< Isaiah 7 >
1 During the days of Ahaz son of Jotham son of Uzziah, king of Judah, Rezin the king of Aram, and Pekah son of Remaliah, king of Israel, went up to Jerusalem to war against it, but they could not prevail against it.
Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.
2 It was reported to the house of David that Aram was allied with Ephraim. His heart trembled, and the heart of his people, as the trees of the forest shake in the wind.
Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.
3 Then Yahweh said to Isaiah, “Go out with your son Shear-Jashub to meet Ahaz at the end of the conduit of the upper pool, on the road to Launderer's Field.
Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu.
4 Tell him, 'Be careful, remain calm, do not be afraid or intimidated by these two smoldering firebrands, by the fierce anger of Rezin and Aram, and of Pekah son of Remaliah.
Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya.
5 Aram, Ephraim, and the son of Remaliah have planned evil against you; they have said,
Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti,
6 “Let us attack Judah and terrify her, and let us break into her and set up our king there, the son of Tabeel.”
‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’
7 The Lord Yahweh says, “It will not take place; it will not happen,
Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi: “‘Zimenezo sizidzatheka, sizidzachitika konse,
8 because the head of Aram is Damascus, and the head of Damascus is Rezin. Within sixty-five years, Ephraim will be shattered and will no longer be a people.
pakuti Siriya amadalira Damasiko, ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi. Zisanathe zaka 65 Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.
9 The head of Ephraim is Samaria, and the head of Samaria is Remaliah's son. If you do not remain firm in faith, surely you will not remain secure.”'”
Dziko la Efereimu limadalira Samariya ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi. Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu, ndithu simudzalimba konse.’”
10 The Lord spoke again to Ahaz,
Yehova anayankhulanso ndi Ahazi,
11 “Ask a sign of Yahweh your God; ask for it in the depths or in the height above.” (Sheol )
“Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol )
12 But Ahaz said, “I will not ask, nor will I test Yahweh.”
Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”
13 So Isaiah replied, “Listen, house of David. Is it not enough for you people to test the patience of people? Must you also test the patience of my God?
Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga?
14 Therefore the Lord himself will give you people a sign: See, the young woman will conceive, bear a son, and will call his name Immanuel.
Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli.
15 He will eat curds and honey when he knows to refuse the evil and choose the good.
Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino.
16 For before the child knows to refuse the evil and choose the good, the land whose two kings you dread will be desolate.
Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja.
17 Yahweh will bring on you, on your people, and on your father's house days unlike any since Ephraim seceded from Judah—he will bring on you the king of Assyria.”
Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”
18 At that time Yahweh will whistle for a fly from the distant streams of Egypt, and for a bee from the land of Assyria.
Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya.
19 They will all come and settle down into all the gorges, into the clefts of the rocks, on all the thornbushes, and onto all the pastures.
Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto.
20 At that time the Lord will shave with a razor that was hired beyond the Euphrates River—the king of Assyria— the head and the hair of the legs; it will also sweep away the beard.
Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe.
21 On that day, a man will keep alive a young cow and two sheep,
Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri.
22 and because of the abundance of milk which they shall give, he will eat curds, for everyone left in the land will eat curds and honey.
Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi.
23 At that time, where there were a thousand vines worth a thousand silver shekels, there will be nothing but briers and thorns.
Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga.
24 Men will go there to hunt with bows, because all the land will be briers and thorns.
Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga.
25 They will stay away from all the hills that were cultivated with the hoe, for fear of the briers and thorns; but it will be a place where cattle and sheep graze.
Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.