< Psalms 95 >

1 Come, we sing to Jehovah, We shout to the rock of our salvation.
Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe, tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
2 We come before His face with thanksgiving, With psalms we shout to Him.
Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.
3 For a great God [is] Jehovah, And a great king over all gods.
Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu, mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
4 In whose hand [are] the deep places of earth, And the strong places of hills [are] His.
Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi, ndipo msonga za mapiri ndi zake.
5 Whose is the sea, and He made it, And His hands formed the dry land.
Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye, ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.
6 Come in, we bow ourselves, and we bend, We kneel before Jehovah our Maker.
Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira, tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
7 For He [is] our God, and we the people of His pasture, And the flock of His hand, To-day, if to His voice ye hearken,
pakuti Iye ndiye Mulungu wathu ndipo ife ndife anthu a pabusa pake, ndi nkhosa za mʼdzanja lake. Lero ngati inu mumva mawu ake,
8 Harden not your heart as [in] Meribah, As [in] the day of Massah in the wilderness,
musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba, monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
9 Where your fathers have tried Me, Have proved Me, yea, have seen My work.
Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa, ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
10 Forty years I am weary of the generation, And I say, 'A people erring in heart — they! And they have not known My ways:'
Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo; ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera ndipo sanadziwe njira zanga.”
11 Where I sware in Mine anger, 'If they come in unto My rest —!'
Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti, “Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”

< Psalms 95 >