< Osée 8 >

1 Ils seront frappés au sein d'un coup rapide contre terre, ou comme l'aigle s'abattant sur la maison du Seigneur, parce qu'ils ont transgressé Mon alliance et péché contre Ma loi.
“Ika lipenga pakamwa pako. Ngati chiwombankhanga, kutsutsana ndi nyumba ya Yehova chifukwa anthu aphwanya pangano langa ndiponso agalukira lamulo langa.
2 Et ils crieront vers Moi, en disant: Ô Dieu, nous Te reconnaissons!
Israeli akulirira kwa Ine kuti, ‘Inu Mulungu wathu, ife timakudziwani!’
3 Israël a pris en haine le bien; ils M'ont poursuivi comme un ennemi.
Koma Israeli wakana zabwino; mdani adzamuthamangitsa.
4 Ils ont fait pour eux, et non pour Moi, des rois qui ont régné, sans Me les faire connaître; avec leur argent et leur or, ils se sont fabriqué des idoles, et c'est pour cela qu'ils ont été exterminés.
Amalonga mafumu mosatsata kufuna kwanga. Amasankha akalonga popanda chilolezo changa. Amadzipangira mafano asiliva ndi agolide koma adzawonongeka nawo.
5 Répudie ton veau, Samarie; Ma colère est exaspérée contre eux: jusques à quand sera-t-il impossible qu'ils soient purifiés
Iwe Samariya, taya fano lako la mwana wangʼombe! Mkwiyo wanga wayakira anthuwo. Padzapita nthawi yayitali chotani asanasinthike kukhala oyera mtima?
6 en Israël? C'est un artisan qui l'a fait; il n'est point Dieu; c'est pourquoi ton veau t'a égaré, Samarie.
Mafanowa ndi ochokera ku Israeli! Mwana wa ngʼombe uyu anapangidwa ndi munthu waluso; si Mulungu amene anamupanga. Adzaphwanyidwa nʼkukhala zidutswa, mwana wangʼombe wa ku Samariya.
7 Ils ont semé du grain éventé, et leur destruction en fera la récolte. Ils n'ont pas une gerbe dont on puisse faire de la farine, et s'il y en a, les étrangers la mangeront.
“Aisraeli amadzala mphepo ndipo amakolola kamvuluvulu. Tirigu alibe ngala; sadzabala chakudya. Akanabala chakudya alendo akanadya chakudyacho.
8 Israël a été dévoré; il est maintenant parmi les nations comme un vase inutile,
Israeli wamezedwa, tsopano ali pakati pa anthu a mitundu ina ngati chinthu cha chabechabe.
9 parce qu'ils sont allés aux Assyriens. Éphraïm a refleuri contre lui-même; ils ont aimé les présents.
Pakuti iwo anapita ku Asiriya ngati mbidzi yongodziyendera pa yokha. Efereimu wadzigulitsa kwa zibwenzi zake.
10 Et c'est pourquoi ils seront livrés aux gentils; alors Je les recevrai, et ils cesseront en peu de temps d'oindre des rois et des princes.
Ngakhale wadzigulitsa pakati pa mitundu ya anthu, Ine ndidzawasonkhanitsa pamodzi. Iwo adzayamba kuzunzika pansi pa ulamuliro wankhanza wa mfumu yamphamvu.
11 Car Éphraïm avait multiplié les autels; mais ceux qu'il a aimés étaient des autels de péché.
“Ngakhale Efereimu anamanga maguwa ambiri a nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo, maguwa amenewa akhala malo ochimwirapo.
12 J'avais écrit pour lui une multitude de préceptes; mais ces lois ont été réputés par lui comme étrangères, même les autels qu'il aime.
Ndinawalembera zinthu zambiri za malamulo anga, koma iwo anaziyesa ngati zinthu zachilendo.
13 Aussi quand ils immoleront une victime et en mangeront les chairs, le Seigneur ne les agréera pas. Alors Il Se souviendra de leur iniquité, et tirera vengeance de leurs crimes. Ils seront retournés en Égypte, et ils mangeront des viandes impures chez les Assyriens.
Amapereka nsembe za nyama kwa Ine ndipo iwo amadya nyamayo, koma Yehova sakondwera nazo. Tsopano Iye adzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo: iwowo adzabwerera ku Igupto.
14 Tel Israël aussi a oublié son Créateur, et ils ont planté des bois sacrés, et Juda a multiplié les villes fortifiées; mais sur ces villes J'enverrai la flamme, et elles seront dévorées jusqu'aux fondations.
Israeli wayiwala Mlengi wake ndipo wamanga nyumba zaufumu; Yuda wachulukitsa mizinda ya malinga. Koma Ine ndidzaponya moto pa mizinda yawoyo, moto umene udzatenthe malinga awo.”

< Osée 8 >