< Haggai 1 >

1 In the second year of Darius the king, in the sixth month, on the first day of the month, the word of Yahweh came by the hand of Haggai the prophet to the governor of Judah, Zerubbabel son of Shealtiel, and to the high priest Joshua son of Jehozadak, saying,
Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:
2 “Yahweh of hosts says this: These people say, 'It is not time for us to come or to build Yahweh's house.'”
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’”
3 Then the word of Yahweh came by the hand of Haggai the prophet, saying,
Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti,
4 “Is it a time for you yourselves to live in your finished houses, while this house lies ruined?
“Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”
5 So now Yahweh of hosts says this: Consider your ways!
Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu.
6 You have sown much seed, but bring in little harvest; you eat but do not have enough; you drink but cannot get drunk. You wear clothes but cannot warm yourselves, and the wage earner earns money only to put it into a bag full of holes!
Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”
7 Yahweh of hosts says this: “Consider your ways!
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu.
8 Go up to the mountain, bring timber, and build my house; then I will take pleasure in it, and I will be glorified!—says Yahweh.”
Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova.
9 “You looked for much, but behold! you have brought little home, for I blew it away! Why?” declares Yahweh of hosts. “Because my house lies in ruins, while every one of you is working on his own house.
“Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake.
10 Because of this the heavens withhold the dew from you, and the earth withholds its produce.
Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera.
11 I have summoned a drought upon the land and upon the mountains, upon the grain and upon the new wine, upon the oil and upon the harvest of the earth, upon men and upon beasts, and upon all the labor of your hands!”
Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”
12 Then Zerubbabel son of Shealtiel, and the high priest Joshua son of Jehozadak, along with all the remnant of the people, obeyed the voice of Yahweh their God and the words of Haggai the prophet, because Yahweh their God had sent him and the people feared the face of Yahweh.
Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.
13 Then Haggai, the messenger of Yahweh, spoke Yahweh's message to the people and said, “I am with you!—this is Yahweh's declaration!”
Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova.
14 So Yahweh stirred up the spirit of the governor of Judah, Zerubbabel son of Shealtiel, and the spirit of the high priest Joshua son of Jehozadak, and the spirit of all the remnant of the people, so that they went and worked on the house of Yahweh of hosts, their God
Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo,
15 in the twenty-fourth day of the sixth month, in the second year of Darius the king.
pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.

< Haggai 1 >