< Isaïe 3 >

1 Voyez, l’Eternel-Cebaot enlève à Jérusalem et à Juda tout appui et tout soutien, toute ressource en pain et toute ressource en eau;
Taonani tsopano, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda zinthu pamodzi ndi thandizo; adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,
2 héros et hommes de guerre, juges et prophètes, devins et anciens;
anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo, oweruza ndi aneneri, anthu olosera ndi akuluakulu,
3 chefs militaires et gens considérés, conseillers ainsi qu’artisans experts et habiles enchanteurs.
atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka, aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.
4 Je leur donnerai des jeunes gens comme maîtres, et des écervelés domineront sur eux.
Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo; ana akhanda ndiwo adzawalamulire.
5 Chez ce peuple, l’un usera de sévices contre l’autre, chacun contre chacun; le jouvenceau sera arrogant envers le vieillard, l’homme de rien envers le plus respectable.
Anthu adzazunzana, munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake. Anthu wamba adzanyoza akuluakulu.
6 Que si quelqu’un exerce une pression sur un parent dans la maison paternelle en disant: "Tu possèdes un manteau, consens donc à être notre chef, à soutenir de ta main cet édifice chancelant;"
Munthu adzagwira mʼbale wake mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati, “Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu; lamulira malo opasuka ano!”
7 celui-ci protestera en ce jour par ces paroles: "Non, je ne puis être votre sauveur, alors que, dans ma maison, il n’y a ni pain ni vêtement; ne m’érigez pas en chef de ce peuple"
Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti, “Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake. Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga; musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”
8 Oui, Jérusalem a trébuché, Juda est tombé; car leurs paroles et leurs actes sont dirigés contre l’Eternel et bravent ses regards augustes.
Yerusalemu akudzandira, Yuda akugwa; zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova, sakulabadira ulemerero wa Mulungu.
9 L’Impudence de leur visage témoigne contre eux, ils affichent leur crime à l’exemple de Sodome et ne dissimulent rien. Malheur à eux! Ils se sont préparés eux-mêmes la ruine.
Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa; amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu; salibisa tchimo lawolo. Tsoka kwa iwo odziputira okha mavuto.
10 Annoncez au juste qu’il sera heureux et jouira du fruit de ses œuvres.
Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino, pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.
11 Mais hélas! le malheur atteindra le méchant, car il sera traité selon l’œuvre de ses mains.
Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo! Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.
12 Mon peuple, des enfants le pressurent, et des femmes le tyrannisent; ô mon peuple, ce sont tes guides qui t’égarent et qui détruisent la trace de tes routes.
Achinyamata akupondereza anthu anga, ndipo amene akuwalamulira ndi akazi. Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani; akukuchotsani pa njira yanu.
13 L’Eternel s’avance pour faire justice; il se présente pour juger les peuples;
Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu; wakonzeka kuti aweruze anthu ake.
14 il vient demander raison aux anciens de son peuple et à ses princes: "C’Est vous qui avez dévoré la vigne, entassé dans vos maisons les dépouilles des pauvres.
Yehova akuwazenga milandu akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake: “Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa; nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.
15 De quel droit écrasez-vous mon peuple et broyez-vous la face des indigents?" Ainsi parle le Seigneur, l’Eternel-Cebaot.
Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga, nʼkudyera masuku pamutu amphawi?” Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
16 L’Eternel dit encore: "Puisque les filles de Sion sont si arrogantes, s’avançant le cou dressé, lançant des regards provocants, puisqu’elles marchent à pas mesurés et font sonner les clochettes de leurs pieds,
Yehova akunena kuti, “Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri, akuyenda atakweza makosi awo, akukopa amuna ndi maso awo akuyenda monyangʼama akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo
17 le Seigneur dépouillera la tête des filles de Sion et mettra à nu leur honte."
Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo; Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”
18 En ce jour, le Seigneur supprimera le luxe des clochettes, les filets et les croissants;
Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi,
19 les pendants d’oreilles, les bracelets et les voiles;
ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope,
20 les diadèmes, les chaînettes des pieds, les ceintures, les boîtes à parfums et les amulettes;
maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa,
21 les bagues et les anneaux du nez;
mphete ndi zipini,
22 les vêtements de fête, les manteaux, les écharpes et les sachets;
zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama,
23 les miroirs, les fines tuniques, les turbans et les surtouts…
magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa.
24 Au lieu de parfums il y aura de la pourriture; au lieu de ceinture, une corde; au lieu de nattes bien tressées, de la calvitie; au lieu d’un large manteau, un cilice; des stigmates de brûlure remplaceront la beauté.
Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha, mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe; mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi; mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli; mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.
25 Tes hommes de guerre tomberont sous le glaive et tes vaillants succomberont dans les combats.
Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga, asilikali ako adzafera ku nkhondo.
26 Une morne tristesse envahira les portes de la ville; Sion, complètement dépouillée, s’assoira à terre.
Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira; Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.

< Isaïe 3 >