< Job 20 >
1 Çophar de Naama prit la parole et dit:
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
2 Eh bien! Mes réflexions m’incitent à répliquer et aussi les impressions que je ressens.
“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
3 Quand j’entends des reproches qui sont un affront pour moi, ma raison me dicte une réponse.
Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
4 Connais-tu ce fait qui a existé de tout temps, depuis que l’homme est placé sur la terre:
“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
5 que le triomphe des méchants est éphémère et que la joie du pervers ne dure qu’un instant?
kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
6 Dût sa stature monter jusqu’au ciel et sa tête atteindre les nuages,
Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
7 aussi sûrement que ses excréments, il périra sans retour: ceux qui le voyaient diront: "Où est-il?"
iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
8 Comme un songe, il s’envole, et l’on perd ses traces; il s’évanouit comme une vision nocturne.
Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
9 L’Œil qui l’a contemplé ne le découvre plus; sa demeure n’a plus de regard pour lui.
Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
10 Ses fils devront solliciter la pitié des pauvres, et ses propres mains restituer la fortune acquise.
Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
11 Ses membres, tout pleins encore de vigueur juvénile, se verront couchés dans la poussière.
Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
12 S’Il arrive que la perversité soit douce à sa bouche, qu’il la fasse glisser sous sa langue;
“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
13 qu’il la ménage longtemps, ne cessant de la savourer, et la retienne encore au fond de son palais,
ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
14 alors son aliment se transforme dans ses entrailles et devient dans son sein l’amer venin de l’aspic.
koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
15 Il a dévoré une fortune et il faut qu’il la rejette: Dieu l’expulsera de ses intestins.
Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
16 C’Est du poison d’aspic qu’il suçait: il périra par la langue de la vipère.
Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
17 Qu’il n’espère point se délecter aux flots des ruisseaux de miel, des torrents de lait!
Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
18 Il faut qu’il rende le fruit de son labeur, avant de le consommer; il en sera de même des biens qu’il s’est acquis par ses échanges: il n’en tirera aucun plaisir.
Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
19 C’Est qu’il a écrasé les faibles et les a abandonnés à eux-mêmes; il a ruiné des maisons par la rapine et ne les a point rebâties.
Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
20 C’Est qu’il n’a pas connu la paix intérieure: il ne sauvera rien de ses plus chers trésors.
“Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
21 Rien n’échappait à ses appétits; aussi son bien-être n’aura-t-il aucune durée.
Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
22 Alors qu’il regorge de biens, il est dans la gêne; la main de tout misérable s’abattra sur lui.
Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
23 Dieu se dispose à lui bourrer le ventre en lâchant contre lui son ardente colère, en la faisant pleuvoir sur lui en guise de nourriture.
Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
24 II voudra fuir les armes de fer: il sera transpercé par un arc d’airain.
Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
25 La flèche qui l’atteint, il la retire de son corps; elle sort étincelante du foie qu’elle a percé; l’épouvante le saisit.
Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
26 Tous les noirs désastres menacent les trésors qu’il a amassés; un feu que personne n’a attisé le consume et dévore tout ce qui est resté dans sa demeure.
mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
27 Les cieux dénoncent son crime et la terre se soulève contre lui.
Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
28 Les biens de sa maison s’en vont; tout s’écroule au jour de la colère divine.
Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
29 Telle est la part que Dieu réserve à l’homme pervers; tel est l’héritage qui lui est destiné par la parole du Tout-Puissant.
Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”