< Psaumes 104 >

1 Bénis Yahvé, mon âme. Yahvé, mon Dieu, tu es très grand. Tu es vêtu d'honneur et de majesté.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
2 Il se couvre de lumière comme d'un vêtement. Il étend les cieux comme un rideau.
Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
3 Il pose les poutres de ses chambres dans les eaux. Il fait des nuages son char. Il marche sur les ailes du vent.
ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
4 Il fait de ses messagers des vents, et ses serviteurs des flammes de feu.
Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
5 Il a posé les fondations de la terre, qu'il ne devrait pas être déplacé pour toujours.
Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
6 Tu l'as couvert de l'abîme comme d'un manteau. Les eaux s'élevaient au-dessus des montagnes.
Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
7 A ta réprimande, ils se sont enfuis. À la voix de votre tonnerre, ils se sont précipités.
Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
8 Les montagnes se sont élevées, les vallées se sont effondrées, à la place que vous leur aviez assignée.
Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
9 Tu as fixé une frontière qu'ils ne pourront pas franchir, qu'ils ne se retournent pas pour recouvrir la terre.
Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
10 Il fait jaillir des sources dans les vallées. Ils courent entre les montagnes.
Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
11 Ils donnent à boire à tous les animaux des champs. Les ânes sauvages étanchent leur soif.
Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
12 Les oiseaux du ciel font leur nid près d'eux. Ils chantent parmi les branches.
Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
13 Il arrose les montagnes depuis ses chambres. La terre est remplie du fruit de tes œuvres.
Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
14 Il fait pousser l'herbe pour le bétail, et des plantes que l'homme peut cultiver, pour qu'il produise de la nourriture à partir de la terre:
Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
15 le vin qui réjouit le cœur de l'homme, de l'huile pour faire briller son visage, et le pain qui fortifie le cœur de l'homme.
vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
16 Les arbres de Yahvé sont bien arrosés, les cèdres du Liban, qu'il a plantés,
Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
17 où les oiseaux font leurs nids. La cigogne a élu domicile dans les cyprès.
Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
18 Les hautes montagnes sont pour les boucs sauvages. Les rochers sont un refuge pour les blaireaux des rochers.
Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
19 Il a établi la lune pour les saisons. Le soleil sait quand se coucher.
Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
20 Tu fais des ténèbres, et c'est la nuit, dans lequel tous les animaux de la forêt rôdent.
Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
21 Les jeunes lions rugissent après leur proie, et cherchent leur nourriture auprès de Dieu.
Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
22 Le soleil se lève, et ils s'enfuient, et se couchent dans leurs tanières.
Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
23 L'homme se rend à son travail, à son travail jusqu'au soir.
Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
24 Yahvé, que tes œuvres sont nombreuses! Dans la sagesse, vous les avez tous créés. La terre est pleine de vos richesses.
Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
25 Voilà la mer, grande et large, dans laquelle se trouvent d'innombrables êtres vivants, les petits et les grands animaux.
Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
26 C'est là que vont les navires, et leviathan, que vous avez formé pour y jouer.
Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
27 Ils t'attendent tous, afin que vous leur donniez leur nourriture en temps voulu.
Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
28 Tu leur donnes, ils recueillent. Vous ouvrez votre main; ils sont satisfaits du bien.
Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
29 Vous cachez votre visage, ils sont troublés. Vous leur coupez le souffle, ils meurent et retournent à la poussière.
Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
30 Tu envoies ton Esprit et ils sont créés. Vous renouvelez la surface du sol.
Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
31 Que la gloire de Yahvé dure à jamais. Que Yahvé se réjouisse de ses œuvres.
Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
32 Il regarde la terre, et elle tremble. Il touche les montagnes, et elles fument.
Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
33 Je chanterai à Yahvé aussi longtemps que je vivrai. Je chanterai les louanges de mon Dieu tant que j'ai un être.
Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
34 Que ma méditation lui soit douce. Je me réjouirai en Yahvé.
Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
35 Que les pécheurs disparaissent de la terre! Que les méchants ne soient plus. Bénis Yahvé, mon âme. Louez Yah!
Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.

< Psaumes 104 >