< Isaïe 2 >

1 Révélation que reçut Isaïe, fils d’Amoç, sur Juda et Jérusalem:
Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:
2 Il arrivera, à la fin des temps, que la montagne de la maison du Seigneur sera affermie sur la cime des montagnes et se dressera au-dessus des collines, et toutes les nations y afflueront.
Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse, lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.
3 Et nombre de peuples iront en disant: "Or çà, gravissons la montagne de l’Eternel pour gagner la maison du Dieu de Jacob, afin qu’il nous enseigne ses voies et que nous puissions suivre ses sentiers, car c’est de Sion que sort la doctrine et de Jérusalem la parole du Seigneur."
Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
4 Il sera un arbitre entre les nations et le précepteur de peuples nombreux; ceux-ci alors de leurs glaives forgeront des socs de charrue et de leurs lances des serpettes; un peuple ne tirera plus l’épée contre un autre peuple, et on n’apprendra plus l’art des combats.
Iye adzaweruza pakati pa mayiko, ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
5 Maison de Jacob, allons, marchons à la lumière de l’Eternel.
Inu nyumba ya Yakobo, bwerani, tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.
6 Certes, tu avais délaissé ton peuple, la maison de Jacob, car ils étaient envahis de superstitions venues de l’Orient, de pratiques de sorcellerie comme les Philistins, ils se complaisaient aux produits des étrangers.
Inu Yehova mwawakana anthu anu, nyumba ya Yakobo. Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa; amawombeza mawula ngati Afilisti, ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
7 Leur pays est gorgé d’argent et d’or, point de limites à leurs trésors; il abonde en chevaux, et ses chars ne se comptent point.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide; ndipo chuma chawo ndi chosatha. Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo; ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
8 Leur pays est rempli aussi d’idoles, ils se prosternent devant l’œuvre de leurs mains, devant les créations de leurs doigts.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano; iwo amapembedza ntchito ya manja awo, amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
9 Toute personne s’est abaissée, tout homme s’est dégradé: tu ne peux leur pardonner.
Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa ndi kutsitsidwa. Inu Yehova musawakhululukire.
10 Qu’on se retire dans les rochers, qu’on cherche un abri dans la poussière, devant la terreur qu’inspire Dieu et l’éclat de sa majesté!
Lowani mʼmatanthwe, bisalani mʼmaenje, kuthawa kuopsa kwa Yehova ndi ulemerero wa ufumu wake!
11 Les yeux hautains seront abaissés, l’orgueil humain sera humilié: Dieu seul sera grand en ce jour.
Kudzikuza kwa anthu kudzatha, ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa; Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.
12 Oui, l’Eternel-Cebaot fixera un jour contre l’orgueilleux et le superbe, contre quiconque s’élève: ils seront abaissés;
Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama, ndipo adzagonjetsa onse amphamvu,
13 contre tous les cèdres élancés et majestueux du Liban et les chênes du Basan;
tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali, ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
14 contre toutes les hautes montagnes et les collines altières;
tsiku la mapiri onse ataliatali ndiponso la zitunda zonse zazitali,
15 contre les tours élevées et les remparts puissants;
tsiku la nsanja zonse zazitali ndiponso malinga onse olimba,
16 et contre les navires de Tarsis et les édifices somptueux.
tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi ndiponso la mabwato onse okongola.
17 L’Orgueil des hommes sera humilié, leur arrogance sera abattue; seul l’Eternel sera grand en ce jour.
Kudzikuza kwa munthu kudzatha ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa, Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
18 Quant aux idoles, elles s’évanouiront toutes.
ndipo mafano onse adzatheratu.
19 On se réfugiera alors dans les cavités des rochers et dans les grottes souterraines devant la terreur répandue par l’Eternel et l’éclat de sa majesté, quand il se lèvera pour épouvanter la terre.
Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndi mʼmaenje a nthaka, kuthawa mkwiyo wa Yehova, ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
20 En ce jour, ils jetteront aux taupes et aux chauves-souris leurs idoles d’argent et d’or, qu’ils avaient fabriquées pour leur rendre hommage,
Tsiku limenelo anthu adzatayira mfuko ndi mileme mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide, amene anawapanga kuti aziwapembedza.
21 et ils iront dans le creux des rochers, dans les crevasses des côtes pierreuses, terrifiés par la crainte de l’Eternel et l’éclat de sa majesté, quand il se lèvera pour épouvanter la terre.
Adzathawira mʼmapanga a matanthwe ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka kuthawa mkwiyo wa Yehova ndiponso ulemerero wa ufumu wake, pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
22 Cessez de vous appuyer sur l’homme, dont la vie n’est qu’un souffle. Quelle peut être sa valeur?
Lekani kudalira munthu, amene moyo wake sukhalira kutha. Iye angathandize bwanji wina aliyense?

< Isaïe 2 >