se lèvera pour frapper la terre.
Adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka kuthawa mkwiyo wa Yehova ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
Lekani kudalira munthu, amene moyo wake sukhalira kutha. Iye angathandize bwanji wina aliyense?

< Isaïe 2 >