< Jérémie 4 >
1 Si tu revenais, ô Israël, dit le Seigneur, revenais à moi, si tu écartais tes abominations loin de ma face, sans plus errer de côté et d’autre,
“Ngati mukufuna kubwerera, inu Aisraeli, bwererani kwa Ine,” akutero Yehova. “Chotsani mafano anu onyansa pamaso panga ndipo musasocherenso.
2 et si tu jurais "par l’Eternel vivant", en vérité, en droiture et justice mais les peuples par lui se diraient heureux, et par lui se diraient glorieux!
Muzilumbira mokhulupirika ndiponso mwa chilungamo kuti, ‘Pali Yehova wamoyo.’ Mukatero anthu a mitundu ina yonse adzandipempha kuti ndiwadalitse ndipo adzanditamanda.”
3 Car c’est ainsi que parle l’Eternel aux gens de Juda et de Jérusalem: "Creusez-vous des sillons, et ne jetez pas vos semences parmi les épines.
Zimene Yehova akunena kwa anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu ndi izi: “Limani masala anu musadzale pakati pa minga.
4 Tâchez de vous circoncire en l’honneur de l’Eternel et d’enlever les excroissances de votre coeur; sans cela ma colère éclatera comme le feu, et brûlera sans qu’on puisse l’éteindre, à cause de la perversité de vos actes."
Dziperekeni nokha kwa Ine kuti munditumikire ndi mtima wanu wonse, inu anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu. Muzichita zimenezi kuopa kuti mkwiyo wanga ungabuke ngati moto ndi kukutenthani, chifukwa cha ntchito zanu zoyipazo popanda wina wowuzimitsa.
5 Annoncez en Juda, proclamez à Jérusalem et dites: "Qu’on fasse retentir la trompette dans le pays! Criez à plein gosier et dites: "Rassemblez-vous, afin de nous retirer dans les villes fortes!"
“Lengeza ku Yuda ndi kulalikira mu Yerusalemu kuti, ‘Lizani lipenga mʼdziko lonse!’ Ndipo fuwulani kuti, ‘Sonkhanani! Tiyeni tithawire ku mizinda yotetezedwa!’
6 Dressez une bannière dans la direction de Sion, fuyez, ne vous arrêtez pas! Car je fais venir du Nord une calamité, une terrible catastrophe.
Kwezani mbendera kuyangʼana ku Ziyoni! Musachedwe, thawani kuti mupulumuke! Pakuti Ine ndikubweretsa chilango kuchokera kumpoto, kudzakhala chiwonongeko choopsa.”
7 Un lion s’est élancé de son hallier, un destructeur de nations s’est mis en route, quittant sa résidence, pour réduire ton pays en ruine; tes villes deviendront des solitudes inhabitées.
Monga mkango umatulukira mʼngaka yake momwemonso wowononga mayiko wanyamuka ndi kutuluka ku mbuto yake. Watero kuti awononge dziko lanu. Mizinda yanu idzakhala mabwinja popanda wokhalamo.
8 C’Est pourquoi ceignez-vous de cilices, exhalez votre douleur, lamentez-vous, puisque le feu de la colère divine ne se détourne pas de nous.
Choncho valani ziguduli, lirani ndi kubuwula, pakuti mkwiyo waukulu wa Yehova sunatichokere.
9 En ce jour, il arrivera, dit l’Eternel, que le coeur du roi et le coeur des chefs seront éperdus; atterrés seront les prêtres et stupéfaits les prophètes.
“Pa tsiku limenelo, mfumu ndi nduna zake adzataya mtima, ansembe adzachita mantha kwambiri, ndipo aneneri adzathedwa nzeru,” akutero Yehova.
10 Et je m’écriai: "Eh quoi! Eternel Dieu! Ainsi donc tu aurais complètement leurré ce peuple et Jérusalem, quand tu disais: "Vous obtiendrez la paix!—Et le glaive pénètre jusqu’à l’âme!
Ndipo ine ndinati, “Haa, Ambuye Yehova, ndithu munawanyenga anthu awa pamodzi ndi Yerusalemu pamene munanena kuti, ‘Mudzakhala pa mtendere,’ chonsecho lupanga lili pakhosi pathu.”
11 En ce temps-là, on dira à ce peuple et à Jérusalem: "II y a un vent embrasé sur les hauteurs dans le désert, venant dans la direction de la fille de mon peuple, mais ne servant ni à vanner ni à épurer le grain.
Nthawi imeneyo anthu awa ndi Yerusalemu adzawawuza kuti, “Mphepo yotentha yochokera ku magomo a mʼchipululu ikuwomba pa anthu anga, osati mphepo yopeta kapena yoyeretsa;
12 Un souffle violent m’arrive de là; maintenant je vais, moi aussi, prononcer l’arrêt contre eux.
koma mphepo yamphamvu kwambiri yochokera kwa Ine. Tsono ndi Ineyo amene ndikuwaweruza.”
13 Voici, il s’élance comme les nuages; ses chars ressemblent à l’ouragan, ses chevaux sont plus rapides que les aigles. Malheur à nous! Car nous sommes, saccagés.
Taonani, adani akubwera ngati mitambo, magaleta awo akubwera ngati kamvuluvulu, akavalo awo ndi aliwiro kupambana chiwombankhanga. Tsoka ilo! Tawonongeka!
14 O Jérusalem, lave ton coeur de toute perversité pour être sauvée: jusqu’à quand logeras-tu dans ton sein tes pensées criminelles?
Iwe Yerusalemu, tsuka mtima wako kuchotsa zoyipa kuti upulumuke. Kodi maganizo ako oyipawo udzakhala nawo mpaka liti?
15 Car une voix se fait entendre de Dan et annonce la calamité depuis la montagne d’Ephraïm.
Pakuti amithenga akulalika mawu mʼdziko la Dani; akulengeza za masautso kuchokera ku mapiri a Efereimu.
16 "Faites-le savoir aux nations, allons, apprenez-le à Jérusalem, que des assiégeants arrivent d’un pays lointain et poussent des clameurs contre les villes de Juda!"
Iwo akuti, “Fotokozani zimenezi kwa anthu a mitundu ina, lengezani zimenezi mu Yerusalemu kuti, ‘Ankhondo akubwera kuchokera ku dziko lakutali, akufuwula ndi kudzazinga mizinda ya Yuda.
17 Comme les gardiens des champs, ils l’enserrent de tous côtés, parce qu’elle s’est révoltée contre moi, dit l’Eternel.
Azinga Yerusalemu ngati anthu olondera munda, chifukwa Yerusalemu wandiwukira,’” akutero Yehova.
18 C’Est ta conduite, ce sont tes actes qui t’ont valu cela; de là ton malheur, qui est si amer, car il t’atteint jusqu’au coeur.
“Makhalidwe anu ndi zochita zanu zakubweretserani zimenezi. Chimenechi ndiye chilango chanu. Nʼchowawa kwambiri! Nʼcholasa mpaka mu mtima!”
19 O mes entrailles, mes entrailles! Je frémis jusqu’au fond de mon coeur! Tout mon coeur est en émoi, je ne puis le calmer; car tu entends, ô mon âme, le son de la trompette. Les fanfares belliqueuses.
Mayo, mayo, ndikumva kupweteka! Aa, mtima wanga ukupweteka, ukugunda kuti thi, thi, thi. Sindingathe kukhala chete. Pakuti ndamva kulira kwa lipenga; ndamva mfuwu wankhondo.
20 On annonce désastres sur désastres, que tout le pays est saccagé; mes tentes ont été saccagées soudainement, mes pavillons en un clin d’oeil.
Tsoka limatsata tsoka linzake; dziko lonse lasanduka bwinja. Mwadzidzidzi matenti athu awonongedwa, mwa kanthawi kochepa nsalu zake zotchinga zagwetsedwa.
21 Jusqu’à quand verrai-je des bannières? Entendrai-je les trompettes retentissantes?
Kodi ndikhale ndikuona mbendera ya nkhondo, ndi kumva kulira kwa lipenga mpaka liti?
22 Certes, mon peuple est dénué de raison, ils ne me connaissent pas; ce sont des enfants insensés, sans aucun discernement, intelligents seulement pour mal faire, incapables de faire le bien.
Yehova akuti, “Anthu anga ndi zitsiru; iwo sandidziwa. Iwo ndi ana opanda nzeru; samvetsa chilichonse. Ali ndi luso lochita zoyipa, koma sadziwa kuchita zabwino.”
23 J’Ai regardé la terre, et voici tout y était chaos informe; et vers les cieuxleur lumière avait disparu.
Ndinayangʼana dziko lapansi, ndipo linali lopanda anthu ndi lopanda kanthu; ndinayangʼana thambo, koma linalibe kuwala kulikonse.
24 J’Ai regardé les montagnes, elles étaient tremblantes; toutes les collineselles étaient violemment agitées.
Ndinayangʼana mapiri, ndipo ankagwedezeka; magomo onse ankangosunthira uku ndi uku.
25 J’Ai regardé et voici, il n’y avait plus d’hommes, et tous les oiseaux du ciel avaient pris leur vol.
Ndinayangʼana, ndipo sindinaone anthu; mbalame iliyonse ya mlengalenga inali itathawa.
26 J’Ai regardé et voici, la campagne fertile était devenue un désert, et toutes ses villes étaient renversées par l’action de l’Eternel, par le feu de sa colère.
Ndinayangʼana, dziko lachonde linali litasanduka chipululu; mizinda yake yonse inali itasanduka bwinja pamaso pa Yehova, chifukwa cha mkwiyo wake.
27 Oui, ainsi parle l’Eternel: "Tout le pays deviendra une solitude, bien que je ne consomme pas la ruine."
Yehova akuti, “Dziko lonse lidzasanduka chipululu komabe sindidzaliwononga kotheratu.
28 C’Est pour cette raison que la terre est en deuil, et les cieux là-haut sont ténébreux, parce que j’ai annoncé ce que j’ai résolu et que je n’entends ni me raviser ni me rétracter.
Chifukwa chake dziko lapansi lidzalira ndipo thambo lidzachita mdima, pakuti ndayankhula ndipo sindidzafewa mtima, ndatsimikiza ndipo sindidzabwerera mʼmbuyo.”
29 Devant la clameur des cavaliers et des archers, toute la ville est en fuite; on pénètre dans les fourrés, on escalade les rochers; toute ville est abandonnée, pas un homme n’y reste.
Pakumva phokoso la okwera pa akavalo ndi la anthu oponya mivi, anthu a mʼmizinda adzathawa. Ena adzabisala ku nkhalango; ena adzakwera mʼmatanthwe mizinda yonse nʼkuyisiya; popanda munthu wokhalamo.
30 Et toi, si complètement ruinée, que vas-tu faire? Tu aurais beau te vêtir de pourpre, te parer de tes bijoux d’or, allonger tes yeux au moyen du fard: vainement tu te ferais belle, les amoureux te dédaignent, c’est à ta vie qu’ils en veulent.
Iwe Yerusalemu, ndiwe bwinja! Ukutanthauza chiyani kuvala zovala zofiira ndi kuvalanso zokometsera zagolide? Ngakhale udzikonze maso ako powapaka zokometsera, ukungodzivuta chabe. Zibwenzi zako zikukunyoza; zikufuna kuchotsa moyo wako.
31 Car j’entends des plaintes comme celles d’une femme en travail, des cris d’angoisse comme ceux d’une mère mettant au monde son premier-né: c’est la voix de Sion qui exhale des soupirs, qui se tord les bras: "Malheur à moi, mon âme est à bout de force devant les meurtriers!"
Ndikumva kulira ngati kwa mayi pa nthawi yake yobereka, kubuwula ngati kwa mayi amene akubereka mwana wake woyamba. Kuliraku ndi kwa anthu a mu Ziyoni, wefuwefu. Atambalitsa manja awo nʼkumati, “Kalanga ife! Tikukomoka. Moyo wathu waperekedwa kwa anthu otipha.”