< Psalms 80 >

1 [Yahweh], you [who lead us like] a shepherd leads his flock [of sheep], listen to us Israeli people. You sit on your throne [in the Very Holy Place in the temple], above the [carvings of] winged creatures.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
2 Show yourself to [the people of the tribes of] Ephraim and Benjamin and Manasseh! Show us that you are powerful and come and rescue us!
kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
3 God, cause our nation to be strong like it was before; be kind to us [IDM] in order that we may be saved [from our enemies.]
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
4 Yahweh, you who are the commander of the armies of heaven, how long will you be angry with us, your people, when we pray to you?
Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
5 [It is as though] the only food and drink that you have given us is a cup full of our tears!
Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
6 You have allowed the people-groups that surround us to fight with [each other to decide which part of our land each of them will take]; our enemies laugh at us.
Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
7 God, commander of the armies of heaven, cause our nation to be strong like it was before! Be kind to us in order that we may be saved!
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
8 [Our ancestors were like] a grapevine [MET] that you brought out of Egypt; you expelled the other people-groups [from this land], and you put your people in their land.
Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
9 [Like people] clear ground to plant a grapevine [MET], [you cleared out the people who were living in this land for us to live in it]. [Like] the roots of a grapevine go deep down into the ground and spread [MET], [you enabled our ancestors to prosper and start living in towns all over this land].
Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
10 [Like huge] grapevines cover the hills with their shade and their branches are taller than big cedar [trees] [MET, HYP],
Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
11 [your people ruled all of Canaan], from the [Mediterranean] Sea [in the west] to the [Euphrates] River [in the east].
Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
12 So why have you abandoned us and [allowed our enemies to] tear down our walls [RHQ]? [You are like] someone who tears down the fences [around his vineyard], with the result that all [the people] who pass by [can] steal the grapes,
Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
13 and wild pigs [can] trample [the vines], and wild animals [can also] eat [the grapes].
Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
14 You who are the commander of the armies of heaven, (turn to/stop abandoning) us! Look down from heaven and see [what is happening to] us! Come and rescue [us who are like] [MET] your grapevine,
Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
15 who are [like] the young vine that you [SYN] planted and caused to grow!
muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
16 Our enemies have torn down and burned everything in our land; look at them angrily and get rid of them!
Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
17 But strengthen [us] people whom you have chosen [IDM], [us] Israeli people whom you [previously] caused to be very strong.
Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
18 When you do that, we will never turn away from you again; (revive us/cause us to be again like we were previously), and [then] we will praise/worship you.
Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
19 Yahweh, commander of the armies of heaven, restore us; be kind to us in order that we may be rescued [from our enemies]!
Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.

< Psalms 80 >