< Psalms 64 >

1 `In Ebrewe thus, To the victorie, the salm of Dauid. `In Jerom `thus, To the ouercomer, the song of Dauid. God, here thou my preier, whanne Y biseche; delyuere thou my soule fro the drede of the enemy.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Ndimvereni Mulungu pomwe ndikunena madandawulo anga; tetezani moyo wanga ku chiopsezo cha mdani.
2 Thou hast defendid me fro the couent of yuele doers; fro the multitude of hem that worchen wickidnesse.
Ndibiseni ku chiwembu cha anthu oyipa, ku gulu laphokoso la anthu ochita zoyipa.
3 For thei scharpiden her tungis as a swerd, thei benten a bowe, a bittir thing;
Iwo amanola malilime awo ngati malupanga, amaponya mawu awo olasa ngati mivi.
4 for to schete in priuetees hym that is vnwemmed.
Iwo amaponya mivi yawo ali pa malo wobisala kwa munthu wosalakwa; amamulasa modzidzimutsa ndi mopanda mantha.
5 Sodeynli thei schulen schete hym, and thei schulen not drede; thei maden stidefast to hem silf a wickid word. Thei telden, that thei schulden hide snaris; thei seiden, Who schal se hem?
Iwo amalimbikitsana wina ndi mnzake pa chikonzero chawo choyipa, amayankhula zobisa misampha yawo; ndipo amati, “Adzayiona ndani?”
6 Thei souyten wickidnessis; thei souyten, and failiden in sekinge. A man neiyhe to deep herte;
Iwo amakonzekera zosalungama ndipo amati, “Takonza ndondomeko yabwino kwambiri!” Ndithu maganizo ndi mtima wa munthu ndi zachinyengo.
7 and God schal be enhaunsid. The arowis of `litle men ben maad the woundis of hem;
Koma Mulungu adzawalasa ndi mivi; mwadzidzidzi adzakanthidwa.
8 and the tungis of hem ben maad sijk ayens hem. Alle men ben disturblid, that sien hem;
Iye adzatembenuza milomo yawoyo kuwatsutsa ndi kuwasandutsa bwinja; onse amene adzawaona adzagwedeza mitu yawo mowanyoza.
9 and ech man dredde. And thei telden the werkis of God; and vndurstoden the dedis of God.
Anthu onse adzachita mantha; adzalengeza ntchito za Mulungu ndi kulingalira mozama zomwe Iye wazichita.
10 The iust man schal be glad in the Lord, and schal hope in hym; and alle men of riytful herte schulen be preisid.
Lolani wolungama akondwere mwa Yehova ndi kubisala mwa Iye, owongoka mtima onse atamande Iye!

< Psalms 64 >