< Zechariah 1 >
1 In the eighth month of the second year of Darius' reign, the word of Yahweh came to Zechariah son of Berechiah son of Iddo, the prophet, saying,
Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:
2 “Yahweh was exceedingly angry with your fathers!
“Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.
3 Say to them, 'Yahweh of hosts says this: Turn to me!—this is the declaration of Yahweh of hosts— and I will return to you, says Yahweh of hosts.
Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
4 Do not be like your fathers to whom the prophets cried out previously, saying, “Yahweh of hosts says this: Turn from your evil ways and wicked practices!” But they would not hear and did not pay attention to me—this is Yahweh's declaration.'
Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova.
5 Your fathers, where are they? Where are the prophets, are they here forever?
Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya?
6 But my words and my decrees that I commanded my servants the prophets, have they not overtaken your fathers? So they repented and said, 'Just as Yahweh of hosts planned to do to us what our ways and actions deserved, so he has dealt with us.'”
Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu? “Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’”
7 On the twenty-fourth day of the eleventh month, which is the month of Shebat, in the second year of Darius' reign, the word of Yahweh came to Zechariah son of Berechiah son of Iddo, the prophet, saying,
Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.
8 “I saw in the night, and, look! a man was riding on a red horse, and he was among the myrtle trees that are in the valley; and behind him there were red, reddish-brown, and white horses.”
Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.
9 I said, “What are these things, Lord?” Then the angel who talked with me said to me, “I will show you what these things are.”
Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?” Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”
10 Then the man who stood among the myrtle trees answered and said, “These are those Yahweh has sent out to roam throughout the earth.”
Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”
11 They answered the angel of Yahweh who stood among the myrtle trees; they said to him, “We have been roaming throughout the earth; see, all the earth sits still and is at rest.”
Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”
12 Then the angel of Yahweh answered and said, “Yahweh of hosts, how long will you show no compassion to Jerusalem and to the cities of Judah, which you have been angry with these seventy years?”
Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?”
13 Yahweh answered the angel who had talked with me, with good words, words of comfort.
Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.
14 So the angel who had talked with me said to me, “Call out and say, 'Yahweh of hosts says this: I have been jealous for Jerusalem and for Zion with a great passion!
Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni,
15 I am very angry with the nations that are at ease. When I was only a little angry with them, they made the disaster worse.
koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’
16 Therefore Yahweh of hosts says this: I have returned to Jerusalem with mercies. My house will be built within her —this is the declaration of Yahweh of hosts—and the measuring line will be stretched out over Jerusalem!'
“Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
17 Again call out, saying, 'Yahweh of hosts says this: My cities will once again overflow with goodness, and Yahweh will again comfort Zion, and he will once again choose Jerusalem.'”
“Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’”
18 Then I lifted up my eyes and saw four horns!
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi.
19 I spoke to the angel who talked with me, “What are these?” He answered me, “These are the horns that have scattered Judah, Israel, and Jerusalem.”
Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?” Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”
20 Then Yahweh showed me four craftsmen.
Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi.
21 I said, “What are these people coming to do?” He answered, and said, “These are the horns that scattered Judah so that no man would lift up his head. But the blacksmiths have come to terrify them, to cast down the horns of the nations that lifted up a horn against the land of Judah to scatter her.”
Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?” Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”