< Isaiah 14 >
1 Yahweh will have compassion on Jacob; he will again choose Israel and restore them into their own land. Foreigners will join with them and attach themselves to the house of Jacob.
Yehova adzachitira chifundo Yakobo; adzasankhanso Israeli ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo. Alendo adzabwera kudzakhala nawo ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.
2 The nations will bring them to their own place. Then the house of Israel will take them in the land of Yahweh as male and female servants. They will take captive those who had captured them, and they will rule over their oppressors.
Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli ku dziko lawo. Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova. Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo. Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.
3 On the day that Yahweh gives you rest from your suffering and anguish, and from the hard labor which you were required to perform,
Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani,
4 you will sing this taunt song against the king of Babylon, “How the oppressor has come to an end, the proud fury ended!
mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti, Wopsinja uja watha! Ukali wake uja watha!
5 Yahweh has broken the staff of the wicked, the scepter of those rulers,
Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa, Iye waphwanya ndodo ya olamulira.
6 that struck the peoples in wrath with unceasing blows, that ruled the nations in anger, with an attack that was unrestrained.
Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali powamenya kosalekeza, Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali ndikuwazunza kosalekeza.
7 The whole earth is at rest and is quiet; they begin celebrating with singing.
Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere; ndipo akuyimba mokondwa.
8 Even the cypress trees rejoice over you with the cedars of Lebanon; they say, 'Since you are laid low, no woodcutter comes up to cut us down.'
Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti, “Chigwetsedwere chako pansi, palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”
9 Sheol below is eager to meet you when you go there. It arouses the dead for you, all the kings of the earth, making them rise up from their thrones, all the kings of the nations. (Sheol )
Ku manda kwatekeseka kuti akulandire ukamabwera; mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri a dziko lapansi, yadzutsidwa. Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu ayimiritsidwa pa mipando yawo. (Sheol )
10 They all will speak and say to you, 'You have become as weak as us. You have become like us.
Onse adzayankha; adzanena kwa iwe kuti, “Iwenso watheratu mphamvu ngati ife; Iwe wafanana ndi ife.”
11 Your pomp has been brought down to Sheol with the sound of your string instruments. Maggots are spread under you, and worms cover you.' (Sheol )
Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda, pamodzi ndi nyimbo za azeze ako; mphutsi zayalana pogona pako ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi. (Sheol )
12 How you are fallen from heaven, daystar, son of the morning! How you are cut down to the ground, you who conquered the nations!
Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha! Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi, Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!
13 You had said in your heart, 'I will ascend into heaven, I will exalt my throne above the stars of God, and I will sit on the mount of assembly, in the far reaches of the north.
Mu mtima mwako unkanena kuti, “Ndidzakwera mpaka kumwamba; ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako, pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.
14 I will ascend above the heights of the clouds; I will make myself like the Most High God.'
Ndidzakwera pamwamba pa mitambo; ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”
15 Yet you are now brought down to Sheol, to the depths of the pit. (Sheol )
Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje. (Sheol )
16 Those who see you will gaze at you and they will pay attention to you. They will say, 'Is this the man who made the earth tremble, who shook kingdoms,
Anthu akufa adzakupenyetsetsa nadzamalingalira za iwe nʼkumati, “Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi ndi kunjenjemeretsa maufumu,
17 who made the world like a wilderness, who overthrew its cities and did not let his prisoners go home?'
munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu, amene anagwetsa mizinda yake ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”
18 All the kings of the nations, all of them lie down in honor, each one in his own tomb.
Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu aliyense mʼmanda akeake.
19 But you are cast out of your grave like a branch thrown away. The dead cover you like a garment, those pierced by the sword, who go down to the stones of the pit.
Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako, ngati nthambi yowola ndi yonyansa. Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa; amene anabayidwa ndi lupanga, anatsikira mʼdzenje lamiyala ngati mtembo woponderezedwa.
20 You will not join them in burial, because you have destroyed your land and killed your people. The offspring of evildoers will never be mentioned again.”
Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu, chifukwa unawononga dziko lako ndi kupha anthu ako. Zidzukulu za anthu oyipa sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.
21 Prepare your slaughter for his children, for the iniquity of their ancestors, so they will not rise up and possess the earth and fill the whole world with cities.
Konzani malo woti muphere ana ake aamuna chifukwa cha machimo a makolo awo; kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.
22 “I will rise up against them”—this is the declaration of Yahweh of hosts. “I will cut off from Babylon name, descendant, and posterity”—this is Yahweh's declaration.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni. Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo. Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,” akutero Yehova.
23 “I will also make her into a possession of owls, and into pools of water, and I will sweep her with the broom of destruction”—this is the declaration of Yahweh of hosts.
“Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu ndiponso dambo lamatope; ndidzawusesa ndi tsache lowononga,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
24 Yahweh of hosts has sworn, “Surely, as I have intended, so it will come about; and as I have purposed, so it will be:
Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti, “Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho, ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.
25 I will break the Assyrian in my land, and on my mountains trample him underfoot. Then his yoke will be lifted from off them and his burden from off their shoulder.” Then his yoke will be lifted from off them and his burden from off their shoulder.”
Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa; ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga; ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga, ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”
26 This is the plan that is intended for the whole earth, and this is the hand that is raised over all the nations.
Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi, ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.
27 For Yahweh of hosts has planned this; who will stop him? His hand is raised, and who will turn it back?
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse? Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?
28 In the year that king Ahaz died this declaration came:
Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:
29 Do not rejoice, all you Philistines, that the rod that struck you is broken. For out of the serpent's root will grow out an adder, and his offspring will be a fiery flying serpent.
Musakondwere inu Afilisti nonse kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa; chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri, ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.
30 The firstborn of the poor will graze their sheep in my pastures, and the needy will lie down in safety. I will kill your root with famine that will put to death all your survivors.
Osaukitsitsa adzapeza chakudya ndipo amphawi adzakhala mwamtendere. Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala, ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.
31 Howl, gate; cry, city; all of you will melt away, Philistia. For out of the north comes a cloud of smoke, and there is no straggler in his ranks.
Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda! Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse! Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto, ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.
32 How will they respond to the messengers of that nation? “Yahweh has founded Zion, and in her the afflicted of his people will find refuge.”
Kodi tidzawayankha chiyani amithenga a ku Filisitiya? “Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”