< 2 Rois 3 >

1 Et Joram, fils d'Achab, commença à régner sur Israël, la dix-huitième année du règne de Josaphat en Juda, et il régna douze ans.
Yoramu mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya mʼchaka cha 18 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda ndipo analamulira zaka khumi ndi ziwiri.
2 Et il fit le mal aux yeux du Seigneur, mais point autant que son père et sa mère; il renversa même les colonnes de Baal que son père avait élevées.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova koma sizinafanane ndi zimene anachita abambo ndi amayi ake. Iye anachotsa fano la mwala la Baala limene abambo ake anapanga.
3 Seulement, il resta attaché au péché de Jéroboam, fils de Nabat, où celui- ci avait fait tomber Israël; il ne s'en éloigna point.
Komabe anawumirira kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli ndipo sanafune kuwaleka.
4 Et Mosa, roi de Moab, était nourrisseur de troupeaux, et il rendait au roi d'Israël cent mille moutons et cent mille béliers dans leur toison, de ceux qu'il élevait chaque année.
Tsono Mesa, mfumu ya ku Mowabu ankaweta nkhosa, ndipo iye ankayenera kumapereka kwa mfumu ya ku Israeli chaka ndi chaka ana ankhosa onenepa okwanira 100,000 pamodzi ndi ubweya wankhosa 100,000 zazimuna.
5 Après la mort d'Achab, le roi de Moab refusa son tribut au roi d'Israël.
Koma atamwalira Ahabu, mfumu ya ku Mowabu inawukira mfumu ya ku Israeli.
6 Et le roi Joram, ce jour-là, sortit de Samarie, et il passa en revue Israël.
Choncho nthawi imeneyi mfumu Yoramu inatuluka mu Samariya ndi kukasonkhanitsa Aisraeli onse.
7 Il partit ensuite, et envoya des gens à Josaphat, roi de Juda, disant: Le roi de Moab m'a refusé son tribut: marcheras-tu avec Israël pour combattre Moab? Il répondit: Je marcherai; tu es comme moi, je suis comme toi; ton peuple est comme mon peuple; tes chevaux sont comme mes chevaux.
Yoramu anatumizanso uthenga uwu kwa Yehosafati mfumu ya ku Yuda: “Mfumu ya ku Mowabu yandiwukira. Kodi ungapite nane kukamenyana ndi Mowabu?” Iye anayankha kuti, “Ine ndidzapita nawe. Iwe ndi ine ndife anthu amodzi, anthu anga ali ngati anthu ako, akavalo anga ali ngati akavalo ako.”
8 Et il ajouta: Quel chemin prendrai-je? Joram lui dit: Le chemin du désert d'Edom.
Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi tidzera njira iti popita ku nkhondoko?” Yoramu anayankha kuti, “Tidzera ku Chipululu cha Edomu.”
9 Et le roi d'Israël partit avec le roi de Juda et le roi d'Edom; ils firent sept journées de marche; or, le camp manquait d'eau pour le bétail qui suivait l'armée.
Choncho mfumu ya ku Israeli inanyamuka pamodzi ndi mfumu ya ku Yuda ndi ya ku Edomu. Ndipo atayenda mozungulira mʼchipululu kwa masiku asanu ndi awiri, asilikali analibe madzi woti amwe kapena kumwetsa nyama zawo zosenza katundu.
10 Le roi d'Israël dit alors: Malheur à nous! le Seigneur a appelé, sur ce chemin, les trois rois pour les livrer aux mains de Moab.
Mfumu inafuwula kuti, “Nʼchiyani chomwe chikutichitikira! Kodi Yehova wasonkhanitsa mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu?”
11 Et Josaphat dit: N'y a-t-il point ici de prophète du Seigneur par qui nous puissions le consulter? L'un des serviteurs du roi d'Israël répondit: il y a ici Elisée, fils de Saphat, celui qui versait de l'eau sur les mains d'Elie.
Koma mfumu Yehosafati inafunsa kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wa Yehova woti tingakafunse kwa Yehova kudzera mwa iyeyo?” Mtsogoleri wa ankhondo wa mfumu ya ku Israeli anayankha kuti, “Alipo, Elisa mwana wa Safati. Iye anali mtumiki wa Eliya.”
12 Josaphat reprit: La parole du Seigneur est avec lui. Et le roi d'Israël, ainsi que le roi de Juda et le roi d'Edom, l'alla trouver.
Yehosafati anati, “Yehova amayankhula kudzera mwa iye.” Choncho mfumu ya ku Israeli pamodzi ndi Yehosafati ndiponso mfumu ya ku Edomu anapita kwa Elisa.
13 Or, Elisée dit au roi d'Israël: Qu'y a-t-il entre moi et toi? Va aux prophètes de ton père et aux prophètes de ta mère. Le roi d'Israël reprit: Le Seigneur n'a-t-il pas appelé les trois rois pour les livrer aux mains de Moab?
Elisa ananena kwa mfumu ya ku Israeli kuti, “Pali ubale wanji pakati pa inu ndi ine? Pitani kwa aneneri a abambo ndi amayi anu.” Mfumu ya ku Israeli inayankha kuti, “Ayi, pakuti ndi Yehova amene anatisonkhanitsa ife mafumu atatu pamodzi kuti atipereke mʼmanja mwa Amowabu.”
14 Elisée répondit: Vive le Seigneur Dieu des armées devant qui je me tiens! je ne t'aurais point regardé, je ne t'aurais point vu, si je n'avais respecté la présence de Josaphat, roi de Juda.
Elisa anati, “Pali Yehova Wamphamvuzonse amene ndimamutumikira, pakanapanda kuti ndimamuchitira ulemu Yehosafati mfumu ya ku Yuda, sindikanakulabadirani kapena kukuyangʼanani nʼkomwe.
15 Maintenant, amenez-moi un joueur de harpe. Or, dans le temps que celui-ci jouait, la main du Seigneur fut sur Elisée.
Koma tsopano ndiyitanireni munthu wodziwa kuyimba bwino zeze.” Munthuyo akuyimba zeze, mphamvu ya Yehova inafika pa Elisa,
16 Et il s'écria: Voici ce que dit le Seigneur: Creusez dans cette vallée, faites-y une multitude de fossés.
ndipo anati, “Yehova akuti, ‘Kumbani ngalande mʼchigwa chonse.’
17 Car voici ce que dit le Seigneur: Vous ne verrez point de vent, vous ne verrez point de pluie; néanmoins cette vallée se remplira d'eau, et vous boirez, puis vous abreuverez vos chevaux et votre bétail.
Pakuti Yehova akunena kuti, ‘Simudzaona mphepo kapena mvula, komabe chigwa ichi chopanda madzi chidzadzaza ndi madzi, ndipo inu mudzamwa pamodzi ndi ngʼombe zanu ndiponso nyama zanu zonse.’
18 Ceci est chose légère aux yeux du Seigneur; et je livrerai Moab à vos mains.
Izi ndi zosavuta pamaso pa Yehova. Ndipo adzaperekanso Amowabu mʼmanja mwanu.
19 Vous raserez toutes ses forteresses, vous abattrez tous ses arbres fruitiers, vous comblerez toutes les fontaines, et vous rendrez stérile toute bonne terre en la couvrant de cailloux.
Mudzagonjetsa mizinda yawo yonse yotetezedwa ndiponso mizinda yawo ikuluikulu. Mudzagwetsa mtengo wabwino uliwonse, mudzatseka akasupe onse amadzi, ndiponso mudzawononga minda yawo yonse yachonde poponyamo miyala.”
20 Le lendemain matin, tandis qu'on brûlait la graisse des victimes, les eaux jaillirent du chemin d'Edom, et la terre en fut couverte.
Mmawa mwake, nthawi yopereka nsembe ili pafupi, anangoona madzi akutuluka kuchokera ku Edomu, ndipo malo onse anadzaza ndi madzi.
21 Or, tout Moab apprit que les trois rois venaient le combattre; et il convoqua de toutes parts ses hommes de guerre, et il dit: Malheur à moi! Et l'armée se rangea sur la frontière.
Tsono nʼkuti Amowabu onse atamva kuti mafumu abwera kudzachita nawo nkhondo. Kotero, anayitana munthu aliyense, wamkulu ndi wamngʼono amene ankatha kugwira chida chankhondo ndipo anakayima ku malire a dziko lawo.
22 Et ils se levèrent de grand matin, et le soleil se leva sur les eaux, et Moab vit en face des eaux rouges comme du sang.
Amowabu atadzuka mmamawa, dzuwa likuwala pa madziwo, anaona madziwo akuoneka wofiira ngati magazi patsogolo pawo.
23 Et il dit: Voici du sang versé par l'épée; les rois se seront combattus, chacun aura tué son voisin; maintenant, Moab, à toi les dépouilles.
Ndipo iwo anati, “Taonani magazi! Mafumu aja amenyana okhaokha ndipo aphana. Amowabu, tsopano ndi nthawi yofunkha!”
24 Et ils entrèrent dans le camp d'Israël; mais Israël était debout, il tailla Moab en pièces; les fuyards se dispersèrent devant lui, il entra dans leur contrée et il frappa Moab.
Koma Amowabu atafika ku misasa ya Israeli, Aisraeli ananyamuka ndi kumenyana nawo mpaka anathawa. Ndipo Aisraeli analowa mʼdzikolo ndi kupha Amowabu.
25 Il rasa ses villes fortes; sur toute terre fertile, chaque homme porta un caillou, de sorte qu'elle en fut couverte; les vainqueurs comblèrent toutes les fontaines; ils abattirent tous les arbres fruitiers; il ne resta que les pierres des remparts abattus. Des frondeurs parcoururent la contrée et la frappèrent.
Aisraeli anagumula mizinda yawo ndipo munthu aliyense anaponya mwala pa munda uliwonse wachonde mpaka utadzaza ndi miyala. Iwo anatseka akasupe onse amadzi ndiponso anadula mtengo wabwino uliwonse. Mzinda wa Kiri Hareseti wokha ndiye unatsala wotetezedwa koma anthu oponya miyala anawuzungulira nawuthiranso nkhondo.
26 Quand il vit la bataille perdue, le roi de Moab s'entoura de sept cents hommes vaillants, qui, l'épée à la main, cherchèrent à passer à travers Edom; mais ils ne le purent.
Mfumu ya ku Mowabu itaona kuti nkhondo ikumulaka, inatenga anthu 700 a malupanga kuti athawe modutsa mfumu ya ku Edomu, koma inalephera.
27 Et il prit son fils premier-né, désigné pour régner à sa place, et il l'offrit en holocauste sur les remparts; tout Israël en eut un grand remords; ils s'éloignèrent de lui, et ils retournèrent en la terre promise.
Choncho inatenga mwana wake wamwamuna woyamba kubadwa, amene akanalowa ufumu mʼmalo mwake, ndi kumupereka nsembe pa khoma la mzinda. Zimenezi zinachititsa kuti mkwiyo ndi ukali wa Amowabu ukule kwambiri pa Aisraeli ndipo Aisraeliwo anathawa nabwerera ku dziko la kwawo.

< 2 Rois 3 >