< Job 33 >

1 Wherefore, Job, I pray thee, hear my speeches, and hearken to all my words.
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 Behold, now I have opened my mouth, my tongue hath spoken in my mouth.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 My words [shall be of] the uprightness of my heart: and my lips shall utter knowledge clearly.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 The Spirit of God hath made me, and the breath of the Almighty hath given me life.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 If thou canst answer me, set [thy words] in order before me, stand up.
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 Behold, I [am] according to thy wish in God's stead: I also am formed out of the clay.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 Behold, my terror shall not make thee afraid, neither shall my hand be heavy upon thee.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 Surely thou hast spoken in my hearing, and I have heard the voice of [thy] words, [saying],
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 I am clean without transgression, I [am] innocent; neither [is there] iniquity in me.
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 Behold, he findeth occasions against me, he counteth me for his enemy,
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 He putteth my feet in the stocks, he marketh all my paths.
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 Behold, [in] this thou art not just: I will answer thee, that God is greater than man.
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Why dost thou strive against him? for he giveth not account of any of his matters.
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 For God speaketh once, yes twice, [yet man] perceiveth it not.
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 In a dream, in a vision of the night, when deep sleep falleth upon men, in slumberings upon the bed;
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 Then he openeth the ears of men, and sealeth their instruction,
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 That he may withdraw man [from his] purpose, and hide pride from man.
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 He keepeth back his soul from the pit, and his life from perishing by the sword.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 He is chastened also with pain upon his bed, and the multitude of his bones with strong [pain]:
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 So that his life abhorreth bread, and his soul dainty food.
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 His flesh is consumed away, that it cannot be seen; and his bones [that] were not seen stick out.
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 Yes, his soul draweth near to the grave, and his life to the destroyers.
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 If there is a messenger with him, an interpreter, one among a thousand, to show to man his uprightness:
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 Then he is gracious to him, and saith, Deliver him from going down to the pit: I have found a ransom.
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 His flesh shall be fresher than a child's: he will return to the days of his youth:
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 He shall pray to God, and he will be favorable to him: and he shall see his face with joy: for he will render to man his righteousness.
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 He looketh upon men, and [if any] shall say, I have sinned, and perverted [that which was] right, and it profited me not;
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 He will deliver his soul from going into the pit, and his life shall see the light.
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 Lo, all these [things] God often worketh with man,
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 To bring back his soul from the pit, to be enlightened with the light of the living.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 Mark well, O Job, hearken to me: hold thy peace, and I will speak.
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 If thou hast any thing to say, answer me: speak, for I desire to justify thee.
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 If not, hearken to me: hold thy peace, and I shall teach thee wisdom.
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

< Job 33 >