< Psalms 65 >

1 `To victorie, `the salm of the song of Dauid. God, heriyng bicometh thee in Syon; and a vow schal be yolden to thee in Jerusalem.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo. Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni; kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
2 Here thou my preier; ech man schal come to thee.
Inu amene mumamva pemphero, kwa inu anthu onse adzafika.
3 The wordis of wickid men hadden the maistrye ouer vs; and thou schalt do merci to oure wickidnessis.
Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo, Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
4 Blessid is he, whom thou hast chose, and hast take; he schal dwelle in thin hallis. We schulen be fillid with the goodis of thin hous;
Odala iwo amene inu muwasankha ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu! Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu, za mʼNyumba yanu yoyera.
5 thi temple is hooli, wondurful in equite. God, oure heelthe, here thou vs; thou art hope of alle coostis of erthe, and in the see afer.
Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo, Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
6 And thou makest redi hillis in thi vertu, and art gird with power;
amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu, mutadziveka nokha ndi mphamvu.
7 which disturblist the depthe of the see, the soun of the wawis therof.
Amene munakhalitsa bata nyanja kukokoma kwa mafunde ake, ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
8 Folkis schulen be disturblid, and thei that dwellen in the endis schulen drede of thi signes; thou schalt delite the outgoingis of the morewtid and euentid.
Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu; kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera. Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.
9 Thou hast visitid the lond, and hast greetli fillid it; thou hast multiplied to make it riche. The flood of God was fillid with watris; thou madist redi the mete of hem, for the makyng redi therof is so.
Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira; Inuyo mumalilemeretsa kwambiri. Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi kuti upereke tirigu kwa anthu, pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
10 Thou fillynge greetli the stremes therof, multiplie the fruytis therof; the lond bringinge forth fruytis schal be glad in goteris of it.
Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake, mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
11 Thou schalt blesse the coroun of the yeer of thi good wille; and thi feeldis schulen be fillid with plentee of fruytis.
Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka, ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
12 The feire thingis of desert schulen wexe fatte; and litle hillis schulen be cumpassid with ful out ioiyng.
Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira; mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
13 The wetheris of scheep ben clothid, and valeis schulen be plenteuouse of wheete; thei schulen crye, and sotheli thei schulen seye salm.
Madambo akutidwa ndi zoweta ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu; izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.

< Psalms 65 >