< 1 Kings 14 >

1 In that tyme Abia, sone of Jeroboam, was sijk.
Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
2 And Jeroboam seide to his wijf, Rise thou, and chaunge clothing, that thou be not knowun, that thou art the wijf of Jeroboam; and go thou in to Silo, where Ahia, the prophete, is, which spak to me, that Y schulde regne on this puple.
ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
3 Also take thou in the hond ten looues, and a cake, and a vessil of hony, and go thou to hym; for he schal schewe to thee, what schal bifalle to this child.
Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
4 The wijf of Jeroboam dide as he seide, and sche roos, and yede in to Silo, and cam in to the hows of Ahia; and he miyte not se, for hise iyen dasewiden for eelde.
Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
5 Forsothe the Lord seide to Ahia, Lo! the wijf of Jeroboam entrith, that sche counsele thee on hir sone, which is sijk; thou schalt speke these and these thingis to hir. Therfor whanne sche hadde entrid, and hadde feyned hir silf to be that `womman which sche was not,
Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
6 Ahia herde the soune of the feet of hir entrynge bi the dore, and he seide, Entre thou, the wijf of Jeroboam; whi feynest thou thee to bee an other womman? Forsothe Y am sent an hard messanger to thee.
Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
7 Go thou, and seie to Jeroboam, The Lord God of Israel seith these thingis, For Y enhaunside thee fro the myddis of the puple, and Y yaf thee duyk on my puple Israel,
Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
8 and Y kittide the rewme of the hows of Dauid, and Y yaf it to thee, and thou were not as my seruaunt Dauid, that kepte myn heestis, and suede me in al his herte, and dide that that was plesaunt in my siyt;
Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
9 but thou wrouytist yuel, ouer alle men that weren bifore thee, and madist to thee alien goddis, and wellid to gidere, that thou schuldist excite me to wrathfulnesse, sotheli thou hast cast forth me bihyndis thi bak.
Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
10 Therfor lo! Y schal brynge in yuels on the hows of Jeroboam, and Y schal smyte of Jeroboam `til to a pissere to the wal, and prisoned, and the laste in Israel; and Y schal clense the relikis of the hows of Jeroboam, as dung is wont to be clensid `til to the purete, `ether clennesse;
“‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
11 sotheli doggis schulen ete hem, that schulen die of the hows of Jeroboam in citee; forsothe briddis of the eyr schulen deuoure hem, that schulen die in the feeld; for the Lord spak.
Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
12 Therfor rise thou, and go in to thin hows; and in thilke entryng of thi feet in to the citee the child schal die.
“Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
13 And al Israel schal biweile him, and schal birie; for this child aloone of Jeroboam schal be borun in to sepulcre, for a good word is foundun on hym of the Lord God of Israel, in the hows of Jeroboam.
Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
14 Forsothe the Lord schal ordeyne to hym a kyng on Israel, that schal smyte the hows of Jeroboam, in this dai and in this tyme;
“Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
15 and the Lord God of Israel schal smyte, as a reed in the water is wont to be mouyd; and he schal drawe out Israel fro this good lond, which he yaf to her fadris, and he schal wyndewe hem ouer the flood, for thei maden to hem woodis, that thei schulden terre the Lord to ire.
Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
16 And the Lord God schal bitake Israel to hise enemyes, for the synnes of Jeroboam, that synnede, and made Israel to do synne.
Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
17 Therfor the wijf of Jeroboam roos, and yede, and cam in to Thersa; whanne sche entride in to the threschfold of the hows, the child was deed.
Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
18 And thei birieden hym; and al Israel biweilide hym, bi the word of the Lord, which he spak in the hoond of his seruaunt, Ahia the prophet.
Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
19 Forsothe, lo! the residue of wordis of Jeroboam, how he fauyt, and how he regnede, ben writun in the book of wordis of the daies of kyngis of Israel.
Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
20 Forsothe the daies, in whiche Jeroboam regnede, ben two and twenti yeer; and Jeroboam slepte with hise fadris, and Nadab, his sone, regnede for hym.
Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
21 Forsothe Roboam, the sone of Salomon, regnede in Juda; Roboam was of oon and fourti yeer, whanne he bigan to regne, and he regnede seuentene yeer in Jerusalem, the citee which the Lord chees of alle the lynagis of Israel, that he schulde sette his name there. Sotheli the name of his moder was Naama Amanyte.
Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
22 And Juda dide yuel bifor the Lord, and thei terriden hym to ire on alle thingis, whiche her fadris diden in her synnes, bi whiche thei synneden.
Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
23 For also thei bildiden to hem silf auters, and ymagis, and wodis, on eche hiy hil, and vndur ech tree ful of bowis.
Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
24 But also `men of wymmens condiciouns weren in the lond, and thei diden alle abhominaciouns of hethene men, whiche the Lord al to-brak bifor the face of the sones of Israel.
Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
25 Forsothe in the fifthe yeer of the rewme of Roboam, Sesach, the kyng of Egipt, styede in to Jerusalem;
Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
26 and he took the tresouris of the hows of the Lord, and the kyngis tresouris, and he rauischide alle thingis; also `he rauischide the goldun scheeldis, whiche Salomon made.
Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
27 For whiche kyng Roboam made brasun scheeldis, and yaf tho in the hondis of duykis of scheeld makeris, and of hem that wakiden bifor the dore of the hows of the Lord.
Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
28 And whanne the kyng entride in to the hows of the Lord, thei that hadden office to go bifore, baren tho, and baren ayen to the place of armer of scheeld makeris.
Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
29 Forsothe, lo! the residue of wordis of Roboam, and alle thingis whiche he dide, ben writun in the book of wordis of daies of kyngis of Juda.
Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
30 And batel was bitwixe Roboam and Jeroboam, in alle daies.
Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
31 And Roboam slepte with hise fadris, and was biried with hem in the citee of Dauid. Forsothe the name of his modir was Naama Amanyte; and Abia, his sone, regnede for hym.
Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.

< 1 Kings 14 >