< Job 34 >

1 Elihou reprit et dit:
Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
2 Ecoutez, ô sages, mes discours, et vous, hommes instruits, prêtez-moi votre attention.
“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
3 Car l’oreille apprécie les discours comme le palais déguste la nourriture.
Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
4 Mettons-nous en quête de ce qui est juste, examinons entre nous ce qui est bon.
Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
5 Car Job a dit: "Je suis innocent, et Dieu m’a refusé justice.
“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
6 En dépit de mon bon droit, je passe pour menteur; cruel est le coup qui m’a frappé, sans que j’aie failli!"
Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
7 Y a-t-il un homme comme Job, buvant le blasphème comme de l’eau,
Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
8 faisant cause commune avec les artisans d’iniquité et allant de pair avec les malfaiteurs?
Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
9 Car il a dit: "L’Homme ne gagne rien à être en bons termes avec Dieu!"
Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
10 C’Est pourquoi, gens d’intelligence, écoutez-moi: loin de Dieu l’iniquité et du Tout-Puissant l’injustice!
“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
11 Car il paie chacun selon ses œuvres et lui assigne le sort mérité par sa conduite.
Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
12 Non, en vérité, Dieu ne commet pas de mal, le Tout-Puissant ne fausse pas la justice.
Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
13 Qui lui a confié la direction de la terre? Qui a mis tout l’univers entre ses mains?
Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
14 S’Il n’avait de pensée que pour lui-même, s’il retirait à lui son esprit et son souffle,
Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
15 toutes les créatures périraient du coup, et l’homme retournerait à la poussière.
zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
16 Or, si tu jouis de ton bon sens, écoute ceci, prête l’oreille au son de mes paroles:
“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
17 Celui qui hait la justice pourrait-il régner? Oseras-tu incriminer l’Etre infiniment juste?
Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
18 Est-il permis de dire au roi: "scélérat!" et aux princes: "criminels!"
Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
19 Eh bien! Lui ne prend pas parti pour les grands, et ne favorise pas le riche contre le pauvre, car ils sont tous l’œuvre de sa main.
Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
20 En un clin d’œil, ils meurent, et au milieu de la nuit, le peuple s’agite et ils disparaissent; on supprime les puissants, sans qu’une main se lève.
Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
21 C’Est que ses yeux sont ouverts sur les voies de l’homme, il observe chacun de ses pas.
“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
22 Point de ténèbres, point d’ombre si profonde où puissent se cacher les malfaiteurs.
Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
23 Car Dieu n’a pas besoin de surveiller longuement un homme, pour le faire comparaître en justice.
Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
24 Il brise les puissants sans long examen et met d’autres à leur place.
Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
25 C’Est parce qu’il connaît leurs œuvres, qu’il les renverse de nuit et les écrase.
Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
26 En qualité d’impies, il les frappe aux yeux de nombreux spectateurs,
Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
27 les punissant de s’être détournés de lui, d’avoir méconnu toutes ses voies,
Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
28 d’avoir fait monter jusqu’à lui les cris du faible, et retentir à ses oreilles la protestation des miséreux.
Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
29 Et s’il fait l’apaisement, qui le lui reprochera? Quand il cache sa face, qui pourra le voir? II domine et sur les nations et sur les individus,
Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
30 ne voulant pas du règne des hommes pervers, de ceux qui sont un piège pour les peuples.
kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
31 Se peut-il qu’on dise à Dieu: "J’Ai expié sans être coupable.
“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
32 Ce qu’il m’est impossible de voir, apprends-le moi toi-même; si j’ai commis des injustices, je ne récidiverai pas?"
ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
33 Est-ce sous ton inspiration qu’Il doit rémunérer, parce que tu exprimes ton dédain ou que tu manifestes tes préférences, toi et non moi? Ce que tu sais, expose-le donc.
Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
34 Les gens sensés me le diront, les hommes sages qui m’écoutent:
“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
35 "Job ne discourt pas en connaissance de cause, ses paroles ne sont pas raisonnables.
‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
36 Mon souhait serait que Job fût éprouvé encore longtemps, à cause de ses réponses dignes d’hommes iniques;
Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
37 car à son péché il ajoute une faute plus grave: il pense triompher au milieu de nous et prodigue ses propos contre Dieu."
Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”

< Job 34 >