< Psaumes 18 >

1 Au maître de chant. Psaume du serviteur de Yahweh, de David, qui adressa à Yahweh les paroles de ce cantique, au jour où Yahweh l’eut délivré de la main de tous ses ennemis et de la main de Saül. Il dit: Je t’aime, Yahweh, ma force!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
2 Yahweh mon rocher, ma forteresse, mon libérateur, mon Dieu, mon roc où je trouve un asile, mon bouclier, la corne de mon salut, ma citadelle!
Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
3 J’invoquai celui qui est digne de louange, Yahweh, et je fus délivré de mes ennemis.
Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
4 Les liens de la mort m’environnaient, les torrents de Bélial m’épouvantaient,
Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
5 les liens du schéol m’enlaçaient, les filets de la mort étaient tombés devant moi. (Sheol h7585)
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
6 Dans ma détresse, j’invoquai Yahweh, et je criai vers mon Dieu; de son temple il entendit ma voix, et mon cri devant lui parvint à ses oreilles.
Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
7 La terre fut ébranlée et trembla, les fondements des montagnes s’agitèrent, et ils furent ébranlés, parce qu’il était courroucé;
Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
8 une fumée montait de ses narines, et un feu dévorant sortait de sa bouche; il en jaillissait des charbons embrasés.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
9 il abaissa les cieux, et descendit; une sombre nuée était sous ses pieds.
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
10 Il monta sur un Chérubin, et il volait; il planait sur les ailes du vent.
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
11 Il fit des ténèbres sa retraite, sa tente autour de lui c’étaient des eaux obscures et de sombres nuages.
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
12 De l’éclat qui le précédait s’élancèrent ses nuées, portant la grêle et les charbons ardents.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
13 Yahweh tonna dans les cieux, le Très-Haut fit retentir sa voix: grêle et charbons ardents!
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
14 Il lança ses flèches et les dispersa; il multiplia ses foudres et il les confondit.
Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
15 Alors le lit des eaux apparut, les fondements de la terre furent mis à nu, à ta menace, Yahweh, au souffle du vent de tes narines.
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
16 Il étendit sa main d’en haut et me saisit, il me retira des grandes eaux.
Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
17 Il me délivra de mon ennemi puissant, de ceux qui me haïssaient, alors qu’ils étaient plus forts que moi.
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
18 Ils m’avaient surpris au jour de mon malheur; mais Yahweh fut mon appui.
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
19 Il m’a mis au large, il m’a sauvé, parce qu’il s’est complu en moi.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
20 Yahweh m’a récompensé selon ma justice, il m’a rendu selon la pureté de mes mains.
Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
21 Car j’ai gardé les voies de Yahweh, et je n’ai pas péché, pour m’éloigner de mon Dieu.
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
22 Tous ses jugements étaient devant moi, et je n’ai pas rejeté loin de moi ses lois.
Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
23 J’étais sans reproche envers lui, et je me tenais en garde contre mon iniquité.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
24 Yahweh m’a rendu selon ma justice, selon la pureté de mes mains devant ses yeux.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
25 Avec celui qui est bon tu te montres bon, avec l’homme droit tu te montres droit;
Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
26 avec celui qui est pur tu te montres pur, et avec le fourbe tu agis perfidement.
kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
27 Car tu sauves le peuple humilié, et tu abaisses les regards hautains.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
28 Oui, tu fais briller mon flambeau; Yahweh, mon Dieu, éclaire mes ténèbres.
Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
29 Avec toi je me précipite sur les bataillons armés; avec mon Dieu je franchis les murailles.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
30 Dieu!... Ses voies sont parfaites; la parole de Yahweh est éprouvée, il est un bouclier pour tous ceux qui se confient en lui.
Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
31 Car qui est Dieu, si ce n’est Yahweh, et qui est un rocher, si ce n’est notre Dieu?
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
32 Le Dieu qui me ceint de force, qui rend ma voie parfaite;
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
33 qui rend mes pieds semblables à ceux des biches, et me fait tenir debout sur mes hauteurs;
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
34 qui forme mes mains au combat, et mes bras tendent l’arc d’airain.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
35 Tu m’as donné le bouclier de ton salut, et ta droite me soutient, et ta douceur me fait grandir.
Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
36 Tu élargis mon pas au-dessous de moi, et mes pieds ne chancellent point.
Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
37 Je poursuis mes ennemis et je les atteins; je ne reviens pas sans les avoir anéantis.
Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
38 Je les brise, et ils ne se relèvent pas; Ils tombent sous mes pieds.
Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
39 Tu me ceins de force pour le combat, tu fais plier sous moi mes adversaires.
Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
40 Mes ennemis!... tu leur fais tourner le dos devant moi, et j’extermine ceux qui me haïssent.
Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
41 Ils crient, et personne pour les sauver! Ils crient vers Yahweh, et il ne leur répond pas!
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
42 Je les broie comme la poussière livrée au vent, je les balaie comme la boue des rues.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
43 Tu me délivres des révoltes du peuple, tu me mets à la tête des nations; Des peuples que je ne connaissais pas me sont asservis.
Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
44 Dès qu’ils ont entendu, ils m’obéissent; les fils de l’étranger me flattent.
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
45 Les fils de l’étranger sont défaillants, ils sortent tremblants de leurs forteresses.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
46 Vive Yahweh et béni soit mon rocher! Que le Dieu de mon salut soit exalté;
Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
47 Dieu qui m’accorde des vengeances, qui me soumet les peuples,
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
48 qui me délivre de mes ennemis! Oui, tu m’élèves au-dessus de mes adversaires, tu me sauves de l’homme de violence.
amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
49 C’est pourquoi je te louerai parmi les nations, ô Yahweh; je chanterai à la gloire de ton nom:
Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
50 Il accorde de glorieuses délivrances à son roi, il fait miséricorde à son oint, à David et à sa postérité pour toujours.
Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.

< Psaumes 18 >