< Job 35 >

1 Elihou reprit et dit:
Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
2 Est-ce cela que tu considères comme juste, cela que tu appelles "ta droiture au regard de Dieu,"
“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
3 de dire: "Quel avantage y trouvé-je? Quel profit de plus que si je faisais mal?"
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
4 Je vais te répondre en quelques mots et à tes amis avec toi.
“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
5 Regarde le ciel et vois, contemple les nuages au-dessus de toi!
Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
6 Si tu agis mal, quelle est ton action sur Dieu? Si tes péchés sont nombreux, que lui importe?
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
7 Si tu agis bien, que lui donnes-tu? Ou qu’est-ce qu’il accepte de toi?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
8 C’Est toi, créature humaine, qu’intéresse ta perversité; c’est à toi, fils d’Adam, qu’importe ta piété.
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
9 On se plaint il est vrai de la multitude d’exactions, on crie contre la violence des grands;
“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 mais on ne dit pas: "Où est Dieu, mon créateur, qui donne lieu à des chants joyeux pendant la nuit;
Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 qui nous Instruit de préférence aux animaux de la terre et nous éclaire plutôt que les oiseaux du ciel?"
amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 Aussi bien, crie-t-on sans trouver d’écho, à cause de l’arrogance des méchants.
Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 Non, Dieu n’écoute pas de vaines doléances, le Tout-Puissant n’y prête nulle attention.
Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 Combien moins encore quand tu dis que tu ne l’aperçois point, que ta cause est par devers lui et que tu es là à l’attendre!
Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
15 Et maintenant si tu prétends que sa colère ne sévit point, parce qu’il ne se soucie pas sérieusement des crimes qui se commettent,
ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 je conclus que Job ouvre la bouche pour des riens, qu’il accumule des paroles manquant de sens.
abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”

< Job 35 >