< 2 Rois 5 >

1 Et Naaman, général de l'armée syrienne, était un homme considérable aux yeux de son maître, et d'un aspect imposant; c'était par lui que le Seigneur avait sauvé la Syrie, et l'homme était très-puissant, mais il était lépreux.
Tsono Naamani anali mtsogoleri wa gulu lankhondo a mfumu ya ku Aramu. Iye anali munthu wodalirika pamaso pa mbuye wake ndipo anali wokondedwa kwambiri, chifukwa kudzera mwa iye Yehova anapambanitsa Aaramu. Anali msilikali wolimba mtima, koma anali ndi khate.
2 Or, des maraudeurs sortis de la Syrie avaient emmené captive, de la terre d'Israël, une petite fille qui servait la femme de Naaman,
Tsono magulu a Aaramu anapita ku nkhondo ndipo anakagwira ukapolo mtsikana wamngʼono wa ku Israeli, ndipo ankatumikira mkazi wa Naamani.
3 Cette fille dit à sa maîtresse: Plût à Dieu que mon maître fût en présence du prophète de Dieu en Samarie; il le guérirait de sa lèpre.
Mtsikanayo anawuza mkazi wa Naamani kuti, “Mbuye wanga akanapita kukaonana ndi mneneri amene amakhala ku Samariya, akanachiritsidwa khate lawo.”
4 Et la femme entra auprès de son seigneur, et elle lui dit: La jeune fille de la terre d'Israël a parlé de telle et telle manière.
Naamani anapita kwa mbuye wake kukamuwuza zomwe mtsikana wochokera ku Israeli ananena.
5 Et le roi de Syrie dit à Naaman: Vas-y, va, et j'enverrai une lettre au roi d'Israël. Naaman partit donc, et il prit avec lui dix talents d'argent, six mille sicles d'or, et dix robes diverses.
Mfumu ya ku Aramu inayankha kuti, “Iwe uyenera kupita. Ine ndilembera kalata mfumu ya ku Israeli.” Choncho Naamani ananyamuka kupita ku Samariya, atatenga ndalama za siliva 30,000, ndalama zagolide 6,000 ndiponso zovala khumi za pa chikondwerero.
6 Et il porta au roi d'Israël la lettre où il était écrit: Dès que tu auras reçu cette lettre, tu guériras de sa lèpre mon serviteur Naaman, que j'ai envoyé auprès de toi.
Kalata imene anapita nayo kwa mfumu ya ku Israeli inali ndi mawu awa: “Taonani, ndikutumiza Naamani mtumiki wanga pamodzi ndi kalatayi kwa inu kuti mumuchiritse khate lake.”
7 Quand le roi d'Israël eut lu la lettre, il déchira ses vêtements, et il s'écria: Suis-je un Dieu pour donner la mort et la vie? Pourquoi celui-ci envoie-t-il un homme auprès de moi, afin que je le guérisse de sa lèpre? Vous le voyez, il cherche un prétexte contre moi.
Mfumu ya ku Israeli itangowerenga kalatayo, inangʼamba mkanjo wake ndipo inati, “Kodi ine ndine Mulungu? Kodi ndingathe kupha kapena kupereka moyo? Chifukwa chiyani munthu ameneyu wanditumizira munthu woti ndimuchiritse khate lake? Taonani, iyeyu akungofuna kuti apeze chifukwa choyambanirana nane!”
8 Aussitôt qu'Elisée apprit que le roi d'Israël avait déchiré ses vêtements, il envoya près de lui, disant: Pourquoi as-tu déchiré tes vêtements? Que Naaman vienne me trouver, qu'il sache qu'en Israël il y a un prophète.
Elisa munthu wa Mulungu atamva kuti mfumu ya ku Israeli yangʼamba mkanjo wake, anatumiza uthenga uwu: “Chifukwa chiyani mwangʼamba mkanjo wanu? Mutumizeni munthuyo kwa ine ndipo iyeyo adzadziwa kuti muli mneneri mu Israeli.”
9 Et Naaman y alla avec ses chevaux et son char, et il se tint à la porte d'Elisée.
Choncho Naamani anapita pamodzi ndi akavalo ake ndi magaleta nakayima pa khomo la nyumba ya Elisa.
10 Et le prophète lui envoya un messager, qui lui dit: Pars et baigne-toi sept fois dans le Jourdain, ta chair te reviendra, et tu seras guéri.
Elisa anatumiza uthenga kwa iye woti, “Pita, kasambe kasanu ndi kawiri mu mtsinje wa Yorodani, thupi lako lidzachira ndi kukhalanso monga kale ndipo udzayeretsedwa.”
11 Mais, Naaman irrité s'en alla en disant: Je m'étais dit: Il va certainement venir me trouver; il se tiendra devant moi, il invoquera le nom du Seigneur son Dieu, il imposera les mains sur mes plaies, et il me guérira de la lèpre.
Koma Naamani anachoka mokwiya ndipo anati, “Ine ndimaganiza kuti munthuyu atuluka ndipo ayimirira nayitana dzina la Yehova Mulungu wake, nayendetsa dzanja lake pamwamba pa nthendayi ndi kundichiritsa khate langa.
12 Les eaux de l'Abana et du Pharphar, fleuves de Damas, ne valent-elles pas mieux que toutes les eaux du Jourdain? Si je m'y baigne après mon retour, ne serai-je point plus tôt guéri? Et il s'éloigna, et il partit courroucé;
Kodi Abana ndi Faripara, mitsinje ya ku Damasiko, siyoposa mitsinje ina yonse ya ku Israeli? Kodi sindikanasamba mʼmitsinje imeneyo ndi kuyeretsedwa?” Kotero anatembenuka nachoka ali wokwiya kwambiri.
13 Et ses serviteurs s'approchèrent de lui, disant: Si le prophète t'avait prescrit une grande chose, ne la ferais-tu point? A plus forte raison, puisqu'il t'a dit: Baigne-toi, et tu seras guéri.
Antchito ake anamuyandikira namufunsa kuti, “Abambo anga, mneneri akanakulamulani chinthu chachikulu, kodi inu simukanachita? Nanga nʼzovuta motani zomwe mneneri wanena kuti ‘Kasambeni ndipo mudzayeretsedwa!’”
14 Et Naaman, ayant mis pied à terre, se baigna sept fois dans le Jourdain selon la parole d'Elisée; et sa chair redevint comme la chair d'un petit enfant; il était guéri.
Choncho Naamani anapita ku Yorodani nakadzimiza mʼmadzimo kasanu nʼkawiri, monga momwe munthu wa Mulungu anamuwuzira. Thupi lake linakhalanso monga kale ndipo linakhala losalala ngati la kamnyamata.
15 Et il retourna en personne auprès d'Elisée avec toute sa troupe; arrivé vers le prophète, il se tint debout devant lui, et dit: Je reconnais qu'il n'y a point de Dieu sur la terre sinon en Israël; maintenant reçois la bénédiction de ton serviteur.
Pamenepo Naamani ndi atumiki ake onse anabwerera kwa munthu wa Mulungu uja. Naamani anayima pamaso pa Elisa ndipo anati, “Tsopano ndikudziwa kuti kulibe Mulungu wina pa dziko lonse lapansi koma mu Israeli mokha. Chonde, tsopano landirani mphatso ya mtumiki wanu.”
16 Elisée répondit: Vive le Seigneur, devant qui je me tiens! je n'accepterai rien. L'autre le pressa d'accepter, mais il ne le voulut pas.
Mneneri anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene ine ndimamutumikira, sindidzalandira zimenezi.” Ndipo ngakhale Naamani anamukakamiza, iye anakanabe.
17 Et Naaman dit: Puisque tu refuses, que l'on donne du moins à ton serviteur assez de terre pour charger deux mulets; car ton serviteur ne fera plus d'holocaustes, et ne brûlera plus d'encens pour d'autres dieux; il ne sacrifiera qu'au Seigneur, à cause de cette affaire.
Naamani anati, “Ngati inu simulandira, chonde lolani mtumiki wanu kuti atengeko dothi lokwanira kunyamula abulu awiri, popeza mtumiki wanu sadzaperekanso nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa mulungu wina koma Yehova.
18 Et que le Seigneur pardonne à ton serviteur, si, lorsque mon maître entrera dans le temple de Remman, pour y adorer, appuyé sur mon bras, je me prosterne aussi dans le temple de Remman, pendant que mon maître y adorera; que le Seigneur pardonne alors à ton serviteur.
Koma Yehova andikhululukire ine pa chinthu ichi: Pamene mbuye wanga alowa mʼnyumba ya mapemphero ya Rimoni ine ndimapita naye ndipo ndimakagwada naye limodzi. Pamene ndikugwada mʼnyumba ya mapemphero ya Rimoni, Yehova azikhululukira mtumiki wanu pa chinthu chimenechi.”
19 Le prophète dit à Naaman: Va-t'en en paix. Et il s'éloigna pour retourner en la terre de Debratha.
Elisa anati, “Pita mu mtendere.” Choncho anachoka nayenda pangʼono.
20 Mais Giézi, le serviteur d'Elisée, se dit: Voilà que mon maître s'est abstenu de rien accepter des choses qu'avait apportées ce Naaman le Syrien; vive le Seigneur! je courrai après lui, et j'en obtiendrai quoi que ce soit.
Koma Gehazi, mtumiki wa Elisa munthu wa Mulungu, anaganiza mu mtima mwake kuti, “Taonani, mbuye wanga wamulekerera Naamani Mwaramuyu, posalandira zomwe anabweretsa. Pali Yehova wamoyo, ine ndimuthamangira ndipo ndikatengako zinthu kwa iye.”
21 Et Giézi courut après Naaman; le Syrien le vit courant après lui, et il retourna son char pour le rencontrer.
Choncho Gehazi anamuthamangira Naamani uja. Naamani ataona Gehazi akumuthamangira, anatsika mʼgaleta lake ndi kukakumana naye. Iye anafunsa Gehazi kuti, “Kodi nʼkwabwino?”
22 Et Giézi dit: Tout va bien, mon maître m'envoie, disant: Voilà que deux jeunes gens fils de prophètes m'arrivent des montagnes d'Ephraïm, donne-leur un talent d'argent et deux robes.
Gehazi anayankha kuti, “Inde nʼkwabwino. Mbuye wanga wandituma kuti ndidzakuwuzeni kuti, ‘Anyamata awiri mwa ana a aneneri angondipeza kumene kuchokera ku dziko la mapiri la Efereimu. Chonde apatseniko ndalama za siliva 3,000 ndi zovala ziwiri za pa phwando.’”
23 Naaman répondit: Prends un double talent d'argent. Et il prit deux talents d'argent, en deux sacs, et deux robes, puis il les donna à porter à ses deux serviteurs qui partirent devant lui.
Naamani anati, “Kuli bwino utenge ndalama zasiliva 6,000.” Iye anakakamiza Gehazi kuti alandire, ndipo kenaka anamanga matumba awiri a ndalama zasiliva pamodzi ndi zovala zinayi za pa mphwando. Naamani anazipereka kwa antchito ake awiri ndipo anazinyamula nayenda patsogolo pa Gehazi.
24 Il arriva à la brune, prit de leurs mains les présents, les déposa dans la maison, et congédia les deux hommes.
Gehazi atafika ku phiri, anawalanda antchito aja zinthu zija nazibisa mʼnyumbamo. Iye anawawuza anthu aja kuti abwerere ndipo anapita.
25 Lui-même entra ensuite, et se tint auprès de son maître. Or, Elisée lui dit: Giézi, d'où viens-tu? Celui-ci répondit: Ton serviteur ne s'éloigne ni à droite, ni à gauche.
Kenaka analowa mʼnyumbamo nakayima pamaso pa mbuye wake Elisa. Elisa anafunsa kuti, “Kodi Gehazi unali kuti?” Iye anayankha kuti, “Mtumiki wanu sanapite kwina kulikonse.”
26 Et le prophète reprit: Est-ce que mon cœur n'était pas avec toi quand l'homme a retourné son char pour aller à ta rencontre? Et maintenant, tu as pris de l'argent, tu as reçu des robes; tu veux acheter des oliviers, des vignes, des brebis, des bœufs, des serviteurs et des servantes.
Koma Elisa anati kwa Gehazi, “Kodi mzimu wanga sunali nawe pamene munthu uja anatsika mʼgaleta lake ndi kukumana nawe? Kodi ino ndi nthawi yolandira ndalama, kapena kulandira zovala, mitengo ya olivi, minda ya mpesa, nkhosa, ngʼombe kapena antchito aamuna kapena antchito aakazi?
27 Eh bien! la lèpre de Naaman s'attachera à toi et à ta race pour toujours. Et Giézi sortit de sa présence, couvert d'une lèpre blanche comme la neige.
Khate la Naamani lidzakumatirira iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya.” Ndipo Gehazi anachoka pamaso pa Elisa ali ndi khate lotuwa ngati phulusa.

< 2 Rois 5 >