< 1 Kings 15 >

1 Therfor in the eiytenthe yeer of the rewme of Jeroboam, sone of Nabath, Abia regnede on Juda.
Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Nebati, Abiya anakhala mfumu ya Yuda,
2 Thre yeer he regnede in Jerusalem; the name of his modir was Maacha, douyter of Abessalon.
ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zitatu. Amayi ake anali Maaka, mwana wa Abisalomu.
3 And he yede in alle the synnes of his fadir, which he dide bifor hym; and his herte was not perfit with his Lord God, as the herte of Dauid, his fadir, `was perfit.
Abiya anachita zoyipa zonse zimene abambo ake anazichita. Sanali wangwiro pamaso pa Yehova Mulungu wake, monga linachitira kholo lake Davide.
4 But for Dauid his Lord God yaf to hym a lanterne in Jerusalem, that he schulde reise his sone after hym, and that he schulde stonde in Jerusalem;
Komabe chifukwa cha Davide, Yehova Mulungu wake anamupatsa nyale mu Yerusalemu pomupatsa mwana wolowa mʼmalo mwake ndi kumukhazikitsa kukhala wamphamvu mu Yerusalemu;
5 for Dauid hadde do riytfulnesse in the iyen of the Lord, and hadde not bowid fro alle thingis whiche the Lord hadde comaundid to him, in alle the daies of his lijf, outakun the word of Urie Ethei.
pakuti Davide anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo sanalephere kusunga chilichonse chimene Yehova anamulamula masiku onse a moyo wake kupatula nkhani ija ya Uriya Mhiti.
6 Netheles batel was bitwix Abia and Jeroboam, in al the tyme of his lijf.
Panali nkhondo pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu masiku onse a moyo wa Abiya.
7 Sotheli the residue of wordis of Abia, and alle thinges whiche he dide, whether these ben not writun in the book of wordis of daies of the kyngys of Juda? And batel was bitwixe Abia and Jeroboam.
Tsono ntchito zina za Abiya, ndi zina zonse anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
8 And Abia slepte with his fadris; and thei birieden hym in the citee of Dauid; and Asa, his sone, regnede for hym.
Ndipo Abiya anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Asa, mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
9 Sotheli Asa, king of Jude, regnede in the twentithe yeer of Jeroboam, kyng of Israel;
Mʼchaka cha makumi awiri cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Asa anakhala mfumu ya Yuda,
10 and Asa regnede oon and fourti yeer in Jerusalem. The name of his modir was Maacha, douyter of Abessalon.
ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 41. Agogo ake akazi anali Maaka mwana wa Abisalomu.
11 And Asa dide riytfulnesse in the siyt of the Lord, as Dauid, his fadir, dide;
Asa anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
12 and he took awey fro the loond men of wymmens condiciouns, and he purgide alle the filthis of idols, whiche his fadris maden.
Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zadama pochita chipembedzo chawo ndiponso anachotsa mafano onse amene makolo ake anawapanga.
13 Ferthermore and he remouyde Maacha, his modir, that sche schulde not be princesse in the solempne thingis of Priapus, and in his wode which sche hadde halewid; and he distriede the denne of hym, and he brak the foulest symylacre, and brente in the stronde of Cedron;
Iye anachotsanso gogo wake Maaka pa udindo wake wa amayi a mfumu, chifukwa choti anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo nakalitentha ku Chigwa cha Kidroni.
14 sotheli he dide not awei hiy thingis; netheles the herte of Asa was perfit with hys Lord God, in alle hise daies.
Ngakhale sanachotse malo opembedzerapo mafano, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova masiku onse a moyo wake.
15 And he brouyte in to the hous of the Lord tho thingis, whiche his fadir hadde halewid and auowid, siluer, and gold, and vessel.
Asa anabweretsa ku Nyumba ya Yehova zinthu zimene abambo ake anazipereka, ndiponso zinthu zimene iye mwini anazipereka: zagolide, siliva ndi ziwiya zotengera.
16 Forsothe batel was bitwixe Asa and Baasa, kyng of Israel, in alle the daies of hem.
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
17 And Baasa, kyng of Israel, stiede in to Juda, and bildide Rama, that no man of the part of Aza, kyng of Juda, myyte go out, ether go yn.
Baasa mfumu ya Israeli anapita kukathira nkhondo dziko la Yuda, ndipo anamangira linga mzinda wa Rama kuletsa kuti wina aliyense asatuluke kapena kulowa mʼdziko la Asa, mfumu ya Yuda.
18 Therfor Asa took al the siluer and gold, that lefte in the tresouris of the hows of the Lord, and in the tresouris of the kyngis hows, and yaf it in to the hondis of hise seruauntis; and sente to Benadab, sone of Tabrennon, sone of Ozion, the kyng of Sirie, that dwellide in Damask, and seide,
Tsono Asa anatenga siliva yense pamodzi ndi golide zimene zinatsala ku malo osungira chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso ku nyumba yake yaufumu. Anazipereka kwa atumiki ake, nawatuma kupita nazo kwa Beni-Hadadi mwana wa Tabirimoni, mwana wa Heziyoni, mfumu ya Aramu, amene ankakhala ku Damasiko ndipo anakamuwuza kuti,
19 Boond of pees is bitwixe me and thee, and bitwixe my fadir and thi fadir, and therfor Y sente to thee yiftis, gold, and siluer; and Y axe, that thou come, and make voide the boond of pees, which thou hast with Baasa, kyng of Israel, and that he go awey fro me.
“Tiyeni tigwirizane inu ndi ine, monga panali mgwirizano pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Onani, ndikukutumizirani mphatso za siliva ndi golide. Tsopano kathetseni mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti andisiye.”
20 Benadab assentide to kyng Asa, and sente the princes of his oost in to the citees of Israel; and thei smytiden Ahion, and Dan, and Abel, the hows of Maacha, and al Cenoroth, that is, al the lond of Neptalym.
Choncho Beni-Hadadi anamvera zimene ananena mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira magulu ake ankhondo ku mizinda ya Israeli. Ndipo iye anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Beti-Maaka ndi dera lonse la Kinereti kuphatikiza dziko lonse la Nafutali.
21 And whanne Baasa hadde herd this thing, he lefte to bilde Rama, and turnede ayen in to Thersa.
Baasa atamva zimenezi, anasiya kumangira linga Rama ndipo anakakhala ku Tiriza.
22 Forsothe kyng Asa sente message in to al Juda, and seide, No man be excusid. And thei token the stoonys of Rama, and the trees therof, bi whiche Baasa hadde bildid; and kyng Asa bildide of the same `stoonys and trees Gabaa of Beniamyn, and Maspha.
Pamenepo Mfumu Asa analamula anthu onse a ku Yuda osasiya ndi mmodzi yemwe, ndipo anachotsa ku Rama miyala ndi matabwa amene Baasa ankamangira kumeneko. Zipangizo zimenezi Mfumu Asa inamangira linga la Geba ku Benjamini ndi la ku Mizipa.
23 Sotheli the residue of alle wordis of Asa, and of al his strengthe, and alle thingis whiche he dide, and the citees whiche he bildide, whether these ben not writun in the book of wordis of daies of kingis of Juda? Netheles Asa hadde ache in feet, in the tyme of his eelde.
Tsono ntchito zina za Asa, za mphamvu zake ndi mizinda imene anayimanga ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Koma pa nthawi ya ukalamba wake anadwala nthenda ya mapazi.
24 And Asa slepte with hise fadris, and he was biried with hem in the citee of Dauid, his fader; and Josophat, his sone, regnede for him.
Ndipo Asa anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu mzinda wa Davide kholo lake. Ndipo Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
25 Forsothe Nadab, the sone of Jeroboam, regnede on Israel, in the secunde yeer of Asa, king of Juda; and he regnede on Israel two yeer.
Nadabu, mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli mʼchaka chachiwiri cha Asa mfumu ya Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
26 And he dide that, that was yuel in the siyt of the Lord, and he yede in the weies of his fadir, and in the synnes of hym, in whiche he made Israel to do synne.
Nadabu anachita zoyipa pamaso pa Yehova, anayenda mʼnjira za abambo ake ndi mu uchimo womwe anachimwitsa nawo Israeli.
27 Forsothe Baasa, the sone of Ahia, of the hows of Ysachar, settide tresoun to hym, and smoot him in Gebethon, which is a citee of Filisteis; sothely Nadab and al Israel bisegiden Gebethon.
Baasa mwana wa Ahiya, wa banja la Isakara anakonzera Nadabuyo chiwembu, ndipo anamukantha ku Gibetoni, mzinda wa Afilisti, pamene Nadabu ndi anthu onse a ku Israeli anali atawuzungulira.
28 Therfor Baasa killide hym, in the thridde yeer of Asa, king of Juda, and regnede for hym.
Baasa anapha Nadabu mʼchaka chachitatu cha Asa, mfumu ya ku Yuda ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 And whanne he hadde regnede, he smoot al the hows of Jeroboam; he lefte not sotheli not o man of his seed, til he dide awei hym, bi the word of the Lord, which he spak in the hond of his seruaunt, Ahia of Silo, a profete,
Iye atangoyamba kulamulira, anapha anthu onse a banja la Yeroboamu. Sanasiye ndi mmodzi yemwe wamoyo pa banjapo, koma anawononga anthu onse, molingana ndi mawu a Yehova amene anayankhula mwa mtumiki wake Ahiya wa ku Silo
30 for the synnes of Jeroboam whiche he synnede, and in whiche he made Israel to do synne, and for the trespas, bi which he wraththide the Lord God of Israel.
chifukwa cha machimo amene Yeroboamu anachita, ndiponso kuchimwitsa anthu a ku Israeli, naputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israeli.
31 Sotheli the residue of wordis of Nadab, and alle thingis whiche he wrouyte, whether these ben not writun in the book of wordis of daies of the kyngis of Israel?
Tsono ntchito za Nadabu ndi zina zonse zimene anazichita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
32 And batel was bitwixe Asa and Baasa, kyng of Israel, in al the daies of hem.
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli pa nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
33 In the thridde yeer of Asa, kyng of Juda, Baasa, sone of Ahia, regnede on al Israel, in Thersa, foure and twenti yeer.
Chaka chachitatu cha Asa mfumu ya Yuda, Baasa mwana wa Ahiya anakhala mfumu ya Aisraeli onse ku Tiriza, ndipo analamulira zaka 24.
34 And he dide yuel bifor the Lord, and he yede in the weies of Jeroboam, and in hise synnes, bi whiche he made Israel to do synne.
Anachita zoyipa pamaso pa Yehova, nayenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchita tchimo lake limene linachimwitsa anthu a ku Israeli.

< 1 Kings 15 >