< Job 19 >

1 Job reprit la parole et dit:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Jusqu’à quand contristerez-vous mon âme et m’accablerez-vous de vos discours?
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 Voilà dix fois que vous m’injuriez; vous ne rougissez pas de me torturer.
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 Mais soit! Admettons que j’aie des torts: ces torts ne pèseraient que sur moi.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 Quant à vous, si vraiment vous prétendez vous grandir à mes dépens et me reprocher la honte où je suis réduit,
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 sachez donc que c’est Dieu qui m’a fait un passe-droit, et qui m’a enveloppé de ses embûches.
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 Quoi! Je crie à la violence et ne trouve point d’écho; j’appelle au secours, et de justice point!
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 Il m’a barré la route, impossible de passer; sur mes sentiers, il a répandu les ténèbres.
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 Il m’a dépouillé de mon honneur; il a enlevé la couronne de ma tête.
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 Il m’a démoli de fond en comble, et je me suis écroulé; il a arraché comme un arbre mon espérance.
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 II a enflammé sa colère contre moi; il m’a traité comme ses ennemis.
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 Ses hordes arrivent en masse, se fraient un chemin contre moi et mettent le siège autour de ma tente.
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 Mes frères, il les a éloignés de moi, mes amis ne sont plus que des étrangers pour moi.
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 Mes proches m’ont délaissé, mes intimes m’ont oublié.
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 Les gens de ma maison, mes propres servantes me considèrent comme un intrus; je suis devenu un inconnu à leurs yeux.
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 J’Appelle mon serviteur: il ne répond pas; je suis obligé de le supplier de ma bouche.
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 Mon haleine est odieuse à ma femme et mes caresses aux fils de mes entrailles,
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 Même de jeunes enfants me montrent leur dédain; quand je veux me lever, ils manifestent contre moi.
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 Tous mes fidèles confidents m’ont pris en horreur, et ceux que j’aimais se sont tournés contre moi.
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 Mes os sont collés à ma peau et à ma chair; je n’ai sauvé du désastre que la peau de mes dents.
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 Ah! Pitié, pitié, vous mes amis! Vous voyez que la main de Dieu m’a frappé.
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Pourquoi me persécutez-vous à l’exemple de Dieu? Pourquoi êtes-vous insatiables de ma chair?
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 Plût à Dieu que mes paroles fussent mises par écrit, qu’elles fussent burinées dans le livre!
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 Qu’avec un stylet de fer et de plomb, elles fussent gravées pour toujours dans le roc!
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 Je sais bien, moi, que mon sauveur vit, et qu’à la fin il se manifestera sur la terre.
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 Après que ma peau, que voilà, sera complètement tombée, libéré de ma chair, je verrai Dieu!
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 Oui, je le contemplerai moi-même pour mon bien, mes yeux le verront, non ceux d’un autre. Mon cœur se consume d’attente dans mon sein.
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 Que si donc vous dites: "Comme nous allons nous acharner contre lui!" le fond du débat tenant à ma personne,
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 eh bien, ayez peur du glaive, car l’emportement dont vous faites preuve est un crime passible du glaive! Ainsi vous apprendrez qu’il y a une justice.
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”

< Job 19 >