< Psalms 59 >

1 God, save me from my enemies! Protect me from those who want to attack me!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe. Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu; munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
2 Rescue me from men who want to do what is wicked, men who are murderers!
Landitseni kwa anthu ochita zoyipa ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.
3 Look! They are waiting to kill me! Fierce men have gathered to assault me. Yahweh, they are doing that even though I have not done what is wrong!
Onani momwe iwo akundibisalira! Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane; osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
4 It is not because I have committed any sin [against them] that they run and get ready to attack me.
Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo. Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
5 Yahweh my God, commander of the armies of heaven, the one we Israelis [worship], arise and punish the [ungodly/heathen people of] all the nations; do not be merciful to those [wicked people] who have (acted treacherously toward/secretly planned to harm) us.
Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse; musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.
6 They return each evening, snarling like vicious dogs [SIM] as they prowl around this city.
Iwo amabweranso madzulo akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
7 They loudly say terrible things; they say [MTY] many things that [injure people like] [MET] swords do, but they think, “No one will [RHQ] hear us!”
Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo; iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo, ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
8 But Yahweh, you laugh at them. You (scoff at/ridicule) the [people of the pagan] nations.
Koma Inu Yehova, mumawaseka, mumayinyoza mitundu yonseyo.
9 God, I have confidence in you because you are very strong; you are my refuge.
Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa.
10 Because you love me, you will come to save me; you will allow me to watch while you defeat my enemies.
Mulungu wanga wachikondi. Mulungu adzapita patsogolo panga ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
11 But do not kill them [immediately] in order that my people will not forget [how you punished them]! [Instead], Lord, [you who are like a] shield [that protects us] [MET], scatter them by your power, and [then] defeat them.
Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu, kuopa kuti anthu anga angayiwale. Mwa mphamvu zanu, lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
12 Because what they say [MTY] is sinful, allow them to be trapped for being proud. Because they are [always] cursing and telling lies,
Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo chifukwa cha mawu a milomo yawo, iwo akodwe mʼkunyada kwawo. Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
13 because you are angry, get rid of them; destroy them completely in order that people will know that you rule over us, your Israeli people, and that you rule over all the earth.
muwawononge mu ukali (wanu) muwawononge mpaka atheretu. Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi kuti Mulungu amalamulira Yakobo.
14 My enemies return each evening, snarling like [vicious] dogs as they prowl around this city.
Iwo amabweranso madzulo, akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyenda mu mzinda.
15 They roam around, searching for food; and if they do not find enough, they growl.
Iwo amayendayenda kufuna chakudya ndipo amawuwa ngati sanakhute.
16 But [as for me], I will sing about your power; [every] morning I will sing joyfully about your faithfully loving [us]. I will sing about how you protected me when I was [very] distressed.
Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu, mmawa ndidzayimba zachikondi chanu; pakuti ndinu linga langa, pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.
17 God, you are the one who enables me to be strong; you are my refuge; you faithfully love me.
Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.

< Psalms 59 >