< Job 21 >

1 But Job answered and said,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Hear diligently my speech, and let this be your consolations.
“Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
3 Suffer me that I may speak; and after I have spoken, mock on.
Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
4 As for me, [is] my complaint to man? and if [it were so], why should not my spirit be troubled?
“Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
5 Mark me, and be astonished, and lay [your] hand upon [your] mouth.
Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
6 Even when I remember I am afraid, and trembling taketh hold on my flesh.
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
7 Why do the wicked live, become old, and, are mighty in power?
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
8 Their seed is established in their sight with them, and their offspring before their eyes.
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
9 Their houses [are] safe from fear, neither [is] the rod of God upon them.
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 Their bull gendereth, and faileth not; their cow calveth, and casteth not her calf.
Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 They send forth their little ones like a flock, and their children dance.
Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
12 They take the timbrel and harp, and rejoice at the sound of the organ.
Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 They spend their days in wealth, and in a moment go down to the grave. (Sheol h7585)
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
14 Therefore they say to God, Depart from us; for we desire not the knowledge of thy ways.
Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 What [is] the Almighty, that we should serve him? and what profit should we have, if we pray to him?
Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 Lo, their good [is] not in their hand: the counsel of the wicked is far from me.
Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
17 How oft is the candle of the wicked put out? and [how oft] cometh their destruction upon them? [God] distributeth sorrows in his anger.
“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 They are as stubble before the wind, and as chaff that the storm carrieth away.
Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 God layeth up his iniquity for his children: he rewardeth him, and he shall know [it].
Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 His eyes shall see his destruction, and he shall drink of the wrath of the Almighty.
Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 For what pleasure [hath] he in his house after him, when the number of his months is cut off in the midst?
Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
22 Shall [any] teach God knowledge? seeing he judgeth those that are high.
“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 One dieth in his full strength, being wholly at ease and quiet.
Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 His breasts are full of milk, and his bones are moistened with marrow.
thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 And another dieth in the bitterness of his soul, and never eateth with pleasure.
Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 They shall lie down alike in the dust, and the worms shall cover them.
Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
27 Behold, I know your thoughts, and the devices [which] ye wrongfully imagine against me.
“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 For ye say, Where [is] the house of the prince? and where [are] the dwelling places of the wicked?
Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 Have ye not asked them that go by the way? and do ye not know their tokens,
Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 That the wicked is reserved to the day of destruction? they will be brought forth to the day of wrath.
Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 Who shall declare his way to his face? and who shall repay him [what] he hath done?
Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 Yet he shall be brought to the grave, and shall remain in the tomb.
Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 The clods of the valley will be sweet to him, and every man will draw after him, as [there are] innumerable before him.
Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
34 How then comfort ye me in vain, seeing in your answers there remaineth falsehood?
“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”

< Job 21 >