< Psaumes 105 >
1 Rendez grâce à Yahvé! Invoquez son nom! Faites connaître ses actions parmi les peuples.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 Chantez-lui, chantez-lui des louanges! Racontez toutes ses œuvres merveilleuses.
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 Gloire à son saint nom. Que le cœur de ceux qui cherchent Yahvé se réjouisse.
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Recherchez Yahvé et sa force. Cherchez son visage pour toujours.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Rappelez-vous les merveilles qu'il a faites: ses merveilles, et les jugements de sa bouche,
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 vous, descendants d'Abraham, son serviteur, vous, enfants de Jacob, ses élus.
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 Il est Yahvé, notre Dieu. Ses jugements sont dans toute la terre.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 Il s'est souvenu de son alliance pour toujours, la parole qu'il a commandée à mille générations,
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 l'alliance qu'il a conclue avec Abraham, son serment à Isaac,
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 et l'a confirmé à Jacob pour une loi; à Israël pour une alliance éternelle,
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 en disant: « Je vous donnerai le pays de Canaan, le lot de votre héritage, »
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 alors qu'ils n'étaient qu'un petit nombre d'hommes, oui, très peu, et des étrangers en son sein.
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 Ils allaient de nation en nation, d'un royaume à un autre peuple.
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 Il n'a permis à personne de leur faire du mal. Oui, il a réprimandé les rois pour leur bien,
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 « Ne touchez pas à mes oints! Ne faites pas de mal à mes prophètes! »
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 Il a appelé la famine sur le pays. Il a détruit les réserves de nourriture.
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 Il envoya un homme devant eux. Joseph a été vendu comme esclave.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 On lui a meurtri les pieds avec des entraves. Son cou a été mis aux fers,
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 jusqu'au moment où sa parole s'est accomplie, et la parole de Yahvé lui a donné raison.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 Le roi l'envoya et le libéra, même le chef des peuples, et le laisser libre.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 Il l'a fait seigneur de sa maison, et le maître de toutes ses possessions,
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 pour discipliner ses princes à son gré, et d'enseigner la sagesse à ses aînés.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 Israël aussi est venu en Égypte. Jacob a vécu dans le pays de Ham.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 Il a beaucoup augmenté son peuple, et les a rendus plus forts que leurs adversaires.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 Il a détourné leur cœur pour qu'ils haïssent son peuple, pour conspirer contre ses serviteurs.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 Il envoya Moïse, son serviteur, et Aaron, qu'il avait choisi.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 Ils faisaient des miracles au milieu d'eux, et des merveilles dans le pays de Ham.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 Il a envoyé les ténèbres, et il a rendu les ténèbres. Ils ne se sont pas rebellés contre ses paroles.
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 Il a changé leurs eaux en sang, et ont tué leurs poissons.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 Leur terre grouillait de grenouilles, même dans les chambres de leurs rois.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 Il parla, et des nuées de mouches vinrent, et des poux dans toutes leurs frontières.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 Il leur a donné de la grêle en guise de pluie, avec des éclairs dans leur pays.
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 Il a frappé leurs vignes et aussi leurs figuiers, et ont brisé les arbres de leur pays.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 Il parla, et les sauterelles vinrent avec les sauterelles, sans nombre.
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 Ils ont dévoré toutes les plantes de leur pays, et ont mangé le fruit de leur sol.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 Il frappa aussi tous les premiers-nés de leur pays, les premiers fruits de toute leur virilité.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 Il les fit sortir avec de l'argent et de l'or. Il n'y avait pas une seule personne faible parmi ses tribus.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 L'Égypte se réjouit de leur départ, car la peur d'eux était tombée sur eux.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 Il a étendu un nuage pour le couvrir, le feu pour donner de la lumière dans la nuit.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 Ils ont demandé, et il a apporté des cailles, et les a rassasiés avec le pain du ciel.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 Il ouvrit le rocher, et des eaux jaillirent. Ils coulaient comme un fleuve dans les endroits secs.
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 Car il s'est souvenu de sa sainte parole, et Abraham, son serviteur.
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 Il a fait sortir son peuple avec joie, son choix avec le chant.
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 Il leur a donné les terres des nations. Ils ont pris le travail des peuples en possession,
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 afin qu'ils gardent ses statuts, et observez ses lois. Louez Yah!
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.