< Psalms 11 >
1 For the chief musician. A psalm of David. I take refuge in Yahweh; how will you say to me, “Flee like a bird to the mountain”?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Yehova ine ndimathawiramo. Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti, “Thawira ku phiri lako ngati mbalame.
2 For see! The wicked prepare their bows. They make ready their arrows on the strings to shoot in the darkness at the upright in heart.
Pakuti taona oyipa akunga mauta awo; ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta, pobisala pawo kuti alase olungama mtima.
3 For if the foundations are ruined, what can the righteous do?
Tsono ngati maziko awonongeka, olungama angachite chiyani?”
4 Yahweh is in his holy temple; his eyes watch, his eyes examine the children of mankind.
Yehova ali mʼNyumba yake yoyera; Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba. Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu; maso ake amawayesa.
5 Yahweh examines both the righteous and the wicked, but he hates those who love to do violence.
Yehova amayesa olungama, koma moyo wake umadana ndi oyipa, amene amakonda zachiwawa.
6 He rains burning coals and brimstone upon the wicked; a scorching wind will be their portion from his cup!
Iye adzakhuthulira pa oyipa makala amoto ndi sulufule woyaka; mphepo yotentha idzakhala yowayenera.
7 For Yahweh is righteous, and he loves righteousness; the upright will see his face.
Pakuti Yehova ndi wolungama, Iye amakonda chilungamo; ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.