< Psaumes 20 >
1 Au maître de chant. Psaume de David. Que Yahweh t’exauce au jour de la détresse, que le nom du Dieu de Jacob te protège!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
2 Que du sanctuaire il t’envoie du secours, que de Sion il te soutienne!
Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
3 Qu’il se souvienne de toutes tes oblations, et qu’il ait pour agréable tes holocaustes! — Séla.
Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
4 Qu’il te donne ce que ton cœur désire, et qu’il accomplisse tous tes desseins!
Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
5 Puissions-nous de nos cris joyeux saluer ta victoire, lever l’étendard au nom de notre Dieu! Que Yahweh accomplisse tous tes vœux!
Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
6 Déjà je sais que Yahweh a sauvé son Oint; il l’exaucera des cieux, sa sainte demeure, par le secours puissant de sa droite.
Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
7 Ceux-ci comptent sur leurs chars, ceux-là sur leurs chevaux; nous, nous invoquons le nom de Yahweh, notre Dieu.
Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
8 Eux, ils plient et ils tombent; nous, nous nous relevons et tenons ferme.
Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
9 Yahweh, sauve le roi! — Qu’il nous exauce au jour où nous l’invoquons.
Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!